Deuteronomo 33
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Mose Adalitsa Mafuko a Aisraeli
33 Awa ndi madalitso amene Mose, munthu wa Mulungu, anawapereka kwa Aisraeli asanafe. 2 Iye anati:
“Yehova anabwera kuchokera ku Sinai
ndipo anatulukira kuchokera ku Seiri;
anawala kuchokera pa Phiri la Parani.
Iye anabwera ndi chiwunyinji cha angelo
kuchokera kummwera, moto woyaka uli mʼdzanja mwake.
3 Ndithu ndinu amene mumakonda anthu anu;
opatulika ake onse ali mʼmanja mwake.
Onse amagwada pansi pa mapazi anu
kuchokera kwa inu amalandira malangizo,
4 malamulo amene Mose anatipatsa,
chuma chopambana cha mtundu wa Yakobo.
5 Iye anali mfumu ya Yesuruni
pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,
pamodzi ndi mafuko a Israeli.
6 “Lolani Rubeni akhale ndi moyo ndipo asafe,
anthu ake asachepe pa chiwerengero.”
7 Ndipo ponena za Yuda anati:
“Inu Yehova, imvani kulira kwa Yuda;
mubweretseni kwa anthu ake.
Ndi manja ake omwe adziteteze yekha.
Inu khalani thandizo lake polimbana ndi adani ake!”
8 Za fuko la Alevi anati:
“Tumimu wanu ndi Urimu ndi za
mtumiki wanu wokhulupirika.
Munamuyesa ku Masa;
munalimbana naye ku madzi a ku Meriba.
9 Iye ananena za abambo ake ndi amayi ake kuti,
‘Sindilabadira za iwo.’
Sanasamale za abale ake
kapena ana ake,
koma anayangʼanira mawu anu
ndipo anateteza pangano lanu.
10 Iye amaphunzitsa Yakobo malangizo anu
ndi malamulo anu kwa Israeli.
Amafukiza lubani pamaso panu
ndiponso amapereka nsembe zanu zonse zopsereza pa guwa lanu.
11 Inu Yehova, dalitsani luso lake lonse
ndipo mukondwere ndi ntchito za manja ake.
Menyani adani awo mʼchiwuno
kanthani amene amuwukira kuti asadzukenso.”
12 Za fuko la Benjamini anati:
“Wokondedwa wa Yehova akhale mwamtendere mwa Iye,
pakuti amamuteteza tsiku lonse,
ndipo amene Yehova amamukonda amawusa pa mapewa ake.”
13 Za fuko la Yosefe anati:
“Yehova adalitse dziko lake
ndi mame ambiri ochokera kumwamba
ndiponso madzi ambiri ochokera pansi pa nthaka;
14 ndi zinthu zambiri zimene zimacha ndi dzuwa
ndiponso ndi zokolola zabwino kwambiri zimene zimacha ndi mwezi uliwonse;
15 ndi zipatso zabwino kwambiri zochokera mʼmapiri amakedzanawa
ndiponso zokolola zochuluka zochokera ku zitunda zakalekale;
16 ndi mphatso zabwino kwambiri zochokera pa dziko lapansi ndi zonse zimene zili mʼmenemo
ndiponso kukoma mtima kwa Iye amene amakhala mʼchitsamba choyaka moto.
Madalitso onsewa akhale pa mutu pa Yosefe,
wapaderadera pakati pa abale ake.
17 Ulemerero wake uli ngati ngʼombe yayimuna yoyamba kubadwa;
nyanga zake zili ngati za njati.
Ndi nyanga zakezo adzapirikitsa anthu a mitundu ina,
ngakhale iwo amene akukhala ku malekezero a dziko lapansi.
Nyanga zimenezi ndiye anthu miyandamiyanda a Efereimu;
nyanga zimenezi ndiye anthu 1,000 a Manase.”
18 Za fuko la Zebuloni anati:
“Kondwera Zebuloni, pamene ukutuluka,
ndipo iwe, Isakara, kondwera mʼmatenti ako.
19 Adzayitanira mitundu ya anthu kumapiri,
kumeneko adzaperekako nsembe zachilungamo;
kumeneko adzadyerera zinthu zochuluka zochokera ku nyanja,
chuma chobisika mu mchenga.”
