Add parallel Print Page Options

Davide Apita ku Adulamu ndi ku Mizipa

22 Davide anachoka kumeneko nathawira ku phanga la Adulamu. Abale ake ndi banja lonse la abambo ake anamva izi, anapita kumene kunali Davide. Ndipo aliyense amene anali pa mavuto, kapena ndi ngongole kapenanso amene anali wosakondwa anasonkhana kwa iye, ndipo iye anakhala mtsogoleri wawo. Onse pamodzi analipo amuna 400.

Kuchokera kumeneko Davide anapita ku Mizipa ku Mowabu ndipo anapempha mfumu ya Mowabu kuti, “Bwanji abambo ndi amayi anga akhale nanu mpaka ine nditadziwa chimene Mulungu adzachite nane?” Choncho iye anawasiya kwa mfumu ya Mowabu ndipo anakhala naye nthawi yonse imene Davide ankabisala ku phanga kuja.

Koma mneneri Gadi anawuza Davide kuti, “Usakhale ku phanga kuno. Pita ku dziko la Yuda.” Kotero Davide anachoka ndi kupita ku nkhalango ya Hereti.

Sauli Apha Ansembe a ku Nobi

Tsono Sauli anamva kuti Davide ndi anthu ake apezeka. Nthawiyo nʼkuti Sauli atakhala pansi pa mtengo wa bwemba pa phiri la ku Gibeya, mkondo uli mʼdzanja lake ndi ankhondo ake atayima chomuzungulira. Tsono Sauli anafunsa ankhondo ake aja kuti, “Tamverani inu anthu a fuko la Benjamini! Kodi mwana wa Yese adzakupatsani nonsenu minda ndi minda ya mpesa? Kodi nonsenu adzakuyikani kukhala atsogoleri a magulu ankhondo? Mwinatu nʼchifukwa chake mwagwirizana zondichita chiwembu. Palibe amene anandiwuza pamene mwana wanga ankapanga pangano ndi mwana wa Yese. Palibe aliyense amene ankalabadirako za ine kapena kundiwuza kuti mwana wanga wautsa mtima wa wantchito wanga kuti andiwukire monga wachitira lero.”

Koma Doegi Mwedomu anayima pafupi ndi nduna za Sauli nati, “Ine ndinaona mwana wa Yese atabwera kwa Ahimeleki mwana wa Ahitubi ku Nobi. 10 Ahimelekiyo anafunsa kwa Yehova chomwe Davide ayenera kuchita. Iye anamupatsa zakudya ndiponso lupanga la Goliati Mfilisiti uja.”

11 Pamenepo mfumu inayitanitsa wansembe Ahimeleki mwana wa Ahitubi ndi banja lonse la abambo ake, amene anali ansembe ku Nobi. Ndipo onse anabwera kwa mfumu. 12 Sauli anati, “Tsono tamvera, mwana wa Ahitubi.”

Iye anayankha kuti, “Inde mbuye wanga.”

13 Sauli anamufunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani iwe ndi mwana wa Yese mwandiwukira ine? Wamupatsa buledi ndi lupanga. Wafunsiranso kwa Yehova zoti andiwukire ndi kundibisalira monga wachita leromu?”

14 Ahimeleki anayankha mfumu kuti, “Kodi ndani mwa ankhondo anu onse amene ali wokhulupirika monga Davide? Iye uja ndi mkamwini wa mfumu, kapitawo wa asilikali okutetezani ndiponso munthu amene amalemekezedwa mʼbanja lanu? 15 Kodi tsiku limeneli linali loyamba kuti ndimufunsire kwa Yehova? Ayi sichoncho! Mfumu musandinenere kanthu kalikonse koyipa kapena banja la abambo anga, pakuti sindikudziwa kanthu kena kalikonse ka zimenezi.”

16 Koma mfumu inati, “Iwe Ahimeleki ndi banja lonse la abambo ako mudzaphedwa ndithu.”

17 Kenaka mfumu inalamulira alonda amene anali naye kuti, “Iphani ansembe a Yehovawa chifukwa iwo akugwirizana ndi Davide. Iwo amadziwa kuti Davide ankathawa koma sanandiwuze.”

Koma antchito a mfumu aja sanasamule dzanja kuti aphe ansembe a Yehova.

