2 Akorinto 6
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
6 Pogwira naye ntchito pamodzi, tikukudandaulirani kuti musangolandira chisomo cha Mulungu pachabe. 2 Pakuti akunena kuti,
“Pa nthawi yanga yabwino yokomera anthu mtima ndinakumvera,
ndipo pa nthawi yopulumutsa ndinakuthandiza.
Taonani, ndikukuwuzani kuti, ino ndiyo nthawi yabwino ya Ambuye, lero ndiye tsiku la chipulumutso.”
Masautso a Paulo
3 Ife sitikuyika chokhumudwitsa pa njira ya wina aliyense, kuti utumiki wathu usanyozeke. 4 Mʼmalo mwake, mwanjira iliyonse timasonyeza kuti ndife atumiki a Mulungu popirira kwambiri mʼmasautso, mʼzowawa ndi mʼzodetsa nkhawa. 5 Pomenyedwa, kuponyedwa mʼndende ndi mʼzipolowe. Pogwira ntchito mwamphamvu, posagona usiku onse, posowa chakudya; 6 pokhala moyo woyera mtima, pomvetsa zinthu, wokoma mtima ndi wachifundo mwa Mzimu Woyera ndi mwachikondi choonadi 7 ndi poyankhula choonadi mwamphamvu ya Mulungu. Zida zimene zili mʼdzanja lamanja ndi lamanzere ndizo chilungamo. 8 Timatumikira Mulungu ngakhale ena amatinyoza ndi ena amatilemekeza, ena amatinenera chipongwe, enanso amatiyamikira. Ena amatitenga kukhala ngati onena zoona, ndipo enanso amatitenga kukhala ngati onena zabodza. 9 Amatiyesa osadziwika komatu ndife odziwika kwambiri. Amatiyesa wooneka ngati tikufa, koma tikupitirirabe ndi moyo, okanthidwa, koma osaphedwa. 10 Amatiyesa achisoni, koma ndife achimwemwe nthawi zonse, aumphawi, koma olemeretsa ambiri; wopanda kanthu, koma tili ndi zonse.
11 Tayankhula momasuka kwa inu, Akorinto, ndipo tanena zonse za kumtima kwathu. 12 Ife sitikukubisirani chikondi chathu pa inu, koma inu mukubisa chikondi chanu pa ife. 13 Pofuna kufanana zochita ndi kuyankhula monga kwa ana anga, nanunso muzinena za kukhosi kwanu.
Kukhala Pamodzi ndi Osakhulupirira
14 Musamasenze goli pamodzi ndi osakhulupirira. Kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kulungama ndi kusalungama? Kapena kodi pali mgwirizano wanji pakati pa kuwala ndi mdima? 15 Pali mgwirizano wanji pakati pa Khristu ndi Beliyali? Kapena munthu wokhulupirira angayanjane bwanji ndi munthu wosakhulupirira? 16 Pali mgwirizano wanji pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi nyumba ya mafano? Popezatu ndife Nyumba ya Mulungu wamoyo. Monga Mulungu wanena kuti,
“Ndidzakhala mwa iwo
ndipo ndidzayendayenda pakati pawo,
ndipo ndidzakhala Mulungu wawo,
ndipo adzakhala anthu anga.”
17 Nʼchifukwa chake
“Tulukani pakati pawo
ndi kudzipatula,
akutero Ambuye.
Musakhudze chodetsedwa chilichonse,
ndipo ndidzakulandirani.”
18 Ndipo
“Ndidzakhala Atate anu,
ndipo inu mudzakhala ana anga aamuna ndi aakazi,
akutero Ambuye, Wamphamvuzonse.”
2 Corinthians 6
New International Version
6 As God’s co-workers(A) we urge you not to receive God’s grace in vain.(B) 2 For he says,
I tell you, now is the time of God’s favor, now is the day of salvation.
Paul’s Hardships
3 We put no stumbling block in anyone’s path,(D) so that our ministry will not be discredited. 4 Rather, as servants of God we commend ourselves in every way: in great endurance; in troubles, hardships and distresses; 5 in beatings, imprisonments(E) and riots; in hard work, sleepless nights and hunger;(F) 6 in purity, understanding, patience and kindness; in the Holy Spirit(G) and in sincere love;(H) 7 in truthful speech(I) and in the power of God;(J) with weapons of righteousness(K) in the right hand and in the left; 8 through glory and dishonor,(L) bad report(M) and good report; genuine, yet regarded as impostors;(N) 9 known, yet regarded as unknown; dying,(O) and yet we live on;(P) beaten, and yet not killed; 10 sorrowful, yet always rejoicing;(Q) poor, yet making many rich;(R) having nothing,(S) and yet possessing everything.(T)
11 We have spoken freely to you, Corinthians, and opened wide our hearts to you.(U) 12 We are not withholding our affection from you, but you are withholding yours from us. 13 As a fair exchange—I speak as to my children(V)—open wide your hearts(W) also.
Warning Against Idolatry
14 Do not be yoked together(X) with unbelievers.(Y) For what do righteousness and wickedness have in common? Or what fellowship can light have with darkness?(Z) 15 What harmony is there between Christ and Belial[b]?(AA) Or what does a believer(AB) have in common with an unbeliever?(AC) 16 What agreement is there between the temple of God and idols?(AD) For we are the temple(AE) of the living God.(AF) As God has said:
“I will live with them
and walk among them,
and I will be their God,
and they will be my people.”[c](AG)
17 Therefore,
“Come out from them(AH)
and be separate,
says the Lord.
Touch no unclean thing,
and I will receive you.”[d](AI)
18 And,
Footnotes
- 2 Corinthians 6:2 Isaiah 49:8
- 2 Corinthians 6:15 Greek Beliar, a variant of Belial
- 2 Corinthians 6:16 Lev. 26:12; Jer. 32:38; Ezek. 37:27
- 2 Corinthians 6:17 Isaiah 52:11; Ezek. 20:34,41
- 2 Corinthians 6:18 2 Samuel 7:14; 7:8
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.