Ezekieli 27
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Nyimbo Yodandaulira Turo
27 Yehova anandiyankhula kuti: 2 “Iwe mwana wa munthu, imba nyimbo yodandaulira Turo. 3 Uza Turo, mzinda wokhala pa dooko la nyanja, wochita malonda ndi anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja kuti: Ambuye Yehova akuti,
“Iwe Turo, umanena kuti,
‘Ndine wokongola kwambiri.’
4 Malire ako anali mʼkati mwenimweni mwa nyanja;
amisiri ako anakukongoletsa kwambiri.
5 Anakupanga ndi matabwa
a payini ochokera ku Seniri;
anatenga mikungudza ya ku Lebanoni
kupangira mlongoti wako.
6 Ndi mitengo ya thundu ya ku Basani
anapanga zopalasira zako;
ndi matabwa a mitengo ya payini yochokera ku zilumba za Kitimu.
Pakuti anapanga thandala lako pakati pa matabwawo panali minyanga ya njovu.
7 Nsalu yabafuta yopeta yochokera ku Igupto inali thanga yako,
ndipo inakhala ngati mbendera.
Nsalu zophimba matenti ako zinali za mtundu wamtambo ndi pepo
zochokera ku zilumba za Elisa.
8 Anthu a ku Sidoni ndi Arivadi ndi amene anali opalasa ako.
Anthu aluso ako, iwe Turo, anali mwa iwe ndiwo amene ankakuyendetsa.
9 Akuluakulu ndi eni luso a ku Gebala anali mʼkati mwako,
ngati okonza zibowo zako.
Sitima za pa nyanja zonse, ndi oyendetsa ake
ankabwera pamodzi ndi katundu kudzachita nawe malonda.
10 “Anthu a ku Perisiya, a ku Ludi ndi Puti
anali asilikali mʼgulu lako la nkhondo.
Iwo ankapachika zishango ndi zipewa zawo zankhondo pa makoma ako,
kubweretsa kwa iwe ulemerero.
11 Anthu a ku Arivadi ndi Heleki
ankalondera mbali zonse za mpanda wako;
anthu a ku Gamadi
anali mu nsanja zako,
Iwo ankapachika zishango zawo pa makoma ako onse.
Amenewo ndiwo anakukongoletsa kwambiri.
12 “Dziko la Tarisisi linachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa katundu wako wamtundumtundu. Iwo ankapereka siliva, chitsulo, chitini ndi mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
13 “Yavani, Tubala ndi Mesaki ankachita nawe malonda; iwo ankapereka akapolo ndi ziwiya za mtovu mosinthanitsa ndi katundu wako.
14 “Anthu a ku Beti Togarima ankapereka akavalo antchito, akavalo ankhondo ndi abulu mosinthanitsa ndi katundu wako.
15 “Anthu a ku Dedani ankachita nawe malonda, ndipo anthu ambiri a mʼmbali mwa nyanja anali ogula malonda ako. Ankakupatsa minyanga ya njovu ndi phingo.
16 “Anthu a ku Aramu ankachita nawe malonda chifukwa cha kuchuluka kwa zinthu zako. Iwo ankapereka miyala ya emeradi, nsalu zapepo, nsalu zopetapeta, nsalu zabafuta, korali ndi miyala ya rubi mosinthanitsa ndi katundu wako.
17 “Yuda ndi Israeli ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka tirigu ochokera ku Miniti ndi zokometsera zakudya, uchi, mafuta ndi mankhwala mosinthanitsa ndi katundu wako.
18 “Anthu a ku Damasiko, chifukwa cha zinthu zako za malonda zambiri ndi katundu wako wosiyanasiyana, ankachita nawe malonda a vinyo wochokera ku Heliboni ndi ubweya wankhosa ochokera ku Zahari. 19 Adani ndi Agriki ochokera ku Uzala ankagula katundu wako. Iwo ankapereka chitsulo chosalala, kasiya ndi bango lonunkhira mosinthanitsa ndi katundu wako.
20 “Anthu a ku Dedani ankakugulitsa nsalu zoyika pa zishalo za akavalo.
