Genesis 47
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
47 Yosefe anapita kukamuwuza Farao kuti, “Abambo anga, abale anga pamodzi ndi nkhosa, ngʼombe zawo, ndi antchito awo abwera kuchokera ku dziko la Kanaani ndipo tsopano ali ku Goseni.” 2 Iye anapita kwa Farao kuja ndi abale ake asanu, kukawaonetsa.
3 Farao anafunsa abale akewo kuti, “Mumagwira ntchito yanji?”
Iwo anamuyankha kuti, “Ife, bwana ndife oweta ziweto, monga ankachitira makolo athu. 4 Ife tabwera kudzakhala kuno kwa kanthawi chifukwa njala yafika poopsa ku Kanaani motero kuti kulibe msipu wodyetsera ziweto. Ndiye bwana tiloleni kuti tikhale ku Goseni.”
5 Farao anati kwa Yosefe, “Abambo ako ndi abale ako abwera kwa iwe. 6 Dziko lonse la Igupto lili mʼdzanja lako. Uwakhazike abambo ako ndi abale ako mʼmalo achonde kwambiri. Akhale ku Goseni. Ndipo ngati ukudziwapo ena mwa iwo amene ali akatswiri pa kuweta ziweto, uwapatse udindo woyangʼanira ziweto zanga.”
7 Kenaka Yosefe anapita ndi abambo ake kwa Farao kukawaonetsa, ndipo Yakobo anadalitsa Faraoyo. 8 Atatero, Farao anafunsa Yakobo kuti, “Muli ndi zaka zingati?”
9 Yakobo anayankha kuti, “Zaka za maulendo anga zakwana 130. Zaka za moyo wanga ndi zowerengeka, komanso zakhala zaka za masautso. Zaka za moyo wanga sizingafanane ndi zaka za moyo wa makolo anga.” 10 Atatha kumudalitsa Farao uja, Yakobo anatsanzika nʼkunyamuka.
11 Choncho Yosefe anakhazika abambo ake aja ndi abale ake mʼdziko la Igupto. Iye anawapatsa dera la Ramesesi limene linali dziko lachonde kwambiri monga analamulira Farao. 12 Yosefe anaperekanso chakudya kwa abambo ake, kwa abale ake ndi kwa onse a mʼnyumba ya abambo ake monga mwa chiwerengero cha ana awo.
Yosefe pa Nthawi ya Njala
13 Njala inakula kwambiri motero kuti chakudya chinasowa mʼdziko lonse. Anthu a ku Igupto ndi ku Kanaani analefuka nayo njalayo. 14 Yosefe anasonkhanitsa ndalama zonse zimene anthu a mu Igupto ndi Kanaani ankapereka pogula tirigu, ndipo anabwera nazo ku nyumba kwa Farao. 15 Anthu a ku Igupto ndi Kanaani ndalama zitawathera, Aigupto onse anabwera kwa Yosefe nati, “Tipatseni chakudya. Nanga tiferenji pamaso panu? Ndalama zathu zatha.”
16 Ndipo Yosefe anawayankha kuti, “Bwerani ndi ziweto zanu ndipo tidzasinthana ndi chakudya poti mukuti ndalama zanu zatha.” 17 Choncho anthu anabwera ndi ziweto zawo monga akavalo, nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi abulu ndipo Yosefe anawapatsa zakudya.
18 Chitatha chaka chimenecho, anthu anapitanso kwa Yosefe chaka chinacho nati, “Ife sitingakubisireni mbuye wathu kuti ndalama zathu zatithera ndipo ziweto zathu zili ndi inu, palibenso choti nʼkukupatsani mbuye wathu kupatula matupi athu ndi dziko lathu. 19 Tiferenji ife ndi dziko lathu inu mukuona? Mutipatse chakudya ndipo tidzigulitsa ife ndi minda yathu yomwe. Ife tidzakhala akapolo a Farao. Tipatseni mbewuzo kuti tikhale ndi moyo tisafe ndipo dziko lisachite bwinja.”