18 Kotero mfumu inalamula Doegi kuti, “Uwaphe ndiwe ansembewa.” Choncho Doegi Mwedomu anapita ndi kuwapha. Tsiku limenelo iye anapha amuna 85 amene amavala efodi wa nsalu yofewa. 19 Kunena za Nobi, mzinda wa ansembe, Sauli anapha amuna ndi amayi, ana ndi makanda pamodzi ndi ngʼombe, abulu ndi nkhosa.

20 Koma Abiatara mwana wa Ahimeleki mwana wa Ahitubi anapulumuka ndi kuthawira kwa Davide. 21 Abiatara anawuza Davide kuti Sauli wapha ansembe a Yehova. 22 Ndipo Davide anati kwa Abiatara, “Tsiku lija pamene Doegi Mwedomu anali kumene kuja, ine ndimadziwa kuti salephera kukamuwuza Sauli. Ine ndi amene ndaphetsa banja lonse la abambo ako. 23 Iwe khala ndi ine, usaope munthu amene akufuna moyo wako komanso wanga. Udzatetezeka ukakhala ndi ine.”

David at Adullam and Mizpah

22 David left Gath and escaped to the cave(A) of Adullam.(B) When his brothers and his father’s household heard about it, they went down to him there. All those who were in distress or in debt or discontented gathered(C) around him, and he became their commander. About four hundred men were with him.

From there David went to Mizpah in Moab and said to the king of Moab, “Would you let my father and mother come and stay with you until I learn what God will do for me?” So he left them with the king of Moab,(D) and they stayed with him as long as David was in the stronghold.

But the prophet Gad(E) said to David, “Do not stay in the stronghold. Go into the land of Judah.” So David left and went to the forest of Hereth.(F)

Saul Kills the Priests of Nob

Now Saul heard that David and his men had been discovered. And Saul was seated,(G) spear in hand, under the tamarisk(H) tree on the hill at Gibeah, with all his officials standing at his side. He said to them, “Listen, men of Benjamin! Will the son of Jesse give all of you fields and vineyards? Will he make all of you commanders(I) of thousands and commanders of hundreds? Is that why you have all conspired(J) against me? No one tells me when my son makes a covenant(K) with the son of Jesse.(L) None of you is concerned(M) about me or tells me that my son has incited my servant to lie in wait for me, as he does today.”

But Doeg(N) the Edomite, who was standing with Saul’s officials, said, “I saw the son of Jesse come to Ahimelek son of Ahitub(O) at Nob.(P) 10 Ahimelek inquired(Q) of the Lord for him; he also gave him provisions(R) and the sword(S) of Goliath the Philistine.”

11 Then the king sent for the priest Ahimelek son of Ahitub and all the men of his family, who were the priests at Nob, and they all came to the king. 12 Saul said, “Listen now, son of Ahitub.”

“Yes, my lord,” he answered.

13 Saul said to him, “Why have you conspired(T) against me, you and the son of Jesse, giving him bread and a sword and inquiring of God for him, so that he has rebelled against me and lies in wait for me, as he does today?”

14 Ahimelek answered the king, “Who(U) of all your servants is as loyal as David, the king’s son-in-law, captain of your bodyguard and highly respected in your household? 15 Was that day the first time I inquired of God for him? Of course not! Let not the king accuse your servant or any of his father’s family, for your servant knows nothing at all about this whole affair.”

16 But the king said, “You will surely die, Ahimelek, you and your whole family.(V)

17 Then the king ordered the guards at his side: “Turn and kill the priests of the Lord, because they too have sided with David. They knew he was fleeing, yet they did not tell me.”

But the king’s officials were unwilling(W) to raise a hand to strike the priests of the Lord.

18 The king then ordered Doeg, “You turn and strike down the priests.”(X) So Doeg the Edomite turned and struck them down. That day he killed eighty-five men who wore the linen ephod.(Y) 19 He also put to the sword(Z) Nob,(AA) the town of the priests, with its men and women, its children and infants, and its cattle, donkeys and sheep.

20 But one son of Ahimelek son of Ahitub,(AB) named Abiathar,(AC) escaped and fled to join David.(AD) 21 He told David that Saul had killed the priests of the Lord. 22 Then David said to Abiathar, “That day, when Doeg(AE) the Edomite was there, I knew he would be sure to tell Saul. I am responsible for the death of your whole family. 23 Stay with me; don’t be afraid. The man who wants to kill you(AF) is trying to kill me too. You will be safe with me.”