Aroma 3
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kukhulupirika kwa Mulungu
3 Nanga kodi pali ubwino wotani pokhala Myuda, kapena muli ubwino wanjinso mu mdulidwe? 2 Ubwino wake ndi wambiri mʼnjira zonse! Choyambirira iwo anapatsidwa Mawu a Mulungu kuti awasunge.
3 Nanga zili bwanji ngati ena analibe chikhulupiriro? Kodi kupanda chikhulupiriro kwawo kukanalepheretsa kukhulupirika kwa Mulungu? 4 Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Mulungu akhale woona, ndi munthu aliyense akhale wonama. Monga kwalembedwa kuti,
“Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula
ndi kupambana pamene muweruza.”
5 Koma ngati kuyipa mtima kwathu kuonetsa poyera kuti Mulungu ndi wolungama, ife tinganene chiyani? Kodi tinganene kuti Mulungu ndi wosalungama pamene aonetsa mkwiyo wake pa ife? (Ine ndikuyankhula monga mmene anthu ena amayankhulira). 6 Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ngati zikanakhala zotero, kodi Mulungu akanaweruza bwanji dziko lapansi? 7 Wina atanena kuti, “Ngati kunama kwanga kukuonetsa koposa kuti Mulungu ndi woona, ndi kuwonjezera pa ulemerero wake, nanga nʼchifukwa chiyani ndikuweruzidwa kuti ndine wochimwa?” 8 Nʼchifukwa chiyani osanena kuti, monga ena amanena mosasamala kuti, “Tiyeni tichite zoyipa kuti zabwino zionekere?” Anthu onena zoterewa kulangidwa kwawo ndi koyenera.
Palibe Munthu Wolungama
9 Kodi timalize bwanji? Kodi Ayuda ndife oposa anthu ena? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Ife tinanena kale kuti Ayuda ndi a mitundu ina omwe ndi ochimwa. 10 Monga kwalembedwa kuti,
“Palibe munthu wolungama, inde palibe ndi mmodzi yemwe.
11 Palibe ndi mmodzi yemwe amene amazindikira,
palibe amene amafunafuna Mulungu.
12 Onse apatukira kumbali,
onse pamodzi asanduka opandapake.
Palibe ndi mmodzi yemwe amene amachita zabwino,
palibe ngakhale mmodzi.”
13 “Kummero kwawo kuli ngati manda apululu;
ndi lilime lawo amayankhula zachinyengo.”
“Ululu wa mamba uli pa milomo yawo.”
14 “Mʼkamwa mwawo ndi modzaza ndi zotemberera ndi mawu owawa.”
15 “Mapazi awo afulumira kukakhetsa magazi.
16 Kusakaza ndi chisoni kumaonekera mʼnjira zawo,
17 ndipo njira ya mtendere sayidziwa.”
18 “Saopa Mulungu ndi pangʼono pomwe.”
19 Tsopano tikudziwa kuti chilichonse Malamulo amanena, amanena kwa amene amalamulidwa ndi Malamulowo, ndi cholinga chakuti aliyense asowe chonena, ndipo dziko lonse lidzayimbidwa mlandu ndi Mulungu. 20 Chifukwa chake palibe mmodzi amene adzayesedwa wolungama pamaso pake chifukwa chosunga Malamulo, kuti ife timazindikira tchimo kupyolera mu Malamulo.
Kulungama Mwachikhulupiriro
21 Koma tsopano chilungamo chochokera kwa Mulungu, osati chochokera ku Malamulo, chaonetsedwa. Ichi ndi chimene Malamulo ndi Aneneri amachitira umboni. 22 Timakhala olungama pamaso pa Mulungu pamene takhulupirira Yesu Khristu. Mulungu amachitira zimenezi anthu onse amene akhulupirira Khristu. Palibe kusiyana pakati pa Myuda ndi a mitundu ina, 23 pakuti onse anachimwa naperewera pa ulemerero wa Mulungu 24 ndipo onse alungamitsidwa mwaulere mwa chisomo chake chifukwa cha Khristu Yesu amene anawawombola. 25 Mulungu anamupereka Iyeyu kuti pokhetsa magazi ake, akhale nsembe yokhululukira machimo. Mulungu anachita zimenezi kufuna kuonetsa chilungamo chake. Chifukwa cha kuleza mtima kwake, sanalange anthu chifukwa cha machimo amene anachita kale. 26 Iye anachita izi kuti aonetse chilungamo chake lero lino. Anthu azindikire kuti Iye ndi wolungama ndipo amalungamitsa aliyense amene akhulupirira Yesu.
