1 Samueli 1
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Banja la Elikana
1 Panali munthu wina wochokera ku Ramataimu, Mzofimu wa ku dziko la mapiri la Efereimu. Iyeyu dzina lake anali Elikana ndipo anali mwana wa Yerohamu, mwana wa Elihu, mwana wa Tohu, mwana wa Zufu wa fuko la Efereimu. 2 Iye anali ndi akazi awiri, Hana ndi Penina. Penina anali ndi ana, koma Hana analibe.
3 Chaka ndi chaka Elikana ankachoka ku mudzi kwawo kupita ku Silo kukapembedza ndi kukapereka nsembe kwa Yehova Wamphamvuzonse. Ku Siloko kunali ana awiri a Eli, Hofini ndi Finehasi amene anali ansembe a Yehova. 4 Tsiku lopereka nsembe likafika Elikana amapereka magawo a nsembeyo kwa mkazi wake Penina ndi kwa ana ake onse aamuna ndi aakazi. 5 Ngakhale ankamukonda Hana, koma ankamupatsa gawo limodzi popeza Yehova sanamupatse ana. 6 Tsono popeza Yehova sanamupatse Hana ana, mkazi mnzakeyo ankamuyamba dala ndi cholinga chomukwiyitsa. 7 Izi zimachitika chaka ndi chaka. Hana ankati akamapita ku Nyumba ya Yehova mkazi mnzakeyo ankamunyogodola. Choncho Hana ankangokhalira kulira osafuna ndi kudya komwe. 8 Tsono mwamuna wake Elikana ankamufunsa kuti, “Hana ukulira chifukwa chiyani? Wakhumudwa ndi chiyani kuti sukufuna ndi kudya komwe? Kodi ine kwa iwe sindili woposa ana aamuna khumi?”
9 Tsiku lina atatha kudya ndi kumwa ku Silo kuja, Hana anayimirira kukapemphera. Nthawiyi nʼkuti wansembe Eli atakhala pa mpando pa khomo la Nyumba ya Yehova. 10 Hana anavutika mʼmoyo mwake, ndipo anapemphera kwa Yehova akulira kwambiri. 11 Ndipo iye analumbira kuti, “Inu Yehova Wamphamvuzonse, ngati muyangʼana kusauka kwa mtumiki wanune, ndi kuyankha pemphero langa osandiyiwala ine mtumiki wanu pondipatsa mwana wamwamuna, ine ndidzamupereka mwanayo kwa inu Yehova masiku onse a moyo wake. Lumo silidzapita pa mutu pake.”
12 Akupemphera choncho kwa Yehova, Eli ankamuyangʼana pakamwa. 13 Hana ankapemphera chamumtima ndipo milomo yake inkangogwedera koma mawu ake samamveka. Choncho Eli anaganiza kuti anali ataledzera. 14 Ndipo anamufunsa Hana kuti, “Kodi mukhala chiledzerere mpaka liti? Pitani, ayambe wakuchokani vinyo mwamwayo.”
15 Koma Hana anayankha kuti, “Sichoncho mbuye wanga. Ndakhala ndikumukhuthulira Yehova chisoni changa. Sindinamwe vinyo kapena chakumwa choledzeretsa chilichonse, popeza nthawi yonseyi ndakhala ndikupereka kwa Yehova nkhawa yayikulu ndi mavuto anga. 16 Musaganize kuti mtumiki wanu ndi kukhala mkazi wachabechabe. Ine ndakhala ndi kupereka nkhawa yanga yayikulu ndi zowawa zanga.”
17 Eli anayankha, “Pitani mu mtendere, ndipo Mulungu wa Israeli akupatseni zimene mwamupemphazo.”
18 Hana anati, “Mundikomerebe mtima mtumiki wanune.” Kenaka anachoka nakadya, ndipo sanaonekenso wachisoni.
19 Elikana ndi banja lake anadzuka mmawa mwake nakapemphera pamaso pa Yehova. Pambuyo pake anabwerera kwawo ku Rama. Elikana anakhala pamodzi ndi mkazi wake, ndipo Yehova anamukumbuka Hanayo. 20 Motero Hana anakhala ndi pakati ndipo anabereka mwana wamwamuna. Anamutcha dzina lake Samueli, popeza anati, “Ndinachita kumupempha kwa Yehova.”
Hana Apereka Samueli kwa Yehova
21 Elikana ndi banja lake lonse anapita kukapereka nsembe ya pa chaka kwa Yehova ndi kukakwaniritsa malonjezo ake. 22 Koma Hana sanapite nawo popeza anawuza mwamuna wake kuti, “Mwanayu akadzaleka kuyamwa, ndidzapita naye ndi kukamupereka pamaso pa Yehova ndipo adzakhala kumeneko moyo wake wonse.”
23 Elikana mwamuna wake anamuwuza kuti, “Chita chimene chakukomera. Tsala kuno mpaka utamusiyitsa kuyamwa, Yehova yekha akwaniritse mawu ake.” Choncho mkaziyo anatsala ku nyumba ndi kusamalira mwana wake mpaka atamuletsa kuyamwa.
24 Atamuletsa kuyamwa, Hana anatenga mwanayo ali wachichepere, ndikupita naye ku nyumba ya Yehova ku Silo. Anatenga ngʼombe yamphongo ya zaka zitatu, ufa wa makilogalamu khumi, ndi thumba lachikopa la vinyo. 25 Tsono anapha ngʼombe yamphongo ija ndi kupereka mwana uja kwa Eli. 26 Ndipo Hana anati kwa Eli, “Mbuye wanga, ine ndikunenetsadi pamaso panu kuti ndine mkazi uja amene anayima pamaso panu ndi kumapemphera kwa Yehova. 27 Ndinapempha mwana uyu, ndipo Yehova wandipatsa chimene ndinamupempha. 28 Ndiye tsopano ine ndikumupereka kwa Yehova. Pa moyo wake wonse adzakhala wa Yehova.” Ndipo onse anapembedza Yehova kumeneko.
