Add parallel Print Page Options

Za Munda Wamphesa wa Yehova

27 Tsiku limenelo,

Yehova ndi lupanga lake
    lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu,
adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija,
    Leviyatani chinjoka chodzikulunga;
adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.

Tsiku limenelo Yehova adzati,

“Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
    Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira;
    ndimawuthirira nthawi zonse.
Ndimawulondera usana ndi usiku
    kuti wina angawononge.
    Ine sindinakwiye.
Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo!
    Ndikachita nazo nkhondo;
    ndikanazitentha zonse ndi moto.
Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze;
    apangane nane za mtendere,
    ndithu, apangane nane za mtendere.”

Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu,
    Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa,
    ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.

Kodi Yehova anakantha Israeli
    ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli?
Kapena kodi Yehova anapha Israeli
    ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo,
    mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa,
    monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo.
    Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja,
ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza
    mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha.
Sipadzapezekanso mafano a Asera
    kapena maguwa ofukiza lubani.
10 Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja,
    wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu;
kumeneko amadyetselako ana angʼombe
    kumeneko zimapumulako ziweto
    ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
11 Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka
    ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni.
Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru;
    kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni,
    ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.

12 Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto. 13 Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.

The Redemption of Israel

27 In that day the Lord with his hard and great and strong (A)sword will punish (B)Leviathan the fleeing serpent, (C)Leviathan the twisting serpent, and he will slay (D)the dragon that is in the sea.

In that day,
(E)“A pleasant vineyard,[a] (F)sing of it!
    I, the Lord, am its keeper;
    every moment I water it.
    Lest anyone punish it,
I keep it night and day;
    I have no wrath.
(G)Would that I had thorns and briers to battle!
    I would march against them,
    I would burn them up together.
Or let them lay hold of my protection,
    let them make peace with me,
    let them make peace with me.”

(H)In days to come[b] Jacob shall take root,
    Israel shall blossom and put forth shoots
    and fill the whole world with fruit.

(I)Has he struck them (J)as he struck those who struck them?
    Or have they been slain (K)as their slayers were slain?
(L)Measure by measure,[c] by exile you contended with them;
    (M)he removed them with his fierce breath[d] in the day of the east wind.
Therefore by this (N)the guilt of Jacob will be atoned for,
    and this will be the full fruit of the removal of his sin:[e]
(O)when he makes all the stones of the altars
    like chalkstones crushed to pieces,
    no (P)Asherim or incense altars will remain standing.
10 (Q)For the fortified city is solitary,
    a habitation deserted and forsaken, like the wilderness;
there the calf grazes;
    there it lies down and strips its branches.
11 When its boughs are dry, they are broken;
    women come and make a fire of them.
(R)For this is a people without discernment;
    therefore he who made them will not have compassion on them;
    he who formed them will show them no favor.

12 In that day (S)from the river Euphrates[f] to the Brook of Egypt the Lord will thresh out the grain, and you will be gleaned one by one, O people of Israel. 13 And in that day (T)a great trumpet will be blown, (U)and those who were lost in the land of Assyria and those who were driven out to the land of Egypt (V)will come and worship the Lord on the holy mountain at Jerusalem.

Footnotes

  1. Isaiah 27:2 Many Hebrew manuscripts A vineyard of wine
  2. Isaiah 27:6 Hebrew In those to come
  3. Isaiah 27:8 Or By driving her away; the meaning of the Hebrew word is uncertain
  4. Isaiah 27:8 Or wind
  5. Isaiah 27:9 Septuagint and this is the blessing when I take away his sin
  6. Isaiah 27:12 Hebrew from the River