Add parallel Print Page Options

Mulungu Apatsa Mose Mphamvu Zochita Zodabwitsa

Mose anayankha, “Aisraeliwo sakandikhulupirira ndipo sakandimvera. Iwowo adzati, ‘Yehova sanakuonekere iwe.’ ”

Ndipo Yehova anamufunsa nati, “Nʼchiyani chili mʼdzanja lakolo?”

Mose anayankha kuti, “Ndodo.”

Yehova anati, “Tayiponya pansi.”

Mose anayiponya pansi ndipo inasanduka njoka ndipo anayithawa. Kenaka Yehova anati kwa iye, “Igwire mtchira.” Ndipo Mose anayigwira mchira njokayo ndipo inasandukanso ndodo mʼdzanja lake. Yehova anati, “Ukachite zimenezi ndipo akakukhulupirira kuti Yehova, Mulungu wa makolo awo, Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo, wakuonekera iwe.”

Yehova anatinso, “Pisa dzanja lako mʼmalaya akowo.” Choncho Mose anapisa dzanja lake mʼmalaya ake ndipo pamene analitulutsa, linali la khate kuchita kuti mbuu ngati ufa.

Yehova anati, “Tsopano pisanso dzanja lako mʼmalaya.” Mose anapisanso dzanja lakelo mʼmalaya ake ndipo atalitulutsa, linali labwinobwino, ngati thupi lake lonse.

Tsono Yehova anati “Akakapanda kukukhulupirira, osalabadira chozizwitsa choyambacho, akakhulupirira ndithu chifukwa cha chozizwitsa chachiwiricho. Koma ngati sakakhulupirira zizindikiro ziwiri izi kapena kukumvera, ukatunge madzi a mu mtsinje wa Nailo ndi kuwathira pa mtunda powuma ndipo madziwo adzasanduka magazi.”

10 Mose anati kwa Yehova, “Chonde Ambuye, chikhalire ine ndakhala munthu wosatha kuyankhula bwino. Ngakhale tsopano pamene mukundiyankhula, lilime langa ndi lolemera. Ndine wachibwibwi.”

11 Yehova anati kwa iye, “Kodi anapatsa munthu pakamwa ndani? Ndani amasandutsa munthu kuti akhale wosayankhula kapena wosamva? Ndani amapanga munthu kukhala wopenya kapena wosaona? Kodi si Ine Yehova? 12 Tsopano pita, Ine ndidzakuthandiza kuyankhula ndipo ndidzakulangiza zoti ukanene.”

13 Koma Mose anati, “Chonde Ambuye, pepani, tumani wina kuti akachite zimenezi.”

14 Kenaka Yehova anamupsera mtima Mose ndipo anati, “Kodi suli ndi mʼbale wako Aaroni wa fuko la Levi? Ine ndikudziwa kuti iye amayankhula bwino. Iye wanyamuka kale kudzakumana nawe ndipo adzasangalala akadzakuona. 15 Iwe udzayankhula naye ndi kumuwuza mawu oti akanene. Ine ndidzakuthandizani kuyankhula nonse awirinu ndi kukulangizani zoti mukachite. 16 Iye akayankhula kwa anthu mʼmalo mwako. Iye adzakhala wokuyankhulira ndipo iweyo udzakhala ngati Mulungu kwa iye. 17 Koma utenge ndodo imene ili mʼdzanja lakoyo kuti ukachite nayo zizindikiro zozizwitsa.”

Mose Abwerera ku Igupto

18 Tsono Mose anabwerera kwa Yetero, mpongozi wake ndipo anati kwa Iye, “Chonde ndiloleni kuti ndibwerere ku Igupto kwa anthu anga kuti ndikaone ngati ali moyo.”

Yeteri anati, “Pitani mu mtendere.”

19 Nthawiyi Yehova anali atamuwuza kale Mose ku Midiyani kuti, “Bwerera ku Igupto, pakuti anthu onse amene amafuna kukupha aja anamwalira.” 20 Kotero Mose anatenga mkazi wake ndi ana ake aamuna, ndipo anawakweza pa bulu nayamba ulendo wobwerera ku Igupto. Ndipo anatenga ndodo ya Mulungu ija mʼdzanja lake.

21 Yehova anati kwa Mose, “Ukaonetsetse kuti wachita pamaso pa Farao zodabwitsa zonse zimene ndayika mphamvu mwa iwe kuti ukachite. Koma Ine ndidzawumitsa mtima wake kotero kuti sadzalola anthuwo kuti apite. 22 Ndipo iwe ukati kwa Farao, ‘Yehova akuti, Israeli ali ngati mwana wanga wachisamba.’ 23 Choncho ndikuti, ‘Mulole mwana wanga apite kuti akandipembedze. Koma ngati ukana, Ine ndidzapha mwana wako wachisamba.’ ”

24 Pambuyo pake Mose ali mʼnjira, pamalo wogona, Yehova anakumana naye, ndipo anafuna kumupha. 25 Koma Zipora anatenga mwala wakuthwa nachita mdulidwe mwana wake ndipo khungulo analikhudzitsa pa mapazi a Mose. Iye anati “Zoonadi, kwa ine ndiwe mkwati wamagazi.” 26 Choncho Yehova anamuleka Mose wosamupha. Pa nthawiyo, Zipora anati, “Mkwati wa magazi,” ponena za mdulidwe.

