Add parallel Print Page Options

Bokosi la Chipangano Pakati pa Afilisti

Afilisti atalanda Bokosi la Mulungu lija, analitenga kuchoka ku Ebenezeri kupita ku Asidodi. Kenaka anatenga Bokosi la Chipanganolo nabwera nalo ku nyumba ya Dagoni ndi kuliyika pambali pa Dagoni. Anthu a ku Asidodi atadzuka mmawa mwake, anangoona Dagoni atagwa pansi chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova! Iwo anatenga Dagoni ndi kumuyimika pamalo pake. Koma mmawa mwakenso atadzuka, anaona Dagoni atagwa chafufumimba pamaso pa Bokosi la Yehova. Mutu wake ndi manja ake zinali zitaduka ndi kugwera pa khonde polowera, thunthu lake lokha ndilo linatsala. Nʼchifukwa chake mpaka lero ansembe a Dagoni kapena wina aliyense amene amalowa mʼkachisi wa Dagoni ku Asidodi saponda pa khonde.

Yehova analanga koopsa anthu a ku Asidodi. Yehova anawawononga ndi kuwazunza ndi zithupsa Asidoniwa pamodzi ndi anthu a madera ozungulira. Anthu a ku Asidodi ataona zimene zimachitika anati, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lisakhale kuno chifukwa akutizunza ife pamodzi ndi mulungu wathu Dagoni.” Choncho anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anawafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu wa Israeli tichite nalo chiyani?”

Iwo anayankha kuti, “Bokosi la Mulungu wa Israeli lipite ku Gati.” Kotero analichotsa Bokosi la Mulungu wa Israelilo.

Koma atafika nalo ku Gati, Yehova analanga mzindawo, ndipo anthu anachita mantha aakulu. Iye anazunza anthu a mu mzindawo, ana ndi akulu omwe, ndi zithupsa. 10 Choncho anatumiza Bokosi la Mulungu ku Ekroni.

Koma Bokosi la Mulungu lija litangofika ku Ekroni, anthu a ku Ekroni analira kuti, “Abwera nalo Bokosi la Mulungu wa Israeli kwa ife kuti atiphe pamodzi ndi anthu athu.” 11 Kotero iwo anayitana atsogoleri onse a Afilisti kuti asonkhane ndipo anati, “Chotsani Bokosi la Mulungu wa Israeli, libwerere ku malo ake. Tikapanda kutero lidzatipha ife ndi anthu athu.” Pakuti mu mzinda monse munali mantha aakulu kwambiri ndipo Mulungu ankawalanga kwambiri anthu a kumeneko. 12 Anthu amene sanafe anavutika ndi zithupsa, ndipo kulira kwa anthu a mu mzindamo kunamveka kumwamba.

The Philistines and the Ark

When the Philistines captured the ark of God, they brought it from (A)Ebenezer to (B)Ashdod. Then the Philistines took the ark of God and brought it into the house of Dagon and set it up beside (C)Dagon. And when the people of Ashdod rose early the next day, behold, (D)Dagon had fallen face downward on the ground before the ark of the Lord. So they took Dagon and put him back in his place. But when they rose early on the next morning, behold, Dagon had fallen face downward on the ground before the ark of the Lord, (E)and the head of Dagon and both his hands were lying cut off on the threshold. Only the trunk of Dagon was left to him. This is why the priests of Dagon and all who enter the house of Dagon (F)do not tread on the threshold of Dagon in Ashdod to this day.

(G)The hand of the Lord was heavy against the people of Ashdod, and he terrified and afflicted them with (H)tumors, both Ashdod and its territory. And when the men of Ashdod saw how things were, they said, “The ark of the God of Israel must not remain with us, for his hand is hard against us and against Dagon our god.” So they sent and gathered together all (I)the lords of the Philistines and said, “What shall we do with the ark of the God of Israel?” They answered, “Let the ark of the God of Israel be brought around to Gath.” So they brought the ark of the God of Israel there. But after they had brought it around, (J)the hand of the Lord was against the city, causing a very great panic, and he afflicted the men of the city, both young and old, so that (K)tumors broke out on them. 10 So they sent the ark of God to Ekron. But as soon as the ark of God came to Ekron, the people of Ekron cried out, “They have brought around to us the ark of the God of Israel to kill us and our people.” 11 (L)They sent therefore and gathered together all the lords of the Philistines and said, “Send away the ark of the God of Israel, and let it return to its own place, that it may not kill us and our people.” For there was a deathly panic throughout the whole city. (M)The hand of God was very heavy there. 12 The men who did not die were struck with (N)tumors, and the cry of the city went up to heaven.