Add parallel Print Page Options

Abramu Asiyana ndi Loti

13 Choncho Abramu pamodzi ndi mkazi wake ndi zonse anali nazo, anachoka ku Igupto kupita ku Negevi. Loti naye anapita nawo. Abramu anali wolemera kwambiri; anali ndi ziweto ndiponso siliva ndi golide.

Atachoka ku Negevi, anayenda malo osiyanasiyana mpaka anafika ku Beteli, ku malo a pakati pa Beteli ndi Ai, kuja kumene anamanga tenti poyamba, ndiponso kumene Abramu anamangira Yehova guwa lansembe kwa nthawi yoyamba ndi kupemphera mʼdzina la Yehova.

Loti amene ankayendayenda ndi Abramu nayenso anali ndi ziweto zosiyanasiyana ndi matenti. Motero dziko linayamba kuwachepera kuti onse nʼkukhala pamodzi, popeza katundu wawo anali wochuluka kwambiri moti sakanatha kukhala pamodzi. Mikangano inayambika pakati pa abusa a Abramu ndi abusa a Loti. Nthawi imeneyo nʼkuti Akanaani ndi Aperezi akukhalanso mʼdziko lomwelo.

Tsono Abramu anati kwa Loti, “Pasakhale mikangano pakati pa iwe ndi ine kapena pakati pa abusa ako ndi anga, popeza ndife abale. Kodi dziko lonseli silili pamaso pako? Tiye tisiyane. Iwe ukalowera kumanzere, ine ndilowera kumanja; ukalowera kumanja, ine ndipita kumanzere.”

10 Loti atamwazamwaza maso anaona kuti chigwa chonse cha mtsinje wa Yorodani chinali chothiriridwa bwino ngati munda wa Yehova, kapena ngati dziko la ku Igupto mpaka ku Zowari. (Nthawi iyi nʼkuti Yehova asanawononge Sodomu ndi Gomora). 11 Choncho Loti anadzisankhira yekha chigwa chonse cha Yorodani nanyamuka kulowera cha kummawa. Choncho anthu awiriwa anasiyana. 12 Abramu anakhala mʼdziko la Kanaani, pamene Loti anakakhala pakati pa mizinda ikuluikulu ya mʼchigwamo. Anamanga tenti yake pafupi ndi Sodomu. 13 Tsono anthu a ku Sodomu anali oyipa ndiponso ankachimwira Yehova kwambiri.

14 Loti atachoka, Yehova anati kwa Abramu, “Kuchokera pamene ulipo tayangʼanayangʼana cha kumpoto, kummwera, kummawa ndi kumadzulo. 15 Dziko lonse ukulionalo ndidzalipereka kwa iwe ndi zidzukulu zako mpaka muyaya. 16 Ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati fumbi lapansi moti amene angathe kuwerenga fumbilo ndiye kuti angathenso kuwerenga zidzukulu zako. 17 Dzuka ndipo uyendere dziko lonseli mulitali ndi mulifupi pakuti ndalipereka kwa iwe.”

18 Choncho Abramu anasamutsa tenti yake napita kukakhala pafupi ndi mitengo ikuluikulu ija ya thundu ya ku Mamre ku Hebroni, kumene anamangira Yehova guwa lansembe.

Abram and Lot Separate

13 So Abram went up from Egypt(A) to the Negev,(B) with his wife and everything he had, and Lot(C) went with him. Abram had become very wealthy(D) in livestock(E) and in silver and gold.

From the Negev(F) he went from place to place until he came to Bethel,(G) to the place between Bethel and Ai(H) where his tent had been earlier and where he had first built an altar.(I) There Abram called on the name of the Lord.(J)

Now Lot,(K) who was moving about with Abram, also had flocks and herds and tents. But the land could not support them while they stayed together, for their possessions were so great that they were not able to stay together.(L) And quarreling(M) arose between Abram’s herders and Lot’s. The Canaanites(N) and Perizzites(O) were also living in the land(P) at that time.

So Abram said to Lot,(Q) “Let’s not have any quarreling between you and me,(R) or between your herders and mine, for we are close relatives.(S) Is not the whole land before you? Let’s part company. If you go to the left, I’ll go to the right; if you go to the right, I’ll go to the left.”(T)

10 Lot looked around and saw that the whole plain(U) of the Jordan toward Zoar(V) was well watered, like the garden of the Lord,(W) like the land of Egypt.(X) (This was before the Lord destroyed Sodom(Y) and Gomorrah.)(Z) 11 So Lot chose for himself the whole plain of the Jordan and set out toward the east. The two men parted company: 12 Abram lived in the land of Canaan,(AA) while Lot(AB) lived among the cities of the plain(AC) and pitched his tents near Sodom.(AD) 13 Now the people of Sodom(AE) were wicked and were sinning greatly against the Lord.(AF)

14 The Lord said to Abram after Lot had parted from him, “Look around from where you are, to the north and south, to the east and west.(AG) 15 All the land that you see I will give to you and your offspring[a] forever.(AH) 16 I will make your offspring like the dust of the earth, so that if anyone could count the dust, then your offspring could be counted.(AI) 17 Go, walk through the length and breadth of the land,(AJ) for I am giving it to you.”(AK)

18 So Abram went to live near the great trees of Mamre(AL) at Hebron,(AM) where he pitched his tents. There he built an altar to the Lord.(AN)

Footnotes

  1. Genesis 13:15 Or seed; also in verse 16