27 Yehova anati kwa Aaroni, “Pita ku chipululu ukakumane ndi Mose.” Iye anapitadi nakakumana ndi Mose pa phiri la Mulungu namupsompsona. 28 Kenaka Mose anamufotokozera Aaroni chilichonse chimene Yehova anamutuma kuti akanene. Anamufotokozera za zizindikiro zozizwitsa zimene anamulamulira kuti akazichite.

29 Mose ndi Aaroni anapita kukasonkhanitsa pamodzi akuluakulu onse a Aisraeli. 30 Ndipo Aaroni anawafotokozera zonse zimene Yehova ananena kwa Mose. Anachita zizindikirozo pamaso pa anthu onse, 31 ndipo anakhulupirira. Iwo atamva kuti Yehova anadzawayendera ndi kuti waona mmene akuzunzikira, anaweramitsa mitu pansi napembedza.

Moses Given Powerful Signs

Then Moses answered, “But behold, they will not believe me or listen to my voice, for they will say, ‘The Lord did not appear to you.’” The Lord said to him, “What is that in your hand?” He said, (A)“A staff.” And he said, “Throw it on the ground.” So he threw it on the ground, and it became a serpent, and Moses ran from it. But the Lord said to Moses, “Put out your hand and catch it by the tail”—so he put out his hand and caught it, and it became a staff in his hand— “that they may (B)believe that the Lord, (C)the God of their fathers, the God of Abraham, the God of Isaac, and the God of Jacob, has appeared to you.” Again, the Lord said to him, “Put your hand inside your cloak.”[a] And he put his hand inside his cloak, and when he took it out, behold, his hand was (D)leprous[b] like snow. Then God said, “Put your hand back inside your cloak.” So he put his hand back inside his cloak, and when he took it out, behold, (E)it was restored like the rest of his flesh. “If they will not believe you,” God said, “or listen to the first sign, they may believe the latter sign. If they will not believe even these two signs or listen to your voice, you shall take some water from the Nile and pour it on the dry ground, and the water that you shall take from the Nile (F)will become blood on the dry ground.”

10 But Moses said to the Lord, “Oh, my Lord, I am not eloquent, either in the past or since you have spoken to your servant, but (G)I am slow of speech and of tongue.” 11 Then the Lord said to him, “Who has made man's mouth? Who makes him mute, or deaf, or seeing, or blind? Is it not I, the Lord? 12 Now therefore go, and (H)I will be with your mouth and teach you what you shall speak.” 13 But he said, “Oh, my Lord, please send someone else.” 14 Then the anger of the Lord was kindled against Moses and he said, “Is there not Aaron, your brother, the Levite? I know that he can speak well. Behold, (I)he is coming out to meet you, and when he sees you, he will be glad in his heart. 15 (J)You shall speak to him and (K)put the words in his mouth, and (L)I will be with your mouth and with his mouth and will teach you both what to do. 16 (M)He shall speak for you to the people, and he shall be your mouth, and (N)you shall be as God to him. 17 And take in your hand (O)this staff, with which you shall do the signs.”

Moses Returns to Egypt

18 Moses went back to (P)Jethro his father-in-law and said to him, “Please let me go back to my brothers in Egypt to see whether they are still alive.” And Jethro said to Moses, “Go in peace.” 19 And the Lord said to Moses in Midian, “Go back to Egypt, for (Q)all the men who were seeking your life are dead.” 20 So Moses took (R)his wife and his sons and had them ride on a donkey, and went back to the land of Egypt. And Moses took (S)the staff of God in his hand.

21 And the Lord said to Moses, “When you go back to Egypt, see that you do before Pharaoh all the (T)miracles that I have put in your power. But (U)I will harden his heart, so that he will not let the people go. 22 Then you shall say to Pharaoh, ‘Thus says the Lord, (V)Israel is my (W)firstborn son, 23 and I say to you, “Let my son go that he may serve me.” If you refuse to let him go, behold, I (X)will kill your firstborn son.’”

24 At a lodging place on the way (Y)the Lord met him and (Z)sought to put him to death. 25 Then (AA)Zipporah took a (AB)flint and cut off her son's foreskin and touched Moses'[c] feet with it and said, “Surely you are a bridegroom of blood to me!” 26 So he let him alone. It was then that she said, “A bridegroom of blood,” because of the circumcision.

27 The Lord said to Aaron, “Go into the wilderness (AC)to meet Moses.” So he went and met him at the (AD)mountain of God and kissed him. 28 And Moses (AE)told Aaron all the words of the Lord with which he had sent him to speak, and all (AF)the signs that he had commanded him to do. 29 Then Moses and Aaron (AG)went and gathered together all the elders of the people of Israel. 30 (AH)Aaron spoke all the words that the Lord had spoken to Moses and did the signs in the sight of the people. 31 And the people (AI)believed; and when they heard that the Lord had (AJ)visited the people of Israel and that he had (AK)seen their affliction, (AL)they bowed their heads and worshiped.

Footnotes

  1. Exodus 4:6 Hebrew into your bosom; also verse 7
  2. Exodus 4:6 Leprosy was a term for several skin diseases; see Leviticus 13
  3. Exodus 4:25 Hebrew his