Add parallel Print Page Options

Ndipo mawu a Samueli anafika kwa Aisraeli onse.

Afilisti Alanda Bokosi la Chipangano

Aisraeli anapita kukamenya nkhondo ndi Afilisti. Aisraeli anamanga misasa yawo ku Ebenezeri, ndipo Afilisti anamanga ku Afeki. Afilisti anandanda kuyangʼana Aisraeli nayamba kumenyana. Nkhondo inakula ndipo Afilisti anagonjetsa Aisraeli napha anthu 4,000 pa malo a nkhondopo. Asilikali atabwerera ku misasa, akuluakulu a Israeli anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Yehova walola kuti tigonjetsedwe lero pamaso pa Afilisti? Tiyeni tikatenge Bokosi la Chipangano cha Yehova ku Silo kuti Yehovayo abwere kukhala pakati pathu ndi kutipulumutsa mʼmanja mwa adani athu.”

Choncho anatuma anthu ku Silo ndipo anakatenga Bokosi la Chipangano cha Yehova Wamphamvuzonse amene amakhala pa akerubi. Ndipo ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi anatsagana nalo Bokosi la Chipangano cha Mulungu.

Bokosi la Chipangano cha Yehova litafika ku msasa, Aisraeli onse anafuwula kwambiri mpaka nthaka inagwedezeka. Atamva kufuwulaku, Afilisti anafunsa, “Kodi kufuwula kwakukulu kumeneku ku misasa ya Ahebri ndi kwachiyani?”

Atamva kuti Bokosi la Yehova lafika ku msasako, Afilisti anachita mantha pakuti iwo ankanena kuti, “Milungu yafika ku msasa. Iwo anati, ‘Tili pamavuto. Chinthu choterechi sichinachitikepo nʼkale lomwe. Atsoka ife! Adzatipulumutsa ndani mʼmanja mwa milungu yamphamvuyi? Iyi ndi milungu imene inakantha Aigupto ndi miliri yosiyanasiyana mʼchipululu. Limbani mtima Afilisti! Chitani chamuna, kuti mungakhale akapolo a Ahebri monga iwowa alili akapolo anu. Chitani chamuna ndipo menyani nkhondo!’ ”

10 Choncho Afilisti anamenya nkhondo, ndipo anagonjetsa Aisraeli. Iwo anathawa aliyense kwawo. Ankhondo a Aisraeli oyenda pansi okwanira 30,000 anaphedwa. 11 Ndipo Bokosi la Chipangano la Yehova linalandidwa, ndiponso ana awiri Eli, Hofini ndi Finehasi anaphedwa.

Imfa ya Eli

12 Tsiku lomwelo munthu wina wa fuko la Benjamini anathawa ku nkhondo ndipo anafika ku Silo. Iyeyu zovala zake zinali zongʼamba ndipo anadzithira dothi kumutu kuonetsa chisoni. 13 Atafika, anapeza Eli atakhala pa mpando wake mʼmbali mwa msewu, akungoyangʼana, pakuti ankadera nkhawa Bokosi la Mulungu. Munthuyo atalowa mu mzindamo ndi kufotokoza zimene zinachitika ku nkhondo, anthu onse a mu mzindamo anayamba kulira.

14 Eli atamva kulirako anafunsa kuti, “Kodi phokosoli likutanthauza chiyani?”

Tsono munthu wa fuko la Benjamini uja anapita msanga kwa Eli kukamufotokozera. 15 Nthawiyo nʼkuti Eli ali wa zaka 98 ndipo maso ake anali atachita khungu kotero kuti samatha kuona. 16 Munthuyo anamuwuza Eli kuti, “Ine ndabwera kuchokera ku nkhondo, ndathawako lero lomwe lino.”

Eli anafunsa, “Nanga nkhondo yayenda bwanji mwana wanga?”

17 Iye anayankha kuti, “Aisraeli athawa pamaso pa Afilisti. Anthu ambirimbiri aphedwa. Ana anunso Hofini ndi Finehasi aphedwa. Bokosi la Mulungu nalonso lalandidwa.”

18 Atangotchula Bokosi la Yehova, Eli anagwa chagada, kuchoka pa mpando wake umene unali mʼmbali mwa chitseko cha mpanda. Khosi lake linathyoka ndipo anafa, pakuti anali okalamba ndi onenepa kwambiri. Iye anatsogolera Israeli zaka makumi anayi.