20 Choncho Yosefe anamugulira Farao dziko lonse la Igupto. Aliyense mu Igupto anagulitsa munda wake chifukwa njala inakula kwambiri. Dziko lonse linasanduka la Farao, 21 ndipo Yosefe anawasandutsa anthu onse kukhala akapolo a Farao, kuchokera ku malire a mbali ina ya Igupto kukafika ku malire a mbali ina ya dzikolo. 22 Komabe, sanagule minda ya ansembe chifukwa Farao ankawapatsa thandizo lokwanira. Nʼchifukwa chake sanagulitse minda yawo.
23 Yosefe anati kwa anthuwo, “Tsono poti ndakugulani inu ndi minda yanu, kugulira Farao. Nayi mbewu kuti mudzale mʼminda yanu. 24 Koma podzakolola, mudzapereka gawo limodzi la magawo asanu aliwonse kwa Farao. Magawo anayi enawo adzakhala anu. Zina mudzasunge mbewu ndi zina mudzadye inuyo, mabanja anu ndi ana anu.”
25 Iwo anati, “Mwatipulumutsa potichitira zabwinozi, mbuye wathu, tsono tidzakhala akapolo a Farao.”
26 Choncho Yosefe anakhazikitsa lamulo limene lilipobe mpaka lero mʼdziko lonse la Igupto kuti limodzi la magawo asanu a zokolola ndi la Farao. Ndi minda ya ansembe yokha imene sinatengedwe kukhala ya Farao.
27 Tsono Aisraeli anakhazikika mʼdziko la Igupto ku chigawo cha Goseni. Kumeneko anapeza chuma ndipo anaberekana nachuluka kwambiri.
28 Yakobo anakhala ku Igupto zaka 17 ndipo zaka za moyo wake zinali 147. 29 Nthawi itayandikira yoti Israeli amwalire, anayitanitsa mwana wake Yosefe nati kwa iye, “Ngati ukundikondadi monga abambo ako, ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga ndipo ulonjeze kuti udzaonetsa kukoma mtima ndi kukhulupirika kwako kwa ine kuti sudzayika mtembo wanga kuno ku Igupto. 30 Ine ndikagona pamodzi ndi makolo anga. Choncho ndikadzamwalira udzanditulutse mu Igupto muno ndipo ukayike mtembo wanga kumene anayikidwa makolo anga.”
Yosefe anati, “Ndidzachita monga mwanenera.”
31 Yakobo anati, “Lumbira kwa ine.” Yosefe analumbira kwa iye, ndipo Israeli anapembedza Mulungu atatsamira ndodo yake.
Genesis 47
New International Version
47 Joseph went and told Pharaoh, “My father and brothers, with their flocks and herds and everything they own, have come from the land of Canaan(A) and are now in Goshen.”(B) 2 He chose five of his brothers and presented them(C) before Pharaoh.
3 Pharaoh asked the brothers, “What is your occupation?”(D)
“Your servants(E) are shepherds,(F)” they replied to Pharaoh, “just as our fathers were.” 4 They also said to him, “We have come to live here for a while,(G) because the famine is severe in Canaan(H) and your servants’ flocks have no pasture.(I) So now, please let your servants settle in Goshen.”(J)
5 Pharaoh said to Joseph, “Your father and your brothers have come to you, 6 and the land of Egypt is before you; settle(K) your father and your brothers in the best part of the land.(L) Let them live in Goshen. And if you know of any among them with special ability,(M) put them in charge of my own livestock.(N)”
7 Then Joseph brought his father Jacob in and presented him(O) before Pharaoh. After Jacob blessed[a] Pharaoh,(P) 8 Pharaoh asked him, “How old are you?”
9 And Jacob said to Pharaoh, “The years of my pilgrimage are a hundred and thirty.(Q) My years have been few and difficult,(R) and they do not equal the years of the pilgrimage of my fathers.(S)” 10 Then Jacob blessed[b] Pharaoh(T) and went out from his presence.
