Add parallel Print Page Options

Za Chilango cha Turo

26 Pa chaka cha khumi ndi chimodzi, tsiku loyamba la mwezi, Yehova anandiyankhula kuti: “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Turo ananyogodola Yerusalemu kuti ‘Hii! Uja amene anali chipata choloweramo anthu a mitundu ina wawonongeka. Zitseko zake zatsekukira ife. Tidzalemera popeza wasanduka bwinja.’ Nʼchifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakulangani, inu anthu a ku Turo. Ndidzakuyitanirani anthu a mitundu ina kuti adzakulangeni monga momwe mafunde amawombera pa Nyanja. Anthuwo adzawononga makoma a Turo ndi kugwetsa nsanja zake. Ndidzapala dothi lake ndipo ndidzamusandutsa thanthwe losalala. Udzakhala poyanikapo makoka pakati pa nyanja. Ine Ambuye Yehova ndayankhula zimenezo. Udzasanduka chofunkha cha anthu a mitundu ina. Anthu okhala ku mtunda adzasakazidwa ndi lupanga. Pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Iwe Turo, ndidzakubweretsera Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni mfumu ya mafumu, kuchokera kumpoto pamodzi ndi akavalo ndiponso magaleta, anthu okwera pa akavalo ndi gulu lalikulu la ankhondo. Anthu okhala ku mtunda adzawapha ndi lupanga. Adzapanga mitumbira yankhondo ndi kukukwezera zishango kuti alimbane nawe. Adzagwetsa makoma ako ndi zida zogumulira khoma ndi kugwetsa nsanja zako ndi nkhwangwa zake. 10 Akavalo ake adzakhala ochuluka kwambiri kotero kuti adzakukwirira ndi fumbi lawo. Makoma ako adzagwedezeka ndi mdidi wa akavalo, ngolo ndi magaleta pamene iye adzalowa pa zipata monga mmene amalowera mu mzinda umene makoma ake agwetsedwa. 11 Akavalo ake adzapondaponda mʼmisewu yako yonse ndi ziboda zawo. Adzapha anthu ako ndi lupanga. Mizati yako yolimba idzagwetsedwa. 12 Iwo adzafunkha chuma chako ndipo adzalanda zinthu zako za malonda. Adzagwetsa makoma ako ndi kuwononga nyumba zako zabwino. Adzaponya miyala yako, matabwa ako ndi dothi lako mʼnyanja. 13 Choncho ndidzathetsa phokoso la nyimbo zanu, ndipo kulira kwa apangwe ako sikudzamvekanso. 14 Ndidzakusandutsa thanthwe losalala, ndipo udzakhala malo woyanikapo makoka a nsomba. Sudzamangidwanso, pakuti Ine Yehova ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.

15 “Ine Ambuye Yehova ndikukuwuza, iwe mzinda wa Turo, kuti zilumba zidzagwedezeka pakumva za kugwa kwako ndiponso poona anthu opweteka akubuwula ndipo anthu akuphedwa pakati pako. 16 Pamenepo mafumu a mʼmbali mwa nyanja adzatsika pa mipando yawo yaufumu. Adzayika pambali mikanjo yawo ndi kuvala zovala zawo zamakaka. Adzachita mantha ndipo adzakhala pansi akunjenjemera kosalekeza. Adzathedwa nzeru poona zimene zakugwera. 17 Pamenepo adzayimba nyimbo yokudandaula ndipo adzati kwa iwe:

“ ‘Nʼkuchita kuwonongeka chotere, iwe mzinda wotchuka,
    wodzaza ndi anthu a ku nyanja!
Unali wamphamvu pa nyanja,
    iwe ndi nzika zako;
unkaopseza anthu onse amene
    ankakhala kumeneko.
18 Tsopano mayiko a mʼmbali mwa nyanja akunjenjemera
    chifukwa cha kugwa kwako;
okhala pa zilumba nawonso agwidwa ndi mantha aakulu
    chifukwa cha kugwa kwako.’

