Add parallel Print Page Options

Moyo Watsopano

Tsono popeza munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, ikani mitima yanu pa zinthu za kumwamba, kumene Khristu akukhala ku dzanja lamanja la Mulungu. Muzifunafuna zinthu za kumwamba, osati zinthu za pa dziko lapansi. Pakuti munafa, ndipo moyo wanu tsopano wabisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu. Khristu, amene ndiye moyo wanu, akadzaonekanso, pamenepo inunso mudzaoneka naye pamodzi mu ulemerero.

Choncho, iphani zilakolako za dziko lapansi mwa inu, monga: dama, zodetsa, kulakalaka zosayenera, kukhumba zoyipa ndi umbombo, pakuti umbombo ndiko kupembedza mafano. Chifukwa cha zimenezi, mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa ana osamvera. Inunso kale munkachita zomwezi, mʼmoyo wanu wakale uja. Koma tsopano mukuyenera kuzichotsa zinthu zonsezi monga: mkwiyo, ukali, dumbo, chipongwe ndi mawu onyansa. Musanamizane wina ndi mnzake, popeza munavula munthu wakale pamodzi ndi zochita zake 10 ndipo mwavala munthu watsopano, amene nzeru zake zikukonzedwanso kuti afanane ndi Mlengi wake. 11 Pano palibe kusiyana pakati pa Mgriki ndi Myuda, wochita mdulidwe ndi wosachita, wosaphunzira kapena wosachangamuka, kapolo kapena mfulu, koma Khristu yekha basi ndipo amakhala mwa onse.

12 Choncho, ngati anthu osankhidwa ndi Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa kwambiri, muvale chifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, kufatsa ndi kupirira. 13 Mulezerane mtima ndipo muzikhululukirana ngati wina ali ndi chifukwa ndi mnzake. Muzikhululukirana monga Ambuye anakhululukira inu. 14 Ndipo kuwonjezera pa zonsezi valani chikondi, chimene chimangirira zonsezi pamodzi mu mgwirizano wangwiro.

15 Mtendere wa Khristu ulamulire mʼmitima mwanu, popeza monga ziwalo za thupi limodzi, munayitanidwa kuti mukhale ndi mtendere. Ndipo muziyamika. 16 Mawu a Khristu akhazikike kwathunthu mʼmitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana wina ndi mnzake ndi nzeru zonse pamene mukuyimba Masalimo, nyimbo zotamanda ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira Mulungu ndi mitima yoyamika. 17 Ndipo chilichonse chimene mungachite, kaya nʼkuyankhula, kaya nʼkugwira ntchito, muchite zonse mʼdzina la Ambuye Yesu, kuyamika kwa Mulungu Atate kudzera mwa Iye.

Malangizo a Moyo wa Mʼbanja la Chikhristu

18 Inu akazi, gonjerani amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.

19 Inu amuna, kondani akazi anu ndipo musawapsere mtima.

20 Inu ana, mverani makolo anu mu zonse pakuti izi zimakondweretsa Ambuye.

21 Inu abambo, musakwiyitse ana anu, kuti angataye mtima.

22 Inu antchito, mverani mabwana anu mu zonse, ndipo muzichita zimenezi osati nthawi yokhayo imene akukuonani kuti akukondeni, koma muzichite moona mtima ndi mopereka ulemu kwa Ambuye. 23 Chilichonse mungachite, muchite ndi mtima wanu onse, monga mmene mungagwirire ntchito ya Ambuye osati ya anthu. 24 Inu mukudziwa kuti mudzalandira mphotho monga cholowa kuchokera kwa Ambuye. Ndi Ambuye Khristu amene mukumutumikira. 25 Aliyense amene amachita zolakwa adzalandira malipiro molingana ndi kulakwa kwake, ndipo palibe tsankho.

Living as Those Made Alive in Christ

Since, then, you have been raised with Christ,(A) set your hearts on things above, where Christ is, seated at the right hand of God.(B) Set your minds on things above, not on earthly things.(C) For you died,(D) and your life is now hidden with Christ in God. When Christ, who is your[a] life,(E) appears,(F) then you also will appear with him in glory.(G)

Put to death,(H) therefore, whatever belongs to your earthly nature:(I) sexual immorality,(J) impurity, lust, evil desires and greed,(K) which is idolatry.(L) Because of these, the wrath of God(M) is coming.[b] You used to walk in these ways, in the life you once lived.(N) But now you must also rid yourselves(O) of all such things as these: anger, rage, malice, slander,(P) and filthy language from your lips.(Q) Do not lie to each other,(R) since you have taken off your old self(S) with its practices 10 and have put on the new self,(T) which is being renewed(U) in knowledge in the image of its Creator.(V) 11 Here there is no Gentile or Jew,(W) circumcised or uncircumcised,(X) barbarian, Scythian, slave or free,(Y) but Christ is all,(Z) and is in all.

12 Therefore, as God’s chosen people, holy and dearly loved, clothe yourselves(AA) with compassion, kindness, humility,(AB) gentleness and patience.(AC) 13 Bear with each other(AD) and forgive one another if any of you has a grievance against someone. Forgive as the Lord forgave you.(AE) 14 And over all these virtues put on love,(AF) which binds them all together in perfect unity.(AG)

15 Let the peace of Christ(AH) rule in your hearts, since as members of one body(AI) you were called to peace.(AJ) And be thankful. 16 Let the message of Christ(AK) dwell among you richly as you teach and admonish one another with all wisdom(AL) through psalms,(AM) hymns, and songs from the Spirit, singing to God with gratitude in your hearts.(AN) 17 And whatever you do,(AO) whether in word or deed, do it all in the name of the Lord Jesus, giving thanks(AP) to God the Father through him.

Instructions for Christian Households(AQ)

18 Wives, submit yourselves to your husbands,(AR) as is fitting in the Lord.

19 Husbands, love your wives and do not be harsh with them.

20 Children, obey your parents in everything, for this pleases the Lord.

21 Fathers,[c] do not embitter your children, or they will become discouraged.

22 Slaves, obey your earthly masters in everything; and do it, not only when their eye is on you and to curry their favor, but with sincerity of heart and reverence for the Lord. 23 Whatever you do, work at it with all your heart, as working for the Lord, not for human masters, 24 since you know that you will receive an inheritance(AS) from the Lord as a reward.(AT) It is the Lord Christ you are serving. 25 Anyone who does wrong will be repaid for their wrongs, and there is no favoritism.(AU)

Footnotes

  1. Colossians 3:4 Some manuscripts our
  2. Colossians 3:6 Some early manuscripts coming on those who are disobedient
  3. Colossians 3:21 Or Parents