Afilipi 1
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
1 Paulo ndi Timoteyo, atumiki a Khristu Yesu.
Kulembera anthu onse oyera mtima a ku Filipi amene ali mwa Khristu Yesu, pamodzi ndi oyangʼanira ndi atumiki awo.
2 Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale kwa inu.
Kuyamika ndi Pemphero
3 Ndimayamika Mulungu wanga nthawi zonse ndikakumbukira inu. 4 Mʼmapemphero anga onse opempherera inu, nthawi zonse ndimapemphera ndi chimwemwe 5 chifukwa mwakhala mukundithandiza polalikira Uthenga Wabwino kuyambira tsiku loyamba mpaka tsopano. 6 Sindikukayika konse kuti Iye amene anayamba ntchito yabwino mwa inu adzayipitiriza ndi kuyimaliza mpaka pa tsiku la kubweranso kwa Khristu Yesu.
7 Kwa ine ndi bwino kuti ndiziganiza zotere za nonsenu, popeza ndimakukondani, ngakhale ndikhale mʼndende, kapena pamene ndikuteteza ndi kukhazikitsa Uthenga Wabwino, inu nonse mumagawana nane chisomo cha Mulungu. 8 Mulungu angandichitire umboni kuti ndimakulakalakani ndi chikondi cha Khristu Yesu.
9 Ndipo pemphero langa ndi lakuti chikondi chanu chipitirire kukulirakulira pa chidziwitso ndi kuzama mʼmaganizo, 10 kuti mukhoza kuzindikira chabwino koposa zonse ndi chiti kuti muthe kukhala wopanda chodetsa ndi wopanda chilema kufikira tsiku la Khristu. 11 Ndipo moyo wanu udzakhala odzazidwa ndi chipatso cha chilungamo chimene chimachokera mwa Yesu Khristu. Pakuti zimenezi zidzapereka ulemerero ndi matamando kwa Mulungu.
Maunyolo a Paulo Apititsa Mʼtsogolo Uthenga Wabwino
12 Tsopano abale, ndikufuna mudziwe kuti chimene chandichitikira ine chathandiza kwambiri kupititsa patsogolo Uthenga Wabwino. 13 Chotsatira chake nʼchakuti zadziwika bwino lomwe kwa onse amene ali ku nyumba yaufumu kuti ine ndili mʼmaunyolo chifukwa cha Khristu. 14 Moti chifukwa cha maunyolo angawa, abale ambiri alimbikitsidwa kuyankhula Mawu a Mulungu molimbika ndi mopanda mantha.
15 Nʼzoonadi kuti ena amalalikira Khristu chifukwa cha kaduka ndi mikangano, koma ena chifukwa cha zolinga zabwino. 16 Olalikira ndi zolinga zabwinowa amachita izi mwachikondi, podziwa kuti ine ndili muno chifukwa cha kuteteza Uthenga Wabwino. 17 Ena aja amalalikira Khristu modzikonda osati moona mtima namaganiza kuti kutero kubweretsa mavuto pamene ndili mʼmaunyolo. 18 Nanga kodi zimenezo zili ndi ntchito? Chofunika ndi chakuti Khristu alalikidwe, kaya ndi mwachinyengo kapena moona. Ndipo ndikukondwera chifukwa cha chimenechi.
Ndithu, ndidzapitirira kukondwera, 19 pakuti ndikudziwa kuti chifukwa cha mapemphero anu ndi thandizo lochokera kwa Mzimu wa Yesu Khristu, zimene zandionekera zidzathandiza kuti ndimasulidwe. 20 Ndili ndi chiyembekezo chonse kuti sindidzachita manyazi ndi pangʼono pomwe, koma ndidzakhala ndi chilimbikitso chokwanira kuti monga mwa nthawi zonse, tsopano Khristu adzakwezedwa mʼthupi langa kaya ndi mʼmoyo kapena mu imfa. 21 Pakuti kwa ine kukhala moyo ndi Khristu ndipo kufa ndi phindu. 22 Ngati nditi ndipitirire kukhala ndi moyo mʼthupi ndiye kuti kwa ine ndi kugwira ntchito yopindulitsa. Kodi ndisankhe chiyani? Sindikudziwa. 23 Ndathinidwa ndi zinthu ziwirizi: Ndikulakalaka kunyamuka kuti ndikakhale ndi Khristu, chimene ndi chinthu chabwino kwambiri. 24 Komanso nʼkofunika kwambiri kuti ndikhalebe mʼthupi chifukwa cha inu. 25 Ndili ndi chitsimikizo, ndikudziwa kuti ndidzakhala ndi moyo ndipo ndidzapitirira nanu kuti nonse mupite mʼtsogolo ndi kukhala ndi chimwemwe mu chikhulupiriro 26 kuti pokhala nanunso, kudzitamandira kwanu mwa Khristu Yesu kudzasefukire chifukwa cha ine.
