Ezekieli 28
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Mawu Odzudzula Mfumu ya Turo
28 Yehova anandiyankhula nati: 2 “Iwe mwana wa munthu, iwuze mfumu ya ku Turo mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,
“ ‘Iwe ndi mtima wako wodzikuza
umanena kuti, ‘Ine ndine mulungu;
ndimakhala pa mpando wa mulungu
pakati pa nyanja.’
Koma ndiwe munthu chabe osati mulungu,
ngakhale ukuganiza kuti ndiwe wanzeru ngati mulungu.
3 Taona, ndiwedi wanzeru kupambana Danieli.
Ndipo palibe chinsinsi chobisika kwa iwe.
4 Mwa nzeru zako ndi kumvetsa kwako
unadzipezera chuma
ndipo unasonkhanitsa golide ndi siliva
mʼnyumba zosungira chuma chako.
5 Ndi nzeru zako zochitira malonda
unachulukitsa chuma chako
ndipo wayamba kunyada
chifukwa cha chuma chakocho.
6 “ ‘Choncho Ine Ambuye Yehova ndikuti,
“ ‘Popeza umadziganizira
kuti ndiwe mulungu,
7 Ine ndidzabwera ndi anthu achilendo, anthu ankhanza,
kuti adzalimbane nawe.
Adzakuthira nkhondo kuti awononge zonse zimene unazipeza ndi nzeru zako,
ndipo adzawononga kunyada kwakoko.
8 Iwo adzakuponyera ku dzenje
ndipo udzafa imfa yoopsa
mʼnyanja yozama.
9 Kodi udzanenabe kuti, ‘Ine ndine mulungu,’
pamaso pa iwo amene akukupha?
Iwe udzaoneka kuti ndiwe munthu chabe, osati mulungu,
mʼmanja mwa iwo amene akukuphawo.
10 Udzafa imfa ya anthu osachita mdulidwe
mʼmanja mwa anthu achilendo.
Ine ndayankhula zimenezi, akutero Ambuye Yehova.’ ”
11 Yehova anandiyankhula kuti: 12 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira mfumu ya Turo ndipo uyiwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti,
“ ‘Iwe unali chitsanzo cha ungwiro weniweni,
wodzaza ndi nzeru ndi wokongola kwambiri.
13 Iwe unkakhala ngati mu Edeni,
munda wa Mulungu.
Miyala yokongola ya mitundu yonse:
rubi, topazi ndi dayimondi,
kirisoliti, onikisi, yasipa,
safiro, kalineliyoni ndi berili ndiwo inali zofunda zako.
Ndipo zoyikamo miyalayo zinali zagolide.
Anakupangira zonsezi pa tsiku limene unalengedwa.
14 Ndinayika kerubi kuti azikulondera.
Unkakhala pa phiri langa lopatulika,
ndipo unkayendayenda
pakati pa miyala ya moto.
15 Makhalidwe ako anali abwino
kuyambira pamene unalengedwa
mpaka nthawi imene unayamba kuchita zoyipa.
16 Unatanganidwa ndi zamalonda.
Zotsatira zake zinali zoti unachulukitsa zandewu
ndi kumachimwa.
Choncho ndinakuchotsa ku phiri langa lopatulika.
Mkerubi amene ankakulondera uja anakupirikitsa
kukuchotsa ku miyala yamoto.
17 Unkadzikuza mu mtima mwako
chifukwa cha kukongola kwako,
ndipo unayipitsa nzeru zako
chifukwa chofuna kutchuka.
Kotero Ine ndinakugwetsa pansi
kuti ukhala chenjezo pamaso pa mafumu.
18 Ndi malonda ako achinyengo unachulukitsa machimo ako.
Motero unayipitsa malo ako achipembedzo.
Choncho ndinabutsa moto pakati pako,
ndipo unakupsereza,
ndipo unasanduka phulusa pa dziko lapansi
pamaso pa anthu onse amene amakuona.
19 Anthu onse amitundu amene ankakudziwa
akuchita mantha chifukwa cha iwe.
Watheratu mochititsa mantha
ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.’ ”
Za Chilango cha Sidoni
20 Yehova anandiyankhula nati: 21 “Iwe mwana wa munthu, utembenukire ku mzinda wa Sidoni ndipo unenere mowudzudzula kuti, 22 ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,
“ ‘Ndine mdani wako, iwe Sidoni,
ndipo ndidzalemekezedwa chifukwa cha iwe.
Anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova
ndikadzakulanga ndi kudzionetsa kuti
ndine woyera pakati pako.
23 Ndidzatumiza mliri pa iwe
ndi kuchititsa magazi kuti ayende mʼmisewu yako.
Anthu ophedwa ndi lupanga
adzagwa mbali zonse.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
24 “ ‘Nthawi imeneyo Aisraeli sadzakhalanso ndi anthu pafupi achipongwe amene ali ngati nthula zowawa ndi ngati minga zopweteka. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.