11 So Joseph settled his father and his brothers in Egypt and gave them property in the best part of the land,(U) the district of Rameses,(V) as Pharaoh directed. 12 Joseph also provided his father and his brothers and all his father’s household with food, according to the number of their children.(W)
Joseph and the Famine
13 There was no food, however, in the whole region because the famine was severe; both Egypt and Canaan wasted away because of the famine.(X) 14 Joseph collected all the money that was to be found in Egypt and Canaan in payment for the grain they were buying,(Y) and he brought it to Pharaoh’s palace.(Z) 15 When the money of the people of Egypt and Canaan was gone,(AA) all Egypt came to Joseph(AB) and said, “Give us food. Why should we die before your eyes?(AC) Our money is all gone.”
16 “Then bring your livestock,(AD)” said Joseph. “I will sell you food in exchange for your livestock, since your money is gone.(AE)” 17 So they brought their livestock to Joseph, and he gave them food in exchange for their horses,(AF) their sheep and goats, their cattle and donkeys.(AG) And he brought them through that year with food in exchange for all their livestock.
18 When that year was over, they came to him the following year and said, “We cannot hide from our lord the fact that since our money is gone(AH) and our livestock belongs to you,(AI) there is nothing left for our lord except our bodies and our land. 19 Why should we perish before your eyes(AJ)—we and our land as well? Buy us and our land in exchange for food,(AK) and we with our land will be in bondage to Pharaoh.(AL) Give us seed so that we may live and not die,(AM) and that the land may not become desolate.”
20 So Joseph bought all the land in Egypt for Pharaoh. The Egyptians, one and all, sold their fields, because the famine was too severe(AN) for them. The land became Pharaoh’s, 21 and Joseph reduced the people to servitude,[c](AO) from one end of Egypt to the other. 22 However, he did not buy the land of the priests,(AP) because they received a regular allotment from Pharaoh and had food enough from the allotment(AQ) Pharaoh gave them. That is why they did not sell their land.
23 Joseph said to the people, “Now that I have bought you and your land today for Pharaoh, here is seed(AR) for you so you can plant the ground.(AS) 24 But when the crop comes in, give a fifth(AT) of it to Pharaoh. The other four-fifths you may keep as seed for the fields and as food for yourselves and your households and your children.”
25 “You have saved our lives,” they said. “May we find favor in the eyes of our lord;(AU) we will be in bondage to Pharaoh.”(AV)
26 So Joseph established it as a law concerning land in Egypt—still in force today—that a fifth(AW) of the produce belongs to Pharaoh. It was only the land of the priests that did not become Pharaoh’s.(AX)
27 Now the Israelites settled in Egypt in the region of Goshen.(AY) They acquired property there(AZ) and were fruitful and increased greatly in number.(BA)
28 Jacob lived in Egypt(BB) seventeen years, and the years of his life were a hundred and forty-seven.(BC) 29 When the time drew near for Israel(BD) to die,(BE) he called for his son Joseph and said to him, “If I have found favor in your eyes,(BF) put your hand under my thigh(BG) and promise that you will show me kindness(BH) and faithfulness.(BI) Do not bury me in Egypt, 30 but when I rest with my fathers,(BJ) carry me out of Egypt and bury me where they are buried.”(BK)
“I will do as you say,” he said.
31 “Swear to me,”(BL) he said. Then Joseph swore to him,(BM) and Israel(BN) worshiped as he leaned on the top of his staff.[d](BO)
Footnotes
- Genesis 47:7 Or greeted
- Genesis 47:10 Or said farewell to
- Genesis 47:21 Samaritan Pentateuch and Septuagint (see also Vulgate); Masoretic Text and he moved the people into the cities
- Genesis 47:31 Or Israel bowed down at the head of his bed
Genesis 47
King James Version
47 Then Joseph came and told Pharaoh, and said, My father and my brethren, and their flocks, and their herds, and all that they have, are come out of the land of Canaan; and, behold, they are in the land of Goshen.
2 And he took some of his brethren, even five men, and presented them unto Pharaoh.
3 And Pharaoh said unto his brethren, What is your occupation? And they said unto Pharaoh, Thy servants are shepherds, both we, and also our fathers.
