Chivumbulutso 15
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Angelo Asanu ndi Awiri Okhala ndi Miliri Isanu ndi Iwiri
15 Kumwamba ndinaona chizindikiro china chachikulu ndi chodabwitsa: angelo asanu ndi awiri ali ndi miliri isanu ndi iwiri yomaliza chifukwa Mulungu anakwiya kotheratu. 2 Ndipo ndinaona chimene chinaoneka ngati nyanja yonyezimira yosakaniza ndi moto, ndipo pambali pa nyanjayo panayima amene anagonjetsa chirombo chija ndi fano lake, ndi nambala yotanthauza dzina lake. Anthuwo ananyamula azeze amene Mulungu anawapatsa. 3 Iwo ankayimba nyimbo ya Mose, mtumiki wa Mulungu, ndi nyimbo ya Mwana Wankhosa. Nyimbo yake inkati,
“Zochita zanu ndi zazikulu ndi zodabwitsa,
Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse
Njira zanu ndi zachilungamo ndi zoona,
Mfumu ya mitundu yonse.
4 Inu Ambuye, ndani angapande kukuopani,
ndi kulemekeza dzina lanu?
Pakuti Inu nokha ndiye woyera.
Anthu a mitundu yonse adzabwera
kudzapembedza pamaso panu,
pakuti ntchito zanu zolungama zaonekera poyera.”
5 Zitatha izi, ndinaona kumwamba Nyumba ya Mulungu imene ndi Tenti ya Umboni, atatsekula. 6 Mʼnyumbamo munatuluka angelo asanu ndi awiri ndi miliri isanu ndi iwiri. Angelowo anavala nsalu zoyera bwino zonyezimira ndi malamba agolide pa zifuwa zawo. 7 Ndipo kenaka chimodzi cha zamoyo zinayi zija chinapereka kwa angelo asanu ndi awiri mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi ukali wa Mulungu amene ali ndi moyo mpaka muyaya. 8 Ndipo Nyumba ya Mulungu inadzaza ndi utsi wochokera ku ulemerero wa Mulungu ndi ku mphamvu zake, ndipo panalibe yemwe akanalowa mʼNyumbayo mpaka miliri isanu ndi iwiri ya angelo asanu ndi awiri aja itatha.
启示录 15
Chinese Contemporary Bible (Simplified)
摩西的歌和羔羊的歌
15 我看见天上又有一个宏大奇异的景象,有七位天使掌管着最后的七种灾祸,上帝要借这些灾祸发尽祂的烈怒。 2 我看见一个好像夹杂着火的玻璃海,玻璃海上站着那些战胜怪兽、兽像及兽名代号的人。他们手里拿着上帝所赐的竖琴, 3 口里唱着上帝的奴仆摩西的歌和羔羊的歌:
“全能的主上帝啊,
你的作为伟大奇妙!
万国的王啊,
你的道路公义真实!
4 主啊,谁敢不敬畏你,
不尊崇你的名呢?
因为只有你是圣洁的,
万民都必到你面前敬拜你,
因为你公义的作为已经彰显出来了。”
天使降七灾
5 这事之后,我看见天上存放约柜的圣殿打开了。 6 那掌管七种灾祸的七位天使都从殿中出来,身穿洁白发光的细麻布衣服,胸佩金带。 7 四个活物中的一个将七只金碗分别交给七位天使,碗中盛满了永活上帝的烈怒。 8 殿里因为上帝的荣耀和权能而烟雾弥漫,人们必须等到七位天使将七样灾祸降完,才能进入圣殿。
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Chinese Contemporary Bible Copyright © 1979, 2005, 2007, 2011 by Biblica® Used by permission. All rights reserved worldwide.