Add parallel Print Page Options

Imfa ya Sauli ndi Ana Ake

31 Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa. Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa. Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza kwambiri.

Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere kudzandizunza ine.”

Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo. Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa naye limodzi. Motero Sauli ndi ana ake atatu, wonyamula zida zake pamodzi ndi anthu ake onse anafera limodzi pa tsikulo.

Pamene Aisraeli amene anali tsidya lina la chigwa ndi amene anali tsidya la chigwa cha Yorodani anaona kuti gulu la ankhondo la Aisraeli lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.

Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa anapeza Sauli ndi ana ake atatu atafa pa phiri la Gilibowa. Iwo anadula mutu wake ndi kumuvula zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo. 10 Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba yopembedzera Asitoreti, ndipo thupi lake analikhomera pa khoma la mzinda wa Beti-Sani.

11 Pamene anthu a ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli, 12 anthu awo onse olimba mtima anayenda usiku wonse kupita ku Beti-Sani. Anakachotsa mtembo wa Sauli ndi mitembo ya ana ake pa khoma la mzinda wa Beti-Sani, ndipo anabwera nayo ku Yabesi kumene anayitentha ndi moto. 13 Pambuyo pake anatenga mafupa awo ndi kuwakwirira pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.

Saul Takes His Life(A)

31 Now the Philistines fought against Israel; the Israelites fled before them, and many fell dead on Mount Gilboa.(B) The Philistines were in hot pursuit of Saul and his sons,(C) and they killed his sons Jonathan,(D) Abinadab and Malki-Shua.(E) The fighting grew fierce around Saul, and when the archers overtook him, they wounded(F) him critically.

Saul said to his armor-bearer, “Draw your sword and run me through,(G) or these uncircumcised(H) fellows will come and run me through and abuse me.”

But his armor-bearer was terrified and would not do it; so Saul took his own sword and fell on it. When the armor-bearer saw that Saul was dead, he too fell on his sword and died with him. So Saul and his three sons and his armor-bearer and all his men died(I) together that same day.

When the Israelites along the valley and those across the Jordan saw that the Israelite army had fled and that Saul and his sons had died, they abandoned their towns and fled. And the Philistines came and occupied them.

The next day, when the Philistines(J) came to strip the dead, they found Saul and his three sons fallen on Mount Gilboa. They cut off his head and stripped off his armor, and they sent messengers throughout the land of the Philistines to proclaim the news(K) in the temple of their idols and among their people.(L) 10 They put his armor in the temple of the Ashtoreths(M) and fastened his body to the wall of Beth Shan.(N)

11 When the people of Jabesh Gilead(O) heard what the Philistines had done to Saul, 12 all their valiant men(P) marched through the night to Beth Shan. They took down the bodies of Saul and his sons from the wall of Beth Shan and went to Jabesh, where they burned(Q) them. 13 Then they took their bones(R) and buried them under a tamarisk(S) tree at Jabesh, and they fasted(T) seven days.(U)