20 Za fuko la Gadi anati:
“Wodala amene amakulitsa malire a Gadi!
Gadi amakhala kumeneko ngati mkango,
kukhadzula mkono kapena mutu.
21 Iye anadzisankhira dziko labwino kwambiri;
gawo la mtsogoleri anasungira iye.
Pamene atsogoleri a anthu anasonkhana,
anachita chifuniro cha Yehova molungama,
ndiponso malamulo onena za Israeli.”
22 Za fuko la Dani anati:
“Dani ndi mwana wamkango,
amene akutuluka ku Basani.”
23 Za fuko la Nafutali anati:
“Nafutali wadzaza ndi kukoma mtima kwa Yehova
ndipo ndi wodzaza ndi madalitso ake;
cholowa chake chidzakhala mbali ya kummwera kwa nyanja.”
24 Za fuko la Aseri anati:
“Mwana wodalitsika kwambiri ndi Aseri;
abale ake amukomere mtima,
ndipo asambe mapazi ake mʼmafuta.
25 Zotsekera za zipata zako zidzakhala za chitsulo ndi za mkuwa,
ndi mphamvu zako zidzakhala ngati masiku a moyo wako.
26 “Palibe wina wofanana ndi Mulungu wa Yesuruni,
amene amakwera pa thambo kukuthandizani
ndiponso pa mitambo ya ulemerero wake.
27 Mulungu wamuyaya ndiye pothawirapo pathu,
ndipo pa dziko lapansi amakusungani ndi mphamvu zosatha.
Adzathamangitsa patsogolo panu mdani wanu,
adzanena kuti, ‘Muwonongeni!’
28 Motero Israeli adzakhala yekha mwamtendere;
zidzukulu za Yakobo zili pa mtendere
mʼdziko la tirigu ndi vinyo watsopano,
kumene thambo limagwetsa mame.
29 Iwe Israeli, ndiwe wodala!
Wofanana nanu ndani
anthu opulumutsidwa ndi Yehova?
Iye ndiye chishango ndi mthandizi wanu
ndi lupanga lanu la ulemerero.
Adani ako adzakugonjera,
ndipo iwe udzapondereza pansi malo awo achipembedzo.”
Deuteronomy 33
New American Standard Bible
The Blessing by Moses
33 Now this is the blessing with which Moses (A)the man of God blessed the sons of Israel before his death. 2 He said,
“(B)The Lord came from Sinai,
(C)And [a]dawned on them from Seir;
(D)He shone from Mount Paran,
And He came from (E)the midst of myriads of [b]holy ones;
(F)At His right hand there was [c]flashing lightning for them.
3 (G)Indeed, He loves [d]the people;
(H)All [e]Your holy ones are in Your hand,
(I)And they [f]followed in Your steps;
Everyone takes of Your words.
4 (J)Moses issued to us the Law,
(K)A possession for the assembly of Jacob.
5 (L)And He was king in [g]Jeshurun,
When the heads of the people gathered,
The tribes of Israel together.
6 “(M)May Reuben live and not die,
Nor may his people be few.”
7 (N)And this was regarding Judah; so he said:
“Hear, Lord, the voice of Judah,
And bring him to his people.
With his hands he contended for [h]them,
And may You be a help against his adversaries.”
8 Of Levi he said,
“Let Your (O)Thummim and Your Urim belong to Your (P)godly man,
(Q)Whom You tested at Massah,
With [i]whom You contended at the waters of Meribah;
9 (R)Who said of his father and his mother,
‘I did not consider them’;
And he did not acknowledge his brothers,
Nor did he regard his own sons,
For (S)they kept Your word,
And complied with Your covenant.
10 (T)They will teach Your ordinances to Jacob,
And Your Law to Israel.
(U)They shall put [j]incense before You,
And (V)whole burnt offerings on Your altar.
11 Lord, bless his strength,
And accept the work of his hands;
Smash the [k]hips of those who rise up against him,
And those who hate him, so that they do not rise again.”