21 “Arabiya ndi mafumu onse a ku Kedara anali ogula malonda ako. Iwo ankachita nawe malonda a ana ankhosa onenepa, nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
22 “Anthu amalonda a ku Seba ndi Raama ankachita nawe malonda. Iwo ankapereka zonunkhira zosiyanasiyana zabwino kwambiri, miyala yokongola ndi golide mosinthanitsa ndi katundu wako.
23 “Amalonda a ku Harani, Kane, Edeni, Seba, Asuri ndi Kilimadi ankachita nawe malonda. 24 Iwowa ankasinthanitsana nawe zovala zokongola, nsalu zopetapeta, zoyala pansi za mawangamawanga, atazimanga bwino ndi zingwe zolimba.
25 “Sitima za pa madzi za ku Tarisisi zinali
zonyamula malonda ako.
Motero iwe uli ngati sitima yapamadzi
yodzaza ndi katundu wolemera.
26 Anthu opalasa ako amakupititsa
pa nyanja yozama.
Koma mphepo yakummawa idzakuthyolathyola
pakati pa nyanja.
27 Chuma chako, katundu wako, malonda ako,
okuyendetsa ako, okuwongolera ako ndi opanga sitima za pa madzi,
anthu ako amalonda ndi asilikali ako onse
ndiponso aliyense amene ali mʼmenemo
adzamira mʼnyanja
tsiku limene udzawonongeka.
28 Madera a mʼmbali mwa nyanja adzagwedezeka
chifukwa cha kufuwula kwa oyendetsa sitimawo.
29 Onse amene amapalasa sitima zapamadzi,
adzatuluka mʼsitima zawo;
oyendetsa ndi onse owongolera sitima zapamadzi
adzayimirira mʼmbali mwa nyanja.
30 Iwo akufuwula,
kukulira iwe kwambiri;
akudzithira fumbi kumutu,
ndi kudzigubuduza pa phulusa.
31 Akumeta mpala mitu yawo chifukwa cha iwe
ndipo akuvala ziguduli.
Akukulira iweyo
ndi mitima yowawa kwambiri.
32 Akuyimba nyimbo
yokudandaulira nʼkumati:
‘Ndani anawonongedwapo ngati Turo
pakati pa nyanja?’
33 Pamene malonda ako ankawoloka nyanja
unakhutitsa mitundu yambiri ya anthu.
Mafumu a dziko lapansi analemera ndi chuma chako
komanso ndi malonda ako.
34 Koma tsopano wathyokera mʼnyanja,
pansi penipeni pa nyanja.
Katundu wako ndi onse amene anali nawe
amira pamodzi nawe.
35 Onse amene amakhala mʼmbali mwa nyanja
aopsedwa ndi zimene zakuchitikira.
Mafumu awo akuchita mantha
ndipo nkhope zangoti khululu.
36 Anthu amalonda a mitundu ina akukunyogodola.
Watha mochititsa mantha
ndipo sudzakhalaponso mpaka muyaya.”
Ezekiel 27
New International Version
A Lament Over Tyre
27 The word of the Lord came to me: 2 “Son of man, take up a lament(A) concerning Tyre. 3 Say to Tyre,(B) situated at the gateway to the sea,(C) merchant of peoples on many coasts, ‘This is what the Sovereign Lord says:
“‘You say, Tyre,
“I am perfect in beauty.(D)”
4 Your domain was on the high seas;
your builders brought your beauty to perfection.(E)
5 They made all your timbers
of juniper from Senir[a];(F)
they took a cedar from Lebanon(G)
to make a mast for you.
6 Of oaks(H) from Bashan
they made your oars;
of cypress wood[b] from the coasts of Cyprus(I)
they made your deck, adorned with ivory.
7 Fine embroidered linen(J) from Egypt was your sail
and served as your banner;
your awnings were of blue and purple(K)
from the coasts of Elishah.(L)
8 Men of Sidon and Arvad(M) were your oarsmen;
your skilled men, Tyre, were aboard as your sailors.(N)
9 Veteran craftsmen of Byblos(O) were on board
as shipwrights to caulk your seams.
All the ships of the sea(P) and their sailors
came alongside to trade for your wares.
10 “‘Men of Persia,(Q) Lydia(R) and Put(S)
served as soldiers in your army.
They hung their shields(T) and helmets on your walls,
bringing you splendor.
11 Men of Arvad and Helek
guarded your walls on every side;
men of Gammad
were in your towers.
