Ezekieli 41
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
41 Ndipo munthuyo anapita nane mʼchipinda chopatulika cha Nyumba ya Mulungu ndipo anayeza khonde lake; mulifupi mwa khondelo munali mamita atatu mbali iliyonse kutalika kwake. 2 Mulifupi mwa khomo munali motalika mamita asanu. Makoma a mbali zonse anali a mamita awiri ndi theka mulifupi mwake. Anayezanso kutalika kwa chipinda chopatulika chija ndipo mulitali mwake munali motalika mamita makumi awiri ndi mulifupi mwake munali mamita khumi.
3 Kenaka munthuyo anakalowa mʼkati ndipo anayeza khonde la pa khomo; khondelo linali mita imodzi mulifupi mwake. Mulifupi mwa khondelo munali mamita atatu. 4 Ndiponso anayeza kutalika kwa chipinda chopatulika chenichenicho. Mulitali mwake munali mamita khumi, ndipo mulifupi mwake munali mamita khumi. Munthuyo anandiwuza kuti, “Ichi ndicho chipinda chopatulika kwambiri.”
5 Tsono munthuyo anayeza khoma la Nyumba ya Mulungu; kuchindikira kwake kunali mamita atatu. Panalinso zipinda zina kuzungulira Nyumba ya Mulungu ndipo chilichonse chinali cha mamita awiri mulifupi wake. 6 Zipindazo zinali zitatu zosanjikizana. Chigawo chilichonse chinali ndi zipinda makumi atatu. Pa makoma a Nyumba ya Mulungu panali zochirikiza zipindazo kuti zisatsamire khoma la Nyumba ya Mulungu. 7 Zipinda za mʼmbalizo zinkapita zikulirakulira pomakwera chipinda ndi chipinda potsata kukulirakulira kwa zochirikiza za zipinda zija. Pambali pa Nyumba ya Mulungu panali makwerero okwerera pamwamba, kuchokera chigawo chapansi kudzera chapakati, mpaka kukafika pamwamba.
8 Ndinaona chiwundo kuzungulira Nyumba ya Mulungu. Chinapanga maziko a zipindazo ndipo chinali cha mamita atatu. 9 Khoma lakunja la zipindazo linali la mamita awiri ndi theka kuchindikira kwake. Pakati pa chiwundocho 10 ndi zipinda za Nyumba ya Mulungu panali bwalo limeneli la mamita khumi kupingasa kwake kuzungulira Nyumba yonse ya Mulungu. 11 Zitseko za zipinda zamʼmbalizo zinali zotsekulira ku chiwundo. Chitseko chimodzi chinkayangʼana kumpoto ndipo china chinkayangʼana kummwera. Chiwundo chosamangapo kanthu chinali mamita awiri ndi theka kukula kwake kuzungulira ponseponse.
12 Nyumba imene inali chakummwera moyangʼanana ndi bwalo la Nyumba ya Mulungu inali mamita 35 mulifupi mwake. Khoma la nyumbayo linali mamita awiri ndi theka kuchindikira kwake kuzungulira ponseponse, ndipo mulitali mwake linali mamita 45.
13 Ndipo munthuyo anayeza Nyumba ya Mulungu ndipo mulitali mwake inali mamita makumi asanu. Nyumbayo ndi makoma ake, zonse zinali za mamita makumi asanu. 14 Kumaso kwa Nyumba ya Mulungu chakummawa kwa bwalolo mulifupi mwake munali mamita makumi asanu.
15 Kenaka anayeza kutalika kwa nyumba yoyangʼanana ndi bwalo chakumadzulo kwa Nyumba ya Mulungu, kuphatikizapo njira zamʼkati ku mbali iliyonse. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu, chimene chili chamʼkati, khonde lamʼkati loyangʼanana ndi bwalo, 16 mazenera ndi maferemu ake, zonsezi zinali zokutidwa ndi matabwa. Pamwamba moyangʼanana ndi chiwundo, Nyumba ya Mulungu inakutidwa ndi matabwa kuyambira pansi mpaka ku mazenera, (mazenerawo anali okutidwa), 17 pamwamba pa khomo lolowera ku malo opatulika amʼkati komanso kuzungulira makoma onse kunja ndi mʼkati, 18 anajambulapo zithunzi za kerubi mmodzi atakhala pakati pa kanjedza muwiri. Kerubi aliyense anali ndi nkhope ziwiri: 19 imodzi inali nkhope ya munthu yoyangʼana kanjedza mbali imodzi, ndi ina inali nkhope ya mkango yoyangʼana kanjedza mbali ina. Zinajambulidwa kuzungulira Nyumba ya Mulungu yonse. 20 Motero kuyambira pansi mpaka pamwamba pa khomo komanso pa makoma onse a chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu, anajambula zithunzi za akerubi ndi kanjedza pa makoma onse a malo opatulika.