12 Of Benjamin he said,
“(W)May the beloved of the Lord live in security beside Him
(X)Who shields him all the day long,
(Y)And he lives between His shoulders.”
13 Of Joseph he said,
“(Z)Blessed of the Lord be his land,
With the choice things of heaven, with the dew,
And from the deep waters lying beneath,
14 And with the choice yield of the sun,
And the choice produce of the months;
15 And with the [l]best things of (AA)the ancient mountains,
With the choice things of the everlasting hills,
16 And with the choice things of the earth and its fullness,
And the favor (AB)of Him who dwelt in the bush.
Let it come to the head of Joseph,
And to the top of the head of the one who was prince among his brothers.
17 As the firstborn of his ox, majesty is his,
And his horns are the horns of (AC)the wild ox;
With them he will (AD)gore the peoples
All [m]at once, to the ends of the earth.
And those are the ten thousands of Ephraim,
And those are the thousands of Manasseh.”
18 (AE)Of Zebulun he said,
“Rejoice, Zebulun, in your going out,
And, Issachar, in your tents.
19 (AF)They will call peoples to the mountain;
There they will offer (AG)righteous sacrifices;
For they will [n]draw out (AH)the abundance of the seas,
And the hidden treasures of the sand.”
20 (AI)Of Gad he said,
“Blessed is the one who enlarges Gad;
He lies down (AJ)as a [o]lion,
And tears the arm, also the crown of the head.
21 (AK)Then he [p]selected the choicest part for himself,
(AL)For there the ruler’s portion was [q]reserved;
(AM)And he came with the leaders of the people;
(AN)He executed the justice of the Lord,
And His ordinances with Israel.”
22 (AO)Of Dan he said,
“Dan is (AP)a lion’s cub;
He leaps out from Bashan.”
23 Of Naphtali he said,
“(AQ)Naphtali, satisfied with favor,
And full of the blessing of the Lord,
Take possession of the sea and the south.”
24 (AR)Of Asher he said,
“More blessed than sons is Asher;
May he be favored by his brothers,
(AS)And may he dip his foot in olive oil.
25 (AT)Your [r]bars will be iron and bronze,
(AU)And as your days, so will your strength be.
26 “(AV)There is no one like the God of [s]Jeshurun,
(AW)Who rides the heavens [t]to your help,
And the clouds in His majesty.
27 (AX)The eternal God is a [u]hiding place,
(AY)And underneath are the everlasting arms;
(AZ)And He drove out the enemy from you,
(BA)And said, ‘Destroy!’
28 (BB)So Israel lives in security,
(BC)The fountain of Jacob secluded,
(BD)In a land of grain and new wine;
(BE)His heavens also drip down dew.
29 (BF)Blessed are you, Israel;
(BG)Who is like you, a people saved by the Lord,
(BH)The shield of your help,
(BI)And He who is the sword of your majesty!
(BJ)So your enemies will cringe before you,
(BK)And you will trample on their high places.”
Footnotes
- Deuteronomy 33:2 Lit rose to
- Deuteronomy 33:2 Lit holiness
- Deuteronomy 33:2 Or a fiery law
- Deuteronomy 33:3 Lit peoples
- Deuteronomy 33:3 Lit His
- Deuteronomy 33:3 Or lie down at Your feet
- Deuteronomy 33:5 A symbolic name for Israel
- Deuteronomy 33:7 Lit him
- Deuteronomy 33:8 Lit him
- Deuteronomy 33:10 Lit smoke in Your nostrils
- Deuteronomy 33:11 Lit loins
- Deuteronomy 33:15 Or chief
- Deuteronomy 33:17 Or together
- Deuteronomy 33:19 Lit suck
- Deuteronomy 33:20 Or lioness
- Deuteronomy 33:21 Lit saw
- Deuteronomy 33:21 Lit covered
- Deuteronomy 33:25 I.e., to secure gates
- Deuteronomy 33:26 I.e., Israel
- Deuteronomy 33:26 Lit in
- Deuteronomy 33:27 Or refuge
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
New American Standard Bible®, Copyright © 1960, 1971, 1977, 1995, 2020 by The Lockman Foundation. All rights reserved.