25 “ ‘Ine Ambuye Yehova mawu anga ndi awa: Nditasonkhanitsa Aisraeli kuchoka ku mayiko kumene anamwazikira, ndidzadzionetsa kuti ndine woyera pakati pawo pamaso pa anthu a mitundu ina. Adzakhala mʼdziko lawo, limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo. 26 Adzakhala kumeneko mwamtendere ndipo adzamanga nyumba ndi kulima minda ya mpesa. Adzakhala kumeneko mwamtendere pamene ndidzalange anthu oyandikana nawo, amene ankawanyoza. Motero iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.’ ”
Ezekiel 28
New International Version
A Prophecy Against the King of Tyre
28 The word of the Lord came to me: 2 “Son of man(A), say to the ruler of Tyre, ‘This is what the Sovereign Lord says:
“‘In the pride of your heart
you say, “I am a god;
I sit on the throne(B) of a god
in the heart of the seas.”(C)
But you are a mere mortal and not a god,
though you think you are as wise as a god.(D)
3 Are you wiser than Daniel[a]?(E)
Is no secret hidden from you?
4 By your wisdom and understanding
you have gained wealth for yourself
and amassed gold and silver
in your treasuries.(F)
5 By your great skill in trading(G)
you have increased your wealth,(H)
and because of your wealth
your heart has grown proud.(I)
6 “‘Therefore this is what the Sovereign Lord says:
“‘Because you think you are wise,
as wise as a god,
7 I am going to bring foreigners against you,
the most ruthless of nations;(J)
they will draw their swords against your beauty and wisdom(K)
and pierce your shining splendor.(L)
8 They will bring you down to the pit,(M)
and you will die a violent death(N)
in the heart of the seas.(O)
9 Will you then say, “I am a god,”
in the presence of those who kill you?
You will be but a mortal, not a god,(P)
in the hands of those who slay you.(Q)
10 You will die the death of the uncircumcised(R)
at the hands of foreigners.
I have spoken, declares the Sovereign Lord.’”
11 The word of the Lord came to me: 12 “Son of man, take up a lament(S) concerning the king of Tyre and say to him: ‘This is what the Sovereign Lord says:
“‘You were the seal of perfection,
full of wisdom and perfect in beauty.(T)
13 You were in Eden,(U)
the garden of God;(V)
every precious stone(W) adorned you:
carnelian, chrysolite and emerald,
topaz, onyx and jasper,
lapis lazuli, turquoise(X) and beryl.[b]
Your settings and mountings[c] were made of gold;
on the day you were created they were prepared.(Y)
14 You were anointed(Z) as a guardian cherub,(AA)
for so I ordained you.
You were on the holy mount of God;
you walked among the fiery stones.
15 You were blameless in your ways
from the day you were created
till wickedness was found in you.
16 Through your widespread trade
you were filled with violence,(AB)
and you sinned.
So I drove you in disgrace from the mount of God,
and I expelled you, guardian cherub,(AC)
from among the fiery stones.
17 Your heart became proud(AD)
on account of your beauty,
and you corrupted your wisdom
because of your splendor.
So I threw you to the earth;
I made a spectacle of you before kings.(AE)
18 By your many sins and dishonest trade
you have desecrated your sanctuaries.
So I made a fire(AF) come out from you,
and it consumed you,
and I reduced you to ashes(AG) on the ground
in the sight of all who were watching.(AH)
19 All the nations who knew you
are appalled(AI) at you;
you have come to a horrible end
and will be no more.(AJ)’”
A Prophecy Against Sidon
20 The word of the Lord came to me: 21 “Son of man, set your face against(AK) Sidon;(AL) prophesy against her 22 and say: ‘This is what the Sovereign Lord says:
“‘I am against you, Sidon,
and among you I will display my glory.(AM)
You will know that I am the Lord,
when I inflict punishment(AN) on you
and within you am proved to be holy.(AO)
23 I will send a plague upon you
and make blood flow in your streets.
The slain will fall within you,
with the sword against you on every side.
Then you will know that I am the Lord.(AP)
24 “‘No longer will the people of Israel have malicious neighbors who are painful briers and sharp thorns.(AQ) Then they will know that I am the Sovereign Lord.
25 “‘This is what the Sovereign Lord says: When I gather(AR) the people of Israel from the nations where they have been scattered,(AS) I will be proved holy(AT) through them in the sight of the nations. Then they will live in their own land, which I gave to my servant Jacob.(AU) 26 They will live there in safety(AV) and will build houses and plant(AW) vineyards; they will live in safety when I inflict punishment(AX) on all their neighbors who maligned them. Then they will know that I am the Lord their God.(AY)’”
Footnotes
- Ezekiel 28:3 Or Danel, a man of renown in ancient literature
- Ezekiel 28:13 The precise identification of some of these precious stones is uncertain.
- Ezekiel 28:13 The meaning of the Hebrew for this phrase is uncertain.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.