4 They said morever unto Pharaoh, For to sojourn in the land are we come; for thy servants have no pasture for their flocks; for the famine is sore in the land of Canaan: now therefore, we pray thee, let thy servants dwell in the land of Goshen.
5 And Pharaoh spake unto Joseph, saying, Thy father and thy brethren are come unto thee:
6 The land of Egypt is before thee; in the best of the land make thy father and brethren to dwell; in the land of Goshen let them dwell: and if thou knowest any men of activity among them, then make them rulers over my cattle.
7 And Joseph brought in Jacob his father, and set him before Pharaoh: and Jacob blessed Pharaoh.
8 And Pharaoh said unto Jacob, How old art thou?
9 And Jacob said unto Pharaoh, The days of the years of my pilgrimage are an hundred and thirty years: few and evil have the days of the years of my life been, and have not attained unto the days of the years of the life of my fathers in the days of their pilgrimage.
10 And Jacob blessed Pharaoh, and went out from before Pharaoh.
11 And Joseph placed his father and his brethren, and gave them a possession in the land of Egypt, in the best of the land, in the land of Rameses, as Pharaoh had commanded.
12 And Joseph nourished his father, and his brethren, and all his father's household, with bread, according to their families.
13 And there was no bread in all the land; for the famine was very sore, so that the land of Egypt and all the land of Canaan fainted by reason of the famine.
14 And Joseph gathered up all the money that was found in the land of Egypt, and in the land of Canaan, for the corn which they bought: and Joseph brought the money into Pharaoh's house.
15 And when money failed in the land of Egypt, and in the land of Canaan, all the Egyptians came unto Joseph, and said, Give us bread: for why should we die in thy presence? for the money faileth.
16 And Joseph said, Give your cattle; and I will give you for your cattle, if money fail.
17 And they brought their cattle unto Joseph: and Joseph gave them bread in exchange for horses, and for the flocks, and for the cattle of the herds, and for the asses: and he fed them with bread for all their cattle for that year.
18 When that year was ended, they came unto him the second year, and said unto him, We will not hide it from my lord, how that our money is spent; my lord also hath our herds of cattle; there is not ought left in the sight of my lord, but our bodies, and our lands:
19 Wherefore shall we die before thine eyes, both we and our land? buy us and our land for bread, and we and our land will be servants unto Pharaoh: and give us seed, that we may live, and not die, that the land be not desolate.
20 And Joseph bought all the land of Egypt for Pharaoh; for the Egyptians sold every man his field, because the famine prevailed over them: so the land became Pharaoh's.
21 And as for the people, he removed them to cities from one end of the borders of Egypt even to the other end thereof.
22 Only the land of the priests bought he not; for the priests had a portion assigned them of Pharaoh, and did eat their portion which Pharaoh gave them: wherefore they sold not their lands.
23 Then Joseph said unto the people, Behold, I have bought you this day and your land for Pharaoh: lo, here is seed for you, and ye shall sow the land.
24 And it shall come to pass in the increase, that ye shall give the fifth part unto Pharaoh, and four parts shall be your own, for seed of the field, and for your food, and for them of your households, and for food for your little ones.
25 And they said, Thou hast saved our lives: let us find grace in the sight of my lord, and we will be Pharaoh's servants.
26 And Joseph made it a law over the land of Egypt unto this day, that Pharaoh should have the fifth part, except the land of the priests only, which became not Pharaoh's.
27 And Israel dwelt in the land of Egypt, in the country of Goshen; and they had possessions therein, and grew, and multiplied exceedingly.
28 And Jacob lived in the land of Egypt seventeen years: so the whole age of Jacob was an hundred forty and seven years.
29 And the time drew nigh that Israel must die: and he called his son Joseph, and said unto him, If now I have found grace in thy sight, put, I pray thee, thy hand under my thigh, and deal kindly and truly with me; bury me not, I pray thee, in Egypt:
30 But I will lie with my fathers, and thou shalt carry me out of Egypt, and bury me in their buryingplace. And he said, I will do as thou hast said.
31 And he said, Swear unto me. And he sware unto him. And Israel bowed himself upon the bed's head.
La Bibbia della Gioia Copyright © 1997, 2006 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.