19 “Mawu a Ine Ambuye Yehova ndi awa: Ndidzakusandutsa bwinja, ngati mizinda imene anthu sangathe kukhalamo. Ndidzakuphimba ndi madzi ozama a mʼnyanja, madzi amphamvu woti akumize. 20 Ndidzakugwetsa pansi kuti ukhale pamodzi ndi anthu amvulazakale amene akutsikira ku manda. Ine ndidzakusunga ku dzenjeko ngati ku bwinja losiyidwa kalekale, pamodzi ndi anthu amene anafa kale motero sudzabwererako kukhala pakati pa anthu amoyo. 21 Ine ndidzakuthetsa mochititsa mantha, ndipo sudzakhalaponso. Anthu adzakufunafuna, koma sudzapezekanso, akutero Ambuye Yehova.”

A Prophecy Against Tyre

26 In the eleventh month of the twelfth[a] year, on the first day of the month, the word of the Lord came to me:(A) “Son of man, because Tyre(B) has said of Jerusalem, ‘Aha!(C) The gate to the nations is broken, and its doors have swung open to me; now that she lies in ruins I will prosper,’ therefore this is what the Sovereign Lord says: I am against you, Tyre, and I will bring many nations against you, like the sea(D) casting up its waves. They will destroy(E) the walls of Tyre(F) and pull down her towers; I will scrape away her rubble and make her a bare rock. Out in the sea(G) she will become a place to spread fishnets,(H) for I have spoken, declares the Sovereign Lord. She will become plunder(I) for the nations,(J) and her settlements on the mainland will be ravaged by the sword. Then they will know that I am the Lord.

“For this is what the Sovereign Lord says: From the north I am going to bring against Tyre Nebuchadnezzar[b](K) king of Babylon, king of kings,(L) with horses and chariots,(M) with horsemen and a great army. He will ravage your settlements on the mainland with the sword; he will set up siege works(N) against you, build a ramp(O) up to your walls and raise his shields against you. He will direct the blows of his battering rams against your walls and demolish your towers with his weapons.(P) 10 His horses will be so many that they will cover you with dust. Your walls will tremble at the noise of the warhorses, wagons and chariots(Q) when he enters your gates as men enter a city whose walls have been broken through. 11 The hooves(R) of his horses will trample all your streets; he will kill your people with the sword, and your strong pillars(S) will fall to the ground.(T) 12 They will plunder your wealth and loot your merchandise; they will break down your walls and demolish your fine houses and throw your stones, timber and rubble into the sea.(U) 13 I will put an end(V) to your noisy songs,(W) and the music of your harps(X) will be heard no more.(Y) 14 I will make you a bare rock, and you will become a place to spread fishnets. You will never be rebuilt,(Z) for I the Lord have spoken, declares the Sovereign Lord.

15 “This is what the Sovereign Lord says to Tyre: Will not the coastlands(AA) tremble(AB) at the sound of your fall, when the wounded groan(AC) and the slaughter takes place in you? 16 Then all the princes of the coast will step down from their thrones and lay aside their robes and take off their embroidered(AD) garments. Clothed(AE) with terror, they will sit on the ground,(AF) trembling(AG) every moment, appalled(AH) at you. 17 Then they will take up a lament(AI) concerning you and say to you:

“‘How you are destroyed, city of renown,
    peopled by men of the sea!
You were a power on the seas,
    you and your citizens;
you put your terror
    on all who lived there.(AJ)
18 Now the coastlands tremble(AK)
    on the day of your fall;
the islands in the sea
    are terrified at your collapse.’(AL)

19 “This is what the Sovereign Lord says: When I make you a desolate city, like cities no longer inhabited, and when I bring the ocean depths(AM) over you and its vast waters cover you,(AN) 20 then I will bring you down with those who go down to the pit,(AO) to the people of long ago. I will make you dwell in the earth below, as in ancient ruins, with those who go down to the pit, and you will not return or take your place[c] in the land of the living.(AP) 21 I will bring you to a horrible end and you will be no more.(AQ) You will be sought, but you will never again be found, declares the Sovereign Lord.”(AR)

Footnotes

  1. Ezekiel 26:1 Probable reading of the original Hebrew text; Masoretic Text does not have month of the twelfth.
  2. Ezekiel 26:7 Hebrew Nebuchadrezzar, of which Nebuchadnezzar is a variant; here and often in Ezekiel and Jeremiah
  3. Ezekiel 26:20 Septuagint; Hebrew return, and I will give glory