27 Nanga tsono pamenepa munthu anganyadenso? Kunyadatu kwachotsedwa. Chifukwa cha Malamulo? Kodi Malamulo samafuna ntchito za munthu? Ayi, koma mwachikhulupiriro. 28 Ife tikunenabe kuti munthu amalungamitsidwa mwachikhulupiriro osati mwakusunga Malamulo. 29 Kodi Mulungu ndi Mulungu wa Ayuda okha? Kodi si Mulungu wa a mitundu inanso? Inde wa a mitundu inanso, 30 popeza ndi Mulungu mmodzi yemweyo amene adzalungamitsa mwachikhulupiriro ochita mdulidwe ndi osachita mdulidwe kudzera mʼchikhulupiriro chomwecho. 31 Kodi tsono ife, tikutaya Malamulo pamene tikunena kuti pafunika chikhulupiriro? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi! Komatu ife tikukwaniritsadi Malamulo.
Romans 3
New King James Version
God’s Judgment Defended
3 What advantage then has the Jew, or what is the profit of circumcision? 2 Much in every way! Chiefly because (A)to them were committed the [a]oracles of God. 3 For what if (B)some did not believe? (C)Will their unbelief make the faithfulness of God without effect? 4 (D)Certainly not! Indeed, let (E)God be [b]true but (F)every man a liar. As it is written:
(G)“That You may be justified in Your words,
And may overcome when You are judged.”
5 But if our unrighteousness demonstrates the righteousness of God, what shall we say? Is God unjust who inflicts wrath? (H)(I speak as a man.) 6 Certainly not! For then (I)how will God judge the world?
7 For if the truth of God has increased through my lie to His glory, why am I also still judged as a sinner? 8 And why not say, (J)“Let us do evil that good may come”?—as we are slanderously reported and as some affirm that we say. Their [c]condemnation is just.
All Have Sinned(K)
9 What then? Are we better than they? Not at all. For we have previously charged both Jews and Greeks that (L)they are all under sin.
10 As it is written:
(M)“There is none righteous, no, not one;
11 There is none who understands;
There is none who seeks after God.
12 They have all turned aside;
They have together become unprofitable;
There is none who does good, no, not one.”
13 “Their(N) throat is an open [d]tomb;
With their tongues they have practiced deceit”;
(O)“The poison of asps is under their lips”;
14 “Whose(P) mouth is full of cursing and bitterness.”
15 “Their(Q) feet are swift to shed blood;
16 Destruction and misery are in their ways;
17 And the way of peace they have not known.”
18 “There(R) is no fear of God before their eyes.”
19 Now we know that whatever (S)the law says, it says to those who are under the law, that (T)every mouth may be stopped, and all the world may become [e]guilty before God. 20 Therefore (U)by the deeds of the law no flesh will be justified in His sight, for by the law is the knowledge of sin.
God’s Righteousness Through Faith
21 But now (V)the righteousness of God apart from the law is revealed, (W)being witnessed by the Law (X)and the Prophets, 22 even the righteousness of God, through faith in Jesus Christ, to all [f]and on all who believe. For (Y)there is no difference; 23 for (Z)all have sinned and fall short of the glory of God, 24 being justified [g]freely (AA)by His grace (AB)through the redemption that is in Christ Jesus, 25 whom God set forth (AC)as a [h]propitiation (AD)by His blood, through faith, to demonstrate His righteousness, because in His forbearance God had passed over (AE)the sins that were previously committed, 26 to demonstrate at the present time His righteousness, that He might be just and the justifier of the one who has faith in Jesus.
Boasting Excluded
27 (AF)Where is boasting then? It is excluded. By what law? Of works? No, but by the law of faith. 28 Therefore we conclude (AG)that a man is [i]justified by faith apart from the deeds of the law. 29 Or is He the God of the Jews only? Is He not also the God of the Gentiles? Yes, of the Gentiles also, 30 since (AH)there is one God who will justify the circumcised by faith and the uncircumcised through faith. 31 Do we then make void the law through faith? Certainly not! On the contrary, we establish the law.
Footnotes
- Romans 3:2 sayings, Scriptures
- Romans 3:4 Found true
- Romans 3:8 Lit. judgment
- Romans 3:13 grave
- Romans 3:19 accountable
- Romans 3:22 NU omits and on all
- Romans 3:24 without any cost
- Romans 3:25 mercy seat
- Romans 3:28 declared righteous
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Scripture taken from the New King James Version®. Copyright © 1982 by Thomas Nelson. Used by permission. All rights reserved.