They hung their shields around your walls;
they brought your beauty to perfection.(U)
12 “‘Tarshish(V) did business with you because of your great wealth of goods;(W) they exchanged silver, iron, tin and lead for your merchandise.
13 “‘Greece,(X) Tubal and Meshek(Y) did business with you; they traded human beings(Z) and articles of bronze for your wares.
14 “‘Men of Beth Togarmah(AA) exchanged chariot horses, cavalry horses and mules for your merchandise.
15 “‘The men of Rhodes[c](AB) traded with you, and many coastlands(AC) were your customers; they paid you with ivory(AD) tusks and ebony.
16 “‘Aram[d](AE) did business with you because of your many products; they exchanged turquoise,(AF) purple fabric, embroidered work, fine linen,(AG) coral(AH) and rubies for your merchandise.
17 “‘Judah and Israel traded with you; they exchanged wheat(AI) from Minnith(AJ) and confections,[e] honey, olive oil and balm(AK) for your wares.(AL)
18 “‘Damascus(AM) did business with you because of your many products and great wealth of goods.(AN) They offered wine from Helbon, wool from Zahar 19 and casks of wine from Izal(AO) in exchange for your wares: wrought iron, cassia(AP) and calamus.
20 “‘Dedan(AQ) traded in saddle blankets with you.
21 “‘Arabia(AR) and all the princes of Kedar(AS) were your customers; they did business with you in lambs, rams and goats.
22 “‘The merchants of Sheba(AT) and Raamah traded with you; for your merchandise they exchanged the finest of all kinds of spices(AU) and precious stones, and gold.(AV)
23 “‘Harran,(AW) Kanneh and Eden(AX) and merchants of Sheba, Ashur(AY) and Kilmad traded with you. 24 In your marketplace they traded with you beautiful garments, blue fabric, embroidered work and multicolored rugs with cords twisted and tightly knotted.
25 “‘The ships of Tarshish(AZ) serve
as carriers for your wares.
You are filled with heavy cargo
as you sail the sea.(BA)
26 Your oarsmen take you
out to the high seas.
But the east wind(BB) will break you to pieces
far out at sea.
27 Your wealth,(BC) merchandise and wares,
your mariners, sailors and shipwrights,
your merchants and all your soldiers,
and everyone else on board
will sink into the heart of the sea(BD)
on the day of your shipwreck.
28 The shorelands will quake(BE)
when your sailors cry out.
29 All who handle the oars
will abandon their ships;
the mariners and all the sailors
will stand on the shore.
30 They will raise their voice
and cry bitterly over you;
they will sprinkle dust(BF) on their heads
and roll(BG) in ashes.(BH)
31 They will shave their heads(BI) because of you
and will put on sackcloth.
They will weep(BJ) over you with anguish of soul
and with bitter mourning.(BK)
32 As they wail and mourn over you,
they will take up a lament(BL) concerning you:
“Who was ever silenced like Tyre,
surrounded by the sea?(BM)”
33 When your merchandise went out on the seas,(BN)
you satisfied many nations;
with your great wealth(BO) and your wares
you enriched the kings of the earth.
34 Now you are shattered by the sea
in the depths of the waters;
your wares and all your company
have gone down with you.(BP)
35 All who live in the coastlands(BQ)
are appalled(BR) at you;
their kings shudder with horror
and their faces are distorted with fear.(BS)
36 The merchants among the nations scoff at you;(BT)
you have come to a horrible end
and will be no more.(BU)’”
Footnotes
- Ezekiel 27:5 That is, Mount Hermon
- Ezekiel 27:6 Targum; the Masoretic Text has a different division of the consonants.
- Ezekiel 27:15 Septuagint; Hebrew Dedan
- Ezekiel 27:16 Most Hebrew manuscripts; some Hebrew manuscripts and Syriac Edom
- Ezekiel 27:17 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
Ezekiel 27
King James Version
27 The word of the Lord came again unto me, saying,
2 Now, thou son of man, take up a lamentation for Tyrus;
3 And say unto Tyrus, O thou that art situate at the entry of the sea, which art a merchant of the people for many isles, Thus saith the Lord God; O Tyrus, thou hast said, I am of perfect beauty.