Moyo Woyenerana ndi Uthenga Wabwino
27 Chilichonse chimene chingachitike, chachikulu nʼchakuti mukhale moyo ofanana ndi Uthenga Wabwino wa Khristu. Tsono ngati ndingabwere kudzakuonani kapena kumangomva za inu ndili kutali, ndidzadziwa kuti mwayima mwamphamvu mwa Mzimu mmodzi, kulimbika pamodzi ngati munthu mmodzi chifukwa cha chikhulupiriro cha Uthenga Wabwino 28 osachita mantha ndi pangʼono pomwe ndi amene akutsutsana nanu. Ichi ndi chizindikiro kwa iwo kuti adzawonongedwa, koma inu mudzapulumutsidwa ndi Mulungu. 29 Pakuti inu mwapatsidwa mwayi osati ongokhulupirira Khristu kokha, koma wakumva zowawa mʼmalo mwa Khristu. 30 Inunso mukudutsa mʼzowawa zomwe zija munaona ndikudutsamo inenso ndipo pano mukumva kuti ndikukumana nazobe.
Philippians 1
English Standard Version
Greeting
1 Paul and Timothy, servants[a] of Christ Jesus,
To all the (A)saints in Christ Jesus who are at Philippi, with the (B)overseers[b] and (C)deacons:[c]
2 (D)Grace to you and peace from God our Father and the Lord Jesus Christ.
Thanksgiving and Prayer
3 (E)I thank my God (F)in all my remembrance of you, 4 always in every prayer of mine for you all making my prayer with joy, 5 (G)because of your partnership in the gospel from the first day until now. 6 And I am sure of this, that he who began (H)a good work in you (I)will bring it to completion at (J)the day of Jesus Christ. 7 It is right for me to feel this way about you all, because I hold you (K)in my heart, for you are all (L)partakers with me of grace,[d] both (M)in my imprisonment and in (N)the defense and confirmation of the gospel. 8 For (O)God is my witness, (P)how I yearn for you all with the affection of Christ Jesus. 9 And it is my prayer that (Q)your love may abound more and more, (R)with knowledge and all discernment, 10 so that you may approve what is excellent, (S)and so be pure and blameless (T)for the day of Christ, 11 filled (U)with the fruit of righteousness that comes (V)through Jesus Christ, (W)to the glory and praise of God.
The Advance of the Gospel
12 I want you to know, brothers,[e] that what has happened to me has really (X)served to advance the gospel, 13 so that it has become known throughout the whole imperial guard[f] and (Y)to all the rest that (Z)my imprisonment is for Christ. 14 And most of the brothers, having become confident in the Lord by my imprisonment, are much more bold (AA)to speak the word[g] without fear.
15 (AB)Some indeed preach Christ from envy and rivalry, but others from good will. 16 The latter do it out of love, (AC)knowing that I am put here for (AD)the defense of the gospel. 17 The former proclaim Christ (AE)out of selfish ambition, not sincerely but thinking to afflict me in my imprisonment. 18 What then? Only that in every way, whether in pretense or in truth, Christ is proclaimed, and in that I rejoice.
To Live Is Christ
Yes, and I will rejoice, 19 for I know that (AF)through your prayers and (AG)the help of (AH)the Spirit of Jesus Christ this will turn out for my deliverance, 20 as it is my eager expectation and hope (AI)that I will not be at all ashamed, but that with full (AJ)courage now as always Christ (AK)will be honored in my body, (AL)whether by life or by death. 21 For to me (AM)to live is Christ, and to die is gain. 22 If I am to live in the flesh, that means fruitful labor for me. Yet which I shall choose I cannot tell. 23 (AN)I am hard pressed between the two. My desire is (AO)to depart and (AP)be with Christ, for that is far better. 24 But to remain in the flesh is more necessary on your account. 25 (AQ)Convinced of this, (AR)I know that I will remain and continue with you all, for your (AS)progress and (AT)joy in the faith, 26 so that in me (AU)you may have ample cause to glory in Christ Jesus, because of my coming to you again.
27 Only (AV)let your manner of life be (AW)worthy[h] of the gospel of Christ, so that whether I come and see you or am absent, I may hear of you (AX)that you are standing firm in one spirit, with (AY)one mind (AZ)striving side by side for the faith of the gospel, 28 and not frightened in anything by your opponents. This is (BA)a clear sign to them of their destruction, but (BB)of your salvation, and that from God. 29 For (BC)it has been granted to you that for the sake of Christ you should not only believe in him but also (BD)suffer for his sake, 30 engaged in the same (BE)conflict that (BF)you saw I had and now hear that I still have.
Footnotes
- Philippians 1:1 For the contextual rendering of the Greek word doulos, see Preface
- Philippians 1:1 Or bishops; Greek episkopoi
- Philippians 1:1 Or servants, or ministers; Greek diakonoi
- Philippians 1:7 Or you all have fellowship with me in grace
- Philippians 1:12 Or brothers and sisters. In New Testament usage, depending on the context, the plural Greek word adelphoi (translated “brothers”) may refer either to brothers or to brothers and sisters; also verse 14
- Philippians 1:13 Greek in the whole praetorium
- Philippians 1:14 Some manuscripts add of God
- Philippians 1:27 Greek Only behave as citizens worthy
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
The ESV® Bible (The Holy Bible, English Standard Version®), © 2001 by Crossway, a publishing ministry of Good News Publishers. ESV Text Edition: 2025.