1 Samuel 1
Evangelical Heritage Version
The Birth of Samuel
1 There was a man from Ramathaim of the Zuphites in the hill country of Ephraim whose name was Elkanah. He was the son of Jeroham, the son of Elihu, the son of Tohu, the son of Zuph, an Ephraimite. 2 He had two wives. One was named Hannah, and the other was named Peninnah. Peninnah had children, but Hannah had no children.
3 Every year this man went up from his city to worship and to offer sacrifices to the Lord of Armies[a] at Shiloh. Hophni and Phinehas, the two sons of Eli, were serving there as priests of the Lord.
4 On the day when Elkanah sacrificed, he gave portions of food to his wife Peninnah and to all her sons and daughters, 5 but to Hannah he gave a double portion, because he loved Hannah, but the Lord had kept her from having children.[b]
6 Hannah’s rival kept taunting her to make her miserable, because the Lord had kept Hannah from having children. 7 Year after year, when Hannah went up to the Lord’s house, her rival taunted her, so Hannah would weep and would not eat. 8 Her husband Elkanah said to her, “Hannah, why are you weeping? Why don’t you eat? Why is your heart so sad? Am I not better to you than ten sons?”
9 Once, when they had finished eating and drinking in Shiloh, Hannah stood up. Eli the priest was sitting on his chair by the doorpost of the Lord’s temple. 10 Hannah’s spirit was very distressed, and as she prayed to the Lord, she sobbed and wept many tears. 11 She made a vow and said, “O Lord of Armies, if you will carefully consider the misery of your servant and remember me, and if you do not forget your servant but give your servant a male child,[c] then I will give him to the Lord all the days of his life, and no razor shall ever touch his head.”
12 As she continued praying before the Lord, Eli was looking at her mouth. 13 Hannah was speaking silently from her heart. Although her lips were moving, her voice could not be heard. Eli thought she was drunk 14 and said to her, “How long are you going to be drunk? Get away from your wine!”
15 Hannah replied, “No, my lord, I am a woman with a very troubled spirit. I have not been drinking wine or beer, but I have poured out my soul to the Lord. 16 Do not regard your servant as a worthless, wicked woman. I have been speaking like this because of my great misery and because of how I have been grieved.”[d]
17 Then Eli answered, “Go in peace, and may the God of Israel give you what you have asked for.”
18 She said, “Let your servant find favor in your sight.” So the woman went on her way. She ate, and her face no longer looked sad.
19 They got up early in the morning and worshipped the Lord. They then returned to their home at Ramah.
Elkanah was intimate with Hannah his wife, and the Lord remembered her. 20 So Hannah conceived and gave birth to a son. She named him Samuel[e] because she said, “I asked for him from the Lord.”
21 When this man Elkanah and his entire household went up to offer the annual sacrifice to the Lord and to fulfill his vow, 22 Hannah did not go up with them, because she said to her husband, “Not until the child is weaned. Then I will bring him, so that he can appear before the Lord and remain there permanently.”
23 Her husband Elkanah said to her, “Do whatever you think is best. Wait until you have weaned him. Yes, then the Lord will establish his word.”
So the woman stayed at home, and she nursed her son until she was ready to wean him. 24 When she had weaned him, she took him up with her. She also took a three-year-old bull,[f] twenty-five pounds[g] of flour, and a container of wine, and she brought him to the House of the Lord in Shiloh. The boy was ⎣with them. And they brought him before the Lord, and his father killed the sacrifice as he regularly did before the Lord, and he brought⎦ the boy.[h] 25 When they had killed the bull, they presented the child to Eli. 26 She said, “Excuse me, my lord. As your soul lives,[i] my lord, I am the woman who stood here next to you, praying to the Lord. 27 I prayed for this child, and the Lord has granted me what I asked for. 28 So now I have also dedicated him to the Lord. As long as he lives, he is dedicated to the Lord.” So he worshipped the Lord there.
Footnotes
- 1 Samuel 1:3 Traditionally Lord of Hosts or Lord Sebaoth. God is the Lord of Armies because he rules the army of angels and the army of stars. If he rules over these great powers, he rules over everything.
- 1 Samuel 1:5 Literally had closed her womb
- 1 Samuel 1:11 Literally seed of men, an unusual expression
- 1 Samuel 1:16 Or provoked
- 1 Samuel 1:20 Samuel sounds like the Hebrew words heard by God.
- 1 Samuel 1:24 The translation follows the reading found in a Hebrew Dead Sea Scroll and in the Greek Old Testament. The main Hebrew text reads three bulls, but the following verse refers to only one animal.
- 1 Samuel 1:24 Hebrew an ephah
- 1 Samuel 1:24 The words in half-brackets are included in a Hebrew Dead Sea Scroll. The main Hebrew text has the cryptic reading the boy [was] a boy. The longer reading may preserve evidence of an accidental skip during the copying of the standard Hebrew text from one occurrence of the word boy to the next. This Dead Sea Scroll also has additional words in verse 25, which specify that Elkanah presented the sacrifice and Hannah presented Samuel to Eli.
- 1 Samuel 1:26 This is an oath that means I swear on your life.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
The Holy Bible, Evangelical Heritage Version®, EHV®, © 2019 Wartburg Project, Inc. All rights reserved.