4 Thy borders are in the midst of the seas, thy builders have perfected thy beauty.
5 They have made all thy ship boards of fir trees of Senir: they have taken cedars from Lebanon to make masts for thee.
6 Of the oaks of Bashan have they made thine oars; the company of the Ashurites have made thy benches of ivory, brought out of the isles of Chittim.
7 Fine linen with broidered work from Egypt was that which thou spreadest forth to be thy sail; blue and purple from the isles of Elishah was that which covered thee.
8 The inhabitants of Zidon and Arvad were thy mariners: thy wise men, O Tyrus, that were in thee, were thy pilots.
9 The ancients of Gebal and the wise men thereof were in thee thy calkers: all the ships of the sea with their mariners were in thee to occupy thy merchandise.
10 They of Persia and of Lud and of Phut were in thine army, thy men of war: they hanged the shield and helmet in thee; they set forth thy comeliness.
11 The men of Arvad with thine army were upon thy walls round about, and the Gammadims were in thy towers: they hanged their shields upon thy walls round about; they have made thy beauty perfect.
12 Tarshish was thy merchant by reason of the multitude of all kind of riches; with silver, iron, tin, and lead, they traded in thy fairs.
13 Javan, Tubal, and Meshech, they were thy merchants: they traded the persons of men and vessels of brass in thy market.
14 They of the house of Togarmah traded in thy fairs with horses and horsemen and mules.
15 The men of Dedan were thy merchants; many isles were the merchandise of thine hand: they brought thee for a present horns of ivory and ebony.
16 Syria was thy merchant by reason of the multitude of the wares of thy making: they occupied in thy fairs with emeralds, purple, and broidered work, and fine linen, and coral, and agate.
17 Judah, and the land of Israel, they were thy merchants: they traded in thy market wheat of Minnith, and Pannag, and honey, and oil, and balm.
18 Damascus was thy merchant in the multitude of the wares of thy making, for the multitude of all riches; in the wine of Helbon, and white wool.
19 Dan also and Javan going to and fro occupied in thy fairs: bright iron, cassia, and calamus, were in thy market.
20 Dedan was thy merchant in precious clothes for chariots.
21 Arabia, and all the princes of Kedar, they occupied with thee in lambs, and rams, and goats: in these were they thy merchants.
22 The merchants of Sheba and Raamah, they were thy merchants: they occupied in thy fairs with chief of all spices, and with all precious stones, and gold.
23 Haran, and Canneh, and Eden, the merchants of Sheba, Asshur, and Chilmad, were thy merchants.
24 These were thy merchants in all sorts of things, in blue clothes, and broidered work, and in chests of rich apparel, bound with cords, and made of cedar, among thy merchandise.
25 The ships of Tarshish did sing of thee in thy market: and thou wast replenished, and made very glorious in the midst of the seas.
26 Thy rowers have brought thee into great waters: the east wind hath broken thee in the midst of the seas.
27 Thy riches, and thy fairs, thy merchandise, thy mariners, and thy pilots, thy calkers, and the occupiers of thy merchandise, and all thy men of war, that are in thee, and in all thy company which is in the midst of thee, shall fall into the midst of the seas in the day of thy ruin.
28 The suburbs shall shake at the sound of the cry of thy pilots.
29 And all that handle the oar, the mariners, and all the pilots of the sea, shall come down from their ships, they shall stand upon the land;
30 And shall cause their voice to be heard against thee, and shall cry bitterly, and shall cast up dust upon their heads, they shall wallow themselves in the ashes:
31 And they shall make themselves utterly bald for thee, and gird them with sackcloth, and they shall weep for thee with bitterness of heart and bitter wailing.
32 And in their wailing they shall take up a lamentation for thee, and lament over thee, saying, What city is like Tyrus, like the destroyed in the midst of the sea?
33 When thy wares went forth out of the seas, thou filledst many people; thou didst enrich the kings of the earth with the multitude of thy riches and of thy merchandise.
34 In the time when thou shalt be broken by the seas in the depths of the waters thy merchandise and all thy company in the midst of thee shall fall.
35 All the inhabitants of the isles shall be astonished at thee, and their kings shall be sore afraid, they shall be troubled in their countenance.
36 The merchants among the people shall hiss at thee; thou shalt be a terror, and never shalt be any more.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.