Add parallel Print Page Options

Ndikufuna mudziwe kuti ndikukuvutikirani kwambiri, inuyo pamodzi ndi anzanu a ku Laodikaya, ndi ena onse amene sitinaonane maso ndi maso. Cholinga changa nʼchakuti alimbikitsidwe ndi kuyanjana pamodzi mʼchikondi, akhale odzaza ndi nzeru zomvetsa zinthu, ndi kuti azindikire chinsinsi cha Mulungu, chimene ndi Khristu. Mwa Iyeyu muli chuma chonse chobisidwa cha nzeru ndi chidziwitso. Ndikukuwuzani zimenezi kuti wina aliyense asakunamizeni ndi kukukopani ndi mawu ake. Pakuti ngakhale sindili pakati panu mʼthupi, ndili nanu pamodzi mu mzimu, ndipo ndikukondwa kuona kuti mukulongosola bwino zonse ndiponso kuti chikhulupiriro chanu mwa Khristu ndi chokhazikika ndithu.

Za Moyo Weniweni mwa Khristu

Tsono popeza munavomereza Khristu Yesu kukhala Ambuye anu, mupitirire kukhala mwa Iyeyo. Mukhale ozikika mizu mwa Iye, ndipo moyo wanu umangike pa Iye. Mulimbike mʼchikhulupiriro monga momwe munaphunzirira, ndipo kuyamika kwanu kusefukire.

Musalole kuti wina aliyense akutengeni ukapolo ndi mʼnzeru zachinyengo zolongosola zinthu zozama, zomwe zimachokera ku miyambo ya anthu ndi ku maganizo awo okhudza za dziko lapansi osati kwa Khristu.

Pakuti mʼthupi la Khristu mumakhala umulungu wonse wathunthu. 10 Ndipo inunso ndinu athunthu mwa Khristu. Iye ndiye mtsogoleri wa pamwamba pa maufumu onse ndi maulamuliro wonse. 11 Mwa Iye inunso munachita mdulidwe mʼthupi lanu, osati mdulidwe ochitidwa ndi manja a anthu ayi, koma ochitidwa ndi Khristu pamene anavula khalidwe lanu lauchimo lija. 12 Mu ubatizo, munayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Khristu ndi kuukitsidwa naye pamodzi, pokhulupirira mphamvu za Mulungu amene anamuukitsa kwa akufa.

13 Pamene munali akufa chifukwa cha machimo anu ndi osachita mdulidwe mʼmitima mwanu, Mulungu anakupatsani moyo mwa Khristu. Iye anatikhululukira machimo athu onse. 14 Anafafaniza kalata ya ngongole yathu, pomwe panali milandu yotitsutsa ife. Iye anayichotsa, nayikhomera pa mtanda. 15 Ndipo atalanda zida maufumu ndi maulamuliro, Iye anawachititsa manyazi powayendetsa pamaso pa anthu onse atawagonjetsa ndi mtanda.

Ufulu Wathu

16 Nʼchifukwa chake musalole wina aliyense kukuzengani mlandu chifukwa cha zimene mumadya kapena kumwa, kapena za masiku achikondwerero cha chipembedzo, za chikondwerero cha mwezi watsopano, kapena za tsiku la Sabata. 17 Zimenezi ndi chithunzithunzi chabe cha zinthu zimene zikubwera, koma choonadi chenicheni chikupezeka mwa Khristu. 18 Musalole kuti wina aliyense amene amakonda kudzichepetsa mwachiphamaso ndi kumapembedza angelo akulepheretseni kukalandira mphotho. Munthu woteroyu amayankhulanso mwatsatanetsatane zinthu zimene akuti anaziona mʼmasomphenya. Anthuwa ndi odzitukumula ndi fundo zopanda pake zochokera mʼmaganizo mwawo amene si auzimu. 19 Iwo sakulumikizananso ndi mutu, kumene kumachokera thupi lonse, logwirizidwa ndi kumangiriridwa pamodzi ndi mʼmitsempha yake ndi mnofu, limene limakula monga mmene Mulungu afunira kuti likulire.

