Yesaya 2:2-4
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
2 Mʼmasiku otsiriza,
phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa
kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse,
lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,
ndipo mayiko onse adzathamangira kumeneko.
3 Anthu ambiri adzabwera ndikunena kuti,
“Tiyeni tikwere ku phiri la Yehova,
ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.
Iye adzatiphunzitsa njira zake,
ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”
Malangizo adzachokera ku Ziyoni,
mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
4 Iye adzaweruza pakati pa mayiko,
ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu ambiri.
Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu
ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.
Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,
kapena kuphunziranso za nkhondo.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.