Hoseya 14
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kulapa Kubweretsa Madalitso
14 Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako.
Machimo anu ndi amene akugwetsani!
2 Bweretsani zopempha zanu
ndipo bwererani kwa Yehova.
Munene kwa Iye kuti,
“Tikhululukireni machimo athu onse
ndi kutilandira mokoma mtima,
kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
3 Asiriya sangatipulumutse;
ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo,
sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’
kwa zimene manja athu omwe anazipanga,
pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
4 Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo
ndipo ndidzawakonda mwaufulu
pakuti ndaleka kuwakwiyira.
5 Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli
Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo.
Adzazika mizu yake pansi
ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
6 mphukira zake zidzakula.
Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi,
kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
7 Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake.
Iye adzakula bwino ngati tirigu.
Adzachita maluwa ngati mphesa
ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
8 Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano?
Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira.
Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira;
zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
9 Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi.
Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi.
Njira za Yehova ndi zolungama;
anthu olungama amayenda mʼmenemo,
koma anthu owukira amapunthwamo.
Hosea 14
New International Version
Repentance to Bring Blessing
14 [a]Return,(A) Israel, to the Lord your God.
Your sins(B) have been your downfall!(C)
2 Take words with you
and return to the Lord.
Say to him:
“Forgive(D) all our sins
and receive us graciously,(E)
that we may offer the fruit of our lips.[b](F)
3 Assyria cannot save us;(G)
we will not mount warhorses.(H)
We will never again say ‘Our gods’(I)
to what our own hands have made,(J)
for in you the fatherless(K) find compassion.”
4 “I will heal(L) their waywardness(M)
and love them freely,(N)
for my anger has turned away(O) from them.
5 I will be like the dew(P) to Israel;
he will blossom like a lily.(Q)
Like a cedar of Lebanon(R)
he will send down his roots;(S)
6 his young shoots will grow.
His splendor will be like an olive tree,(T)
his fragrance like a cedar of Lebanon.(U)
7 People will dwell again in his shade;(V)
they will flourish like the grain,
they will blossom(W) like the vine—
Israel’s fame will be like the wine(X) of Lebanon.(Y)
8 Ephraim, what more have I[c] to do with idols?(Z)
I will answer him and care for him.
I am like a flourishing juniper;(AA)
your fruitfulness comes from me.”
Footnotes
- Hosea 14:1 In Hebrew texts 14:1-9 is numbered 14:2-10.
- Hosea 14:2 Or offer our lips as sacrifices of bulls
- Hosea 14:8 Or Hebrew; Septuagint What more has Ephraim
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.