19 Nthawiyo, mpongozi wa Eli, mkazi wa Finehasi anali woyembekezera ndipo anali pafupi kuchira. Atamva kuti Bokosi la Mulungu lalandidwa ndi kuti mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake amwalira, ululu wa pobereka mwana unamufikira modzidzimutsa ndipo anabereka mwana. 20 Popeza mkaziyo anali pafupi kumwalira, akazi amene amamuthandiza anati, “Usaope, wabereka mwana wamwamuna” Koma iye sanayankhe kapena kulabadirako.

21 Tsono iye anatcha mwanayo dzina loti Ikabodi kutanthauza kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli,” chifukwa cha kulandidwa Bokosi la Mulungu ndi imfa ya mpongozi wake Eli ndi mwamuna wake. 22 Ananena momwemo kuti, “Ulemerero wachoka mu Israeli, pakuti Bokosi la Mulungu lalandidwa.”

The Philistines Capture the Ark

And the word of Samuel came to all Israel.

Now Israel went out to battle against the Philistines. They encamped at (A)Ebenezer, and the Philistines encamped at (B)Aphek. The Philistines drew up in line against Israel, and when the battle spread, Israel was defeated before the Philistines, who killed about four thousand men on the field of battle. And when the people came to the camp, the elders of Israel said, “Why has the Lord defeated us today before the Philistines? Let us bring the ark of the covenant of the Lord here (C)from Shiloh, that it[a] may come among us and save us from the power of our enemies.” So the people sent to Shiloh and brought from there the ark of the covenant of the Lord of hosts, (D)who is enthroned on the cherubim. And the two sons of Eli, Hophni and Phinehas, were there with the ark of the covenant of God.

As soon as the ark of the covenant of the Lord came into the camp, all Israel (E)gave a mighty shout, so that the earth resounded. And when the Philistines heard the noise of the shouting, they said, “What does this great shouting in the camp of the Hebrews mean?” And when they learned that the ark of the Lord had come to the camp, the Philistines were afraid, for they said, “A god has come into the camp.” And they said, “Woe to us! For nothing like this has happened before. Woe to us! Who can deliver us from the power of these mighty gods? These are the gods who struck the Egyptians with every sort of plague in the wilderness. (F)Take courage, and be men, O Philistines, lest you become slaves to the Hebrews (G)as they have been to you; be men and fight.”

10 So the Philistines fought, (H)and Israel was defeated, (I)and they fled, every man to his home. And there was a very great slaughter, for thirty thousand foot soldiers of Israel fell. 11 (J)And the ark of God was captured, (K)and the two sons of Eli, Hophni and Phinehas, died.

The Death of Eli

12 A man of Benjamin ran from the battle line and came to Shiloh the same day, (L)with his clothes torn and with dirt on his head. 13 When he arrived, (M)Eli was sitting on his seat by the road watching, for his heart trembled for the ark of God. And when the man came into the city and told the news, all the city cried out. 14 When Eli heard the sound of the outcry, he said, “What is this uproar?” Then the man hurried and came and told Eli. 15 Now Eli was ninety-eight years old (N)and his eyes were set so that he could not see. 16 And the man said to Eli, “I am he who has come from the battle; I fled from the battle today.” And he said, (O)“How did it go, my son?” 17 He who brought the news answered and said, “Israel has fled before the Philistines, and there has also been a great defeat among the people. Your two sons also, Hophni and Phinehas, are dead, and the ark of God has been captured.” 18 As soon as he mentioned the ark of God, Eli fell over backward (P)from his seat by the side of the gate, and his neck was broken and he died, for the man was old and heavy. He had judged Israel forty years.

19 Now his daughter-in-law, the wife of Phinehas, was pregnant, about to give birth. And when she heard the news that the ark of God was captured, and that her father-in-law and her husband were dead, she bowed and gave birth, for her pains came upon her. 20 And about the time of her death the women attending her said to her, (Q)“Do not be afraid, for you have borne a son.” But she did not answer or pay attention. 21 And she named the child (R)Ichabod, saying, (S)“The glory has departed[b] from Israel!” because (T)the ark of God had been captured and because of her father-in-law and her husband. 22 And she said, “The glory has departed from Israel, (U)for the ark of God has been captured.”

Footnotes

  1. 1 Samuel 4:3 Or he
  2. 1 Samuel 4:21 Or gone into exile; also verse 22