Add parallel Print Page Options

Yotamu Mfumu ya Yuda

27 Yotamu anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Dzina la amayi ake linali Yerusa mwana wa Zadoki. Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga anachitira Uziya abambo ake, kupatula kuti iyeyo sanalowe mʼNyumba ya Yehova. Komabe anthu anapitirira kuchita zoyipa. Yotamu anamanganso chipata chakumtunda cha Nyumba ya Yehova ndipo anagwira ntchito yayikulu yomanga khoma la ku phiri la Ofeli. Iye anamanga mizinda mʼmapiri a ku Yuda ndipo anamanganso malinga ndi nsanja mʼmadera a ku nkhalango.

Yotamu anachita nkhondo ndi mfumu ya Aamoni ndipo anawagonjetsa. Chaka chimenecho Aamoni anapereka makilogalamu 3,400, matani 1,000 a tirigu ndiponso matani 1,000 a barele. Aamoni anabweretsa zinthu zomwezi chaka chachiwiri ndi chachitatu.

Yotamu anakula mphamvu chifukwa anayenda molungama pamaso pa Yehova Mulungu wake.

Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Yotamu, kuphatikizapo nkhondo zake zonse ndi zinthu zina zimene anachita, zinalembedwa mʼbuku la mafumu a Israeli ndi Yuda. Iye anakhala mfumu ali ndi zaka 25 ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 16. Yotamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Mzinda wa Davide. Ndipo Ahazi mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

Jotham King of Judah(A)

27 Jotham(B) was twenty-five years old when he became king, and he reigned in Jerusalem sixteen years. His mother’s name was Jerusha daughter of Zadok. He did what was right in the eyes of the Lord, just as his father Uzziah had done, but unlike him he did not enter the temple of the Lord. The people, however, continued their corrupt practices. Jotham rebuilt the Upper Gate of the temple of the Lord and did extensive work on the wall at the hill of Ophel.(C) He built towns in the hill country of Judah and forts and towers in the wooded areas.

Jotham waged war against the king of the Ammonites(D) and conquered them. That year the Ammonites paid him a hundred talents[a] of silver, ten thousand cors[b] of wheat and ten thousand cors[c] of barley. The Ammonites brought him the same amount also in the second and third years.

Jotham grew powerful(E) because he walked steadfastly before the Lord his God.

The other events in Jotham’s reign, including all his wars and the other things he did, are written in the book of the kings of Israel and Judah. He was twenty-five years old when he became king, and he reigned in Jerusalem sixteen years. Jotham rested with his ancestors and was buried in the City of David. And Ahaz his son succeeded him as king.

Footnotes

  1. 2 Chronicles 27:5 That is, about 3 3/4 tons or about 3.4 metric tons
  2. 2 Chronicles 27:5 That is, probably about 1,800 tons or about 1,600 metric tons of wheat
  3. 2 Chronicles 27:5 That is, probably about 1,500 tons or about 1,350 metric tons of barley