Add parallel Print Page Options

Za Kumanga Nyumba ya Yehova

Chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo, tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chimodzi, Yehova anapatsa mneneri Hagai uthenga wopita kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, ndiponso kwa mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki:

Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu awa amanena kuti, ‘Nthawi sinafike yoti nʼkumanga Nyumba ya Yehova.’ ”

Tsono Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti, “Kodi ino ndi nthawi yoti inuyo muzikhala mʼnyumba zomanga bwino, pamene Nyumba yangayi ikanali bwinja?”

Tsono zimene Yehova Wamphamvuzonse akunena ndi izi, “Ganizirani bwino njira zanu. Mwadzala zambiri, koma mwakolola zochepa. Mumadya, koma simukhuta. Mumamwa, koma ludzu lanu silitha. Mumavala, koma simumva kutentha. Mumalandira malipiro, koma ndalama zanu zimatha ngati mwaziyika mʼthumba lobowoka.”

Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ganizirani bwino njira zanu. Pitani ku mapiri ndipo mukatenge matabwa oti mudzamangire Nyumba yanga, kuti ndikondwere nayo ndi kulandiramo ulemu,” akutero Yehova. “Mumayembekezera zambiri, koma taonani mwapeza pangʼono pokha. Zimene munazibweretsa ku nyumba, Ine ndinazimwaza. Nʼchifukwa chiyani?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Chifukwa Nyumba yanga ikanali bwinja, pamene aliyense wa inu watanganidwa kumanga nyumba yake. 10 Choncho, chifukwa cha inu, mitambo yaleka kugwetsa mvula ndipo dziko lapansi laleka kutulutsa zomera. 11 Ndabweretsa chilala pa minda ndi pa mapiri, chilala chawumitsa tirigu, mphesa, mafuta a olivi ndi chilichonse chimene chimamera pa nthaka, pa anthu ndi pa ngʼombe, ndi pa ntchito zonse za manja anu.”

12 Pamenepo Zerubabeli mwana wa Sealatieli, mkulu wa ansembe Yoswa mwana wa Yehozadaki, ndi anthu onse otsala anamvera mawu a Yehova Mulungu wawo ndi uthenga wa Hagai, chifukwa anatumidwa ndi Yehova Mulungu wawo. Ndipo anthuwo anaopa Yehova.

13 Tsono Hagai, mthenga wa Yehova, anapereka kwa anthuwo uthenga uwu wa Yehova: “Ine ndili nanu,” akutero Yehova. 14 Kotero Yehova anakhudza mtima wa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, mtima wa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndiponso mitima ya anthu onse otsala. Iwo anabwera ndi kuyamba ntchito yomanga Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wawo, 15 pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chimodzi, wa chaka chachiwiri cha Mfumu Dariyo.

A Call to Build the House of the Lord

In the second year of King Darius,(A) on the first day of the sixth month, the word of the Lord came through the prophet Haggai(B) to Zerubbabel(C) son of Shealtiel, governor(D) of Judah, and to Joshua(E) son of Jozadak,[a](F) the high priest:(G)

This is what the Lord Almighty(H) says: “These people(I) say, ‘The time has not yet come to rebuild the Lord’s house.(J)’”

Then the word of the Lord came through the prophet Haggai:(K) “Is it a time for you yourselves to be living in your paneled houses,(L) while this house remains a ruin?(M)

Now this is what the Lord Almighty says: “Give careful thought(N) to your ways. You have planted much, but harvested little.(O) You eat, but never have enough.(P) You drink, but never have your fill.(Q) You put on clothes, but are not warm. You earn wages,(R) only to put them in a purse with holes in it.”

This is what the Lord Almighty says: “Give careful thought(S) to your ways. Go up into the mountains and bring down timber(T) and build my house, so that I may take pleasure(U) in it and be honored,(V)” says the Lord. “You expected much, but see, it turned out to be little.(W) What you brought home, I blew(X) away. Why?” declares the Lord Almighty. “Because of my house, which remains a ruin,(Y) while each of you is busy with your own house. 10 Therefore, because of you the heavens have withheld(Z) their dew(AA) and the earth its crops.(AB) 11 I called for a drought(AC) on the fields and the mountains,(AD) on the grain, the new wine,(AE) the olive oil(AF) and everything else the ground produces, on people and livestock, and on all the labor of your hands.(AG)

12 Then Zerubbabel(AH) son of Shealtiel, Joshua son of Jozadak, the high priest, and the whole remnant(AI) of the people obeyed(AJ) the voice of the Lord their God and the message of the prophet Haggai, because the Lord their God had sent him. And the people feared(AK) the Lord.

13 Then Haggai,(AL) the Lord’s messenger,(AM) gave this message of the Lord to the people: “I am with(AN) you,” declares the Lord. 14 So the Lord stirred up(AO) the spirit of Zerubbabel(AP) son of Shealtiel, governor of Judah, and the spirit of Joshua son of Jozadak,(AQ) the high priest, and the spirit of the whole remnant(AR) of the people. They came and began to work on the house of the Lord Almighty, their God, 15 on the twenty-fourth day of the sixth month.(AS)

The Promised Glory of the New House

In the second year of King Darius,(AT)

Footnotes

  1. Haggai 1:1 Hebrew Jehozadak, a variant of Jozadak; also in verses 12 and 14