21 Mphuthu za chipinda chachikulu cha Nyumba ya Mulungu kutalika kwake mbali zonse kunali kofanana. Ndipo kumaso kwa malo opatulika kunali chinthu china chooneka ngati 22 guwa lansembe la matabwa. Msinkhu wake unali mita imodzi ndi theka, mulitali mwake munali mita imodzi, mulifupi mwake munalinso mita imodzi. Mphuthu zake, tsinde lake ndi mbali zonse zinali za matabwa. Munthuyo anandiwuza kuti, “Tebulo limeneli ndilo limakhala pamaso pa Yehova.” 23 Chipinda chachikulu chija chinali ndi zitseko ziwiri. Malo opatulika aja analinso ndi zitseko ziwiri. 24 Chitseko chilichonse chinali ndi zigawo ziwiri zopatukana. 25 Ndipo pa zitsekopo anajambulipo zithunzi za akerubi ndi kanjedza monga zomwe anajambulapo pa makoma. Kunja kwake kunali ngati denga lamatabwa pamwamba pa khonde lamʼkati. 26 Pa mbali zonse za khonde lamʼkatilo panali mazenera, ndipo pa makoma ake onse anajambulapo zithunzi za kanjedza.
Ezekiel 41
New International Version
41 Then the man brought me to the main hall(A) and measured the jambs; the width of the jambs was six cubits[a] on each side.[b] 2 The entrance was ten cubits[c] wide, and the projecting walls on each side of it were five cubits[d] wide. He also measured the main hall; it was forty cubits long and twenty cubits wide.[e](B)
3 Then he went into the inner sanctuary and measured the jambs of the entrance; each was two cubits[f] wide. The entrance was six cubits wide, and the projecting walls on each side of it were seven cubits[g] wide. 4 And he measured the length of the inner sanctuary; it was twenty cubits, and its width was twenty cubits across the end of the main hall.(C) He said to me, “This is the Most Holy Place.(D)”
5 Then he measured the wall of the temple; it was six cubits thick, and each side room around the temple was four cubits[h] wide. 6 The side rooms were on three levels, one above another, thirty(E) on each level. There were ledges all around the wall of the temple to serve as supports for the side rooms, so that the supports were not inserted into the wall of the temple.(F) 7 The side rooms all around the temple were wider at each successive level. The structure surrounding the temple was built in ascending stages, so that the rooms widened as one went upward. A stairway(G) went up from the lowest floor to the top floor through the middle floor.
8 I saw that the temple had a raised base all around it, forming the foundation of the side rooms. It was the length of the rod, six long cubits. 9 The outer wall of the side rooms was five cubits thick. The open area between the side rooms of the temple 10 and the priests’ rooms was twenty cubits wide all around the temple. 11 There were entrances to the side rooms from the open area, one on the north and another on the south; and the base adjoining the open area was five cubits wide all around.
12 The building facing the temple courtyard on the west side was seventy cubits[i] wide. The wall of the building was five cubits thick all around, and its length was ninety cubits.[j]
13 Then he measured the temple; it was a hundred cubits[k] long, and the temple courtyard and the building with its walls were also a hundred cubits long. 14 The width of the temple courtyard on the east, including the front of the temple, was a hundred cubits.(H)
15 Then he measured the length of the building facing the courtyard at the rear of the temple, including its galleries(I) on each side; it was a hundred cubits.
The main hall, the inner sanctuary and the portico facing the court, 16 as well as the thresholds and the narrow windows(J) and galleries around the three of them—everything beyond and including the threshold was covered with wood. The floor, the wall up to the windows, and the windows were covered.(K) 17 In the space above the outside of the entrance to the inner sanctuary and on the walls at regular intervals all around the inner and outer sanctuary 18 were carved(L) cherubim(M) and palm trees.(N) Palm trees alternated with cherubim. Each cherub had two faces:(O) 19 the face of a human being toward the palm tree on one side and the face of a lion toward the palm tree on the other. They were carved all around the whole temple.(P) 20 From the floor to the area above the entrance, cherubim and palm trees were carved on the wall of the main hall.
21 The main hall(Q) had a rectangular doorframe, and the one at the front of the Most Holy Place was similar. 22 There was a wooden altar(R) three cubits[l] high and two cubits square[m]; its corners, its base[n] and its sides were of wood. The man said to me, “This is the table(S) that is before the Lord.” 23 Both the main hall(T) and the Most Holy Place had double doors.(U) 24 Each door had two leaves—two hinged leaves(V) for each door. 25 And on the doors of the main hall were carved cherubim and palm trees like those carved on the walls, and there was a wooden overhang on the front of the portico. 26 On the sidewalls of the portico were narrow windows with palm trees carved on each side. The side rooms of the temple also had overhangs.(W)
Footnotes
- Ezekiel 41:1 That is, about 11 feet or about 3.2 meters; also in verses 3, 5 and 8
- Ezekiel 41:1 One Hebrew manuscript and Septuagint; most Hebrew manuscripts side, the width of the tent
- Ezekiel 41:2 That is, about 18 feet or about 5.3 meters
- Ezekiel 41:2 That is, about 8 3/4 feet or about 2.7 meters; also in verses 9, 11 and 12
- Ezekiel 41:2 That is, about 70 feet long and 35 feet wide or about 21 meters long and 11 meters wide
- Ezekiel 41:3 That is, about 3 1/2 feet or about 1.1 meters; also in verse 22
- Ezekiel 41:3 That is, about 12 feet or about 3.7 meters
- Ezekiel 41:5 That is, about 7 feet or about 2.1 meters
- Ezekiel 41:12 That is, about 123 feet or about 37 meters
- Ezekiel 41:12 That is, about 158 feet or about 48 meters
- Ezekiel 41:13 That is, about 175 feet or about 53 meters; also in verses 14 and 15
- Ezekiel 41:22 That is, about 5 1/4 feet or about 1.5 meters
- Ezekiel 41:22 Septuagint; Hebrew long
- Ezekiel 41:22 Septuagint; Hebrew length
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.