Add parallel Print Page Options

Afilisti Akana Davide

29 Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli. Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi. Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?”

Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”

Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa? Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti,

“ ‘Sauli wapha anthu 1,000
    koma Davide wapha miyandamiyanda?’ ”

Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna. Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”

Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”

Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’ 10 Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”

11 Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.

Achish Sends David Back to Ziklag

29 The Philistines gathered(A) all their forces at Aphek,(B) and Israel camped by the spring in Jezreel.(C) As the Philistine rulers marched with their units of hundreds and thousands, David and his men were marching at the rear(D) with Achish. The commanders of the Philistines asked, “What about these Hebrews?”

Achish replied, “Is this not David,(E) who was an officer of Saul king of Israel? He has already been with me for over a year,(F) and from the day he left Saul until now, I have found no fault in him.”

But the Philistine commanders were angry with Achish and said, “Send(G) the man back, that he may return to the place you assigned him. He must not go with us into battle, or he will turn(H) against us during the fighting. How better could he regain his master’s favor than by taking the heads of our own men? Isn’t this the David they sang about in their dances:

“‘Saul has slain his thousands,
    and David his tens of thousands’?”(I)

So Achish called David and said to him, “As surely as the Lord lives, you have been reliable, and I would be pleased to have you serve with me in the army. From the day(J) you came to me until today, I have found no fault in you, but the rulers(K) don’t approve of you. Now turn back and go in peace; do nothing to displease the Philistine rulers.”

“But what have I done?” asked David. “What have you found against your servant from the day I came to you until now? Why can’t I go and fight against the enemies of my lord the king?”

Achish answered, “I know that you have been as pleasing in my eyes as an angel(L) of God; nevertheless, the Philistine commanders(M) have said, ‘He must not go up with us into battle.’ 10 Now get up early, along with your master’s servants who have come with you, and leave(N) in the morning as soon as it is light.”

11 So David and his men got up early in the morning to go back to the land of the Philistines, and the Philistines went up to Jezreel.