20 Popeza munafa pamodzi ndi Khristu kusiyana nayo miyambo ya dziko lapansi lino, nʼchifukwa chiyani mukukhalanso ngati a dziko lapansi lino? Bwanji mukumvera malamulo monga awa: 21 “Usagwire chakuti,” “Usalawe chakuti,” “Usakhudze chakuti?” 22 Malamulo amenewa amakhudza zinthu zimene zimatha zikamagwiritsidwa ntchito, ndipo malamulo ndi zophunzitsa za anthu chabe. 23 Ndithu malamulo oterewa amaoneka ngati anzeru, pakuti amalamulira anthu ambiri pa zachipembedzo ndi pa zakudzichepetsa kwa chiphamaso, ndi pa zakuzunza thupi lawo, koma alibe mphamvu zoletsa kuchita zofuna za thupilo.

I want you to know how hard I am contending(A) for you and for those at Laodicea,(B) and for all who have not met me personally. My goal is that they may be encouraged in heart(C) and united in love, so that they may have the full riches of complete understanding, in order that they may know the mystery(D) of God, namely, Christ, in whom are hidden all the treasures of wisdom and knowledge.(E) I tell you this so that no one may deceive you by fine-sounding arguments.(F) For though I am absent from you in body, I am present with you in spirit(G) and delight to see how disciplined(H) you are and how firm(I) your faith in Christ(J) is.

Spiritual Fullness in Christ

So then, just as you received Christ Jesus as Lord,(K) continue to live your lives in him, rooted(L) and built up in him, strengthened in the faith as you were taught,(M) and overflowing with thankfulness.

See to it that no one takes you captive through hollow and deceptive philosophy,(N) which depends on human tradition and the elemental spiritual forces[a] of this world(O) rather than on Christ.

For in Christ all the fullness(P) of the Deity lives in bodily form, 10 and in Christ you have been brought to fullness. He is the head(Q) over every power and authority.(R) 11 In him you were also circumcised(S) with a circumcision not performed by human hands. Your whole self ruled by the flesh[b](T) was put off when you were circumcised by[c] Christ, 12 having been buried with him in baptism,(U) in which you were also raised with him(V) through your faith in the working of God, who raised him from the dead.(W)

13 When you were dead in your sins(X) and in the uncircumcision of your flesh, God made you[d] alive(Y) with Christ. He forgave us all our sins,(Z) 14 having canceled the charge of our legal indebtedness,(AA) which stood against us and condemned us; he has taken it away, nailing it to the cross.(AB) 15 And having disarmed the powers and authorities,(AC) he made a public spectacle of them, triumphing over them(AD) by the cross.[e]

Freedom From Human Rules

16 Therefore do not let anyone judge you(AE) by what you eat or drink,(AF) or with regard to a religious festival,(AG) a New Moon celebration(AH) or a Sabbath day.(AI) 17 These are a shadow of the things that were to come;(AJ) the reality, however, is found in Christ. 18 Do not let anyone who delights in false humility(AK) and the worship of angels disqualify you.(AL) Such a person also goes into great detail about what they have seen; they are puffed up with idle notions by their unspiritual mind. 19 They have lost connection with the head,(AM) from whom the whole body,(AN) supported and held together by its ligaments and sinews, grows as God causes it to grow.(AO)

20 Since you died with Christ(AP) to the elemental spiritual forces of this world,(AQ) why, as though you still belonged to the world, do you submit to its rules:(AR) 21 “Do not handle! Do not taste! Do not touch!”? 22 These rules, which have to do with things that are all destined to perish(AS) with use, are based on merely human commands and teachings.(AT) 23 Such regulations indeed have an appearance of wisdom, with their self-imposed worship, their false humility(AU) and their harsh treatment of the body, but they lack any value in restraining sensual indulgence.

Footnotes

  1. Colossians 2:8 Or the basic principles; also in verse 20
  2. Colossians 2:11 In contexts like this, the Greek word for flesh (sarx) refers to the sinful state of human beings, often presented as a power in opposition to the Spirit; also in verse 13.
  3. Colossians 2:11 Or put off in the circumcision of
  4. Colossians 2:13 Some manuscripts us
  5. Colossians 2:15 Or them in him