Add parallel Print Page Options

Kupambana kwa Davide pa Nkhondo

Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.

Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.

Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate. Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.

Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000. Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.

Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu. Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.

Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri, 10 anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.

11 Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa: 12 Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.

13 Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.

14 Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.

Akuluakulu a Davide

15 Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse. 16 Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika. 17 Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi; 18 Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.

David’s Victories(A)

In the course of time, David defeated the Philistines(B) and subdued(C) them, and he took Metheg Ammah from the control of the Philistines.

David also defeated the Moabites.(D) He made them lie down on the ground and measured them off with a length of cord. Every two lengths of them were put to death, and the third length was allowed to live. So the Moabites became subject to David and brought him tribute.(E)

Moreover, David defeated Hadadezer(F) son of Rehob, king of Zobah,(G) when he went to restore his monument at[a] the Euphrates(H) River. David captured a thousand of his chariots, seven thousand charioteers[b] and twenty thousand foot soldiers. He hamstrung(I) all but a hundred of the chariot horses.

When the Arameans of Damascus(J) came to help Hadadezer king of Zobah, David struck down twenty-two thousand of them. He put garrisons(K) in the Aramean kingdom of Damascus, and the Arameans became subject(L) to him and brought tribute. The Lord gave David victory wherever he went.(M)

David took the gold shields(N) that belonged to the officers of Hadadezer and brought them to Jerusalem. From Tebah[c] and Berothai,(O) towns that belonged to Hadadezer, King David took a great quantity of bronze.

When Tou[d] king of Hamath(P) heard that David had defeated the entire army of Hadadezer,(Q) 10 he sent his son Joram[e] to King David to greet him and congratulate him on his victory in battle over Hadadezer, who had been at war with Tou. Joram brought with him articles of silver, of gold and of bronze.

11 King David dedicated(R) these articles to the Lord, as he had done with the silver and gold from all the nations he had subdued: 12 Edom[f](S) and Moab,(T) the Ammonites(U) and the Philistines,(V) and Amalek.(W) He also dedicated the plunder taken from Hadadezer son of Rehob, king of Zobah.

13 And David became famous(X) after he returned from striking down eighteen thousand Edomites[g] in the Valley of Salt.(Y)

14 He put garrisons throughout Edom, and all the Edomites(Z) became subject to David.(AA) The Lord gave David victory(AB) wherever he went.(AC)

David’s Officials(AD)

15 David reigned over all Israel, doing what was just and right(AE) for all his people. 16 Joab(AF) son of Zeruiah was over the army; Jehoshaphat(AG) son of Ahilud was recorder;(AH) 17 Zadok(AI) son of Ahitub and Ahimelek son of Abiathar(AJ) were priests; Seraiah was secretary;(AK) 18 Benaiah(AL) son of Jehoiada was over the Kerethites(AM) and Pelethites; and David’s sons were priests.[h]

Footnotes

  1. 2 Samuel 8:3 Or his control along
  2. 2 Samuel 8:4 Septuagint (see also Dead Sea Scrolls and 1 Chron. 18:4); Masoretic Text captured seventeen hundred of his charioteers
  3. 2 Samuel 8:8 See some Septuagint manuscripts (see also 1 Chron. 18:8); Hebrew Betah.
  4. 2 Samuel 8:9 Hebrew Toi, a variant of Tou; also in verse 10
  5. 2 Samuel 8:10 A variant of Hadoram
  6. 2 Samuel 8:12 Some Hebrew manuscripts, Septuagint and Syriac (see also 1 Chron. 18:11); most Hebrew manuscripts Aram
  7. 2 Samuel 8:13 A few Hebrew manuscripts, Septuagint and Syriac (see also 1 Chron. 18:12); most Hebrew manuscripts Aram (that is, Arameans)
  8. 2 Samuel 8:18 Or were chief officials (see Septuagint and Targum; see also 1 Chron. 18:17)