Add parallel Print Page Options

Pamene ndinabwera kwa inu, abale, sindinabwere ndi luntha lodziwa kuyankhula kapena nzeru zapamwamba pamene ndinachitira umboni chinsinsi cha Mulungu. Pakuti ndinatsimikiza pamene ndinali ndi inu kuti ndisadziwe kanthu kena kupatula Yesu Khristu wopachikidwayo. Ndinabwera kwa inu wofowoka ndi wamantha, ndiponso wonjenjemera kwambiri. Uthenga ndi ulaliki wanga sunali wa mawu anzeru ndi onyengerera koma woonetsa mphamvu za Mzimu, kuti chikhulupiriro chanu chisatsamire pa nzeru ya anthu koma pa mphamvu za Mulungu.

Nzeru Yochokera kwa Mzimu

Komabe ife timayankhula uthenga wa nzeru kwa okhwima, koma osati ndi nzeru ya mʼbado uno kapena ya olamula a mʼbado uno, amene mphamvu yawo ikutha. Ayi, ife timayankhula za nzeru yobisika ya Mulungu, nzeru imene inabisidwa ndipo imene Mulungu anatikonzera mu ulemerero wathu isanayambe nthawi. Palibe olamulira aliyense wa mʼbado uno amene anamumvetsetsa popeza anakamumvetsetsa sakanamupachika Ambuye wa ulemerero. Komabe monga zalembedwa kuti,

“Palibe diso linaona,
    palibe khutu linamva,
palibe amene anaganizira,
    zimene Mulungu anakonzera amene amukonda”

10 koma Mulungu waululira ife mwa Mzimu wake.

Mzimu amafufuza zinthu zonse, ndi zozama za Mulungu zomwe. 11 Kodi ndani mwa anthu angadziwe maganizo a munthu wina, kupatula mzimu wa munthuyo wokhala mʼkati mwake? Chimodzimodzinso palibe amene adziwa maganizo a Mulungu kupatula Mzimu wa Mulunguyo. 12 Mzimu amene tinalandira ife si wa dziko lapansi koma Mzimu wochokera kwa Mulungu wotipatsa ife mwaulere. 13 Izi ndi zimene timayankhula osati mʼmawu wophunzitsidwa ndi nzeru za munthu koma mʼmawu wophunzitsidwa ndi Mzimu, kufotokozera zoonadi zauzimu mʼmawu auzimu. 14 Munthu wopanda Mzimu savomereza zinthu zimene zichokera kwa Mzimu wa Mulungu, popeza ndi zopusa kwa iyeyo, ndipo sangazimvetsetse chifukwa zimazindikirika mwa Mzimu. 15 Munthu wauzimu amaweruza pa zinthu zonse, koma iye mwini saweruzidwa ndi munthu aliyense. 16 Pakuti

“Ndani anadziwa malingaliro a Ambuye,
    kuti akhoza kumulangiza Iye.”

Koma tili nawo mtima wa Khristu.

信仰的基礎

弟兄姊妹,我當初到你們那裡傳揚上帝的奧祕,並沒有用高深的言論或哲理。 因為我已決定在你們當中不談別的,只講耶穌基督和祂被釘十字架的事。 那時我在你們當中很軟弱,害怕,戰戰兢兢。 我說話、講道不是靠充滿智慧的雄辯之詞,而是靠聖靈的能力作明證, 好使你們的信仰不是以人的智慧為基礎,而是以上帝的能力為基礎。

當然我們也跟成熟的人談論智慧,不過並非這個世代的智慧,也不是那些在世上當權、將來要衰亡之人的智慧。 我們所講的是上帝隱藏在奧祕中的智慧,是祂為了使我們得榮耀而在萬世以前定好的智慧。 只可惜世上當權的人沒有一個明白這智慧。他們要是明白,就不會把榮耀的主釘在十字架上了。 正如聖經上說:

「上帝為愛祂的人所預備的,
是眼睛未曾見過,
耳朵未曾聽聞,
人心也未曾想到的。」

10 然而,上帝藉著聖靈將這一切啟示給我們,因為聖靈洞悉萬事,連上帝深奧的事都瞭若指掌。 11 除了人裡面的靈,誰能瞭解人的事呢?照樣,除了上帝的聖靈,誰也不能瞭解上帝的事。 12 我們接受的不是這世界的靈,而是上帝的聖靈,使我們可以領會上帝開恩啟示給我們的事。 13 我們講述這些事,不是用人類智慧所教的話,而是用聖靈所教的話,用屬靈的話解釋屬靈的事[a]

14 然而,屬血氣的人不接受從上帝來的聖靈的教導,認為愚不可及,無法明白,因為只有屬靈的人才能參透。 15 屬靈的人能夠參透萬事,但沒有人能參透他。

16 「誰曾知道主的心意,
能夠指教祂呢?」

但我們明白基督的心意。

Footnotes

  1. 2·13 用屬靈的話解釋屬靈的事」或譯「向屬靈的人解釋屬靈的事」。