Add parallel Print Page Options

Magulu a Anthu Ankhondo

27 Uwu ndi mndandanda wa Aisraeli, atsogoleri a mabanja, olamulira asilikali 1,000, olamulira asilikali 100 ndi akuluakulu awo, amene ankatumikira mfumu mʼzonse zokhudza magulu a ankhondo, amene amagwira ntchito mwezi ndi mwezi chaka chonse. Gulu lililonse linali ndi anthu 24,000.

Amene amalamulira gulu loyamba pa mwezi woyamba anali Yasobeamu mwana wa Zabidieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000. Iyeyu anali chidzukulu cha Perezi ndipo anali mkulu wa atsogoleri onse a ankhondo mwezi woyamba.

Amene amalamulira gulu lachiwiri pa mwezi wachiwiri anali Dodai Mwahohi; Mikiloti ndiye anali mtsogoleri wa gulu lake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Wolamulira ankhondo wachitatu, pa mwezi wachitatu anali Benaya, mwana wa wansembe Yehoyada. Iye anali mtsogoleri ndipo pa gulu lake panali ankhondo 24,000. Uyu ndi Benaya uja amene anali wamphamvu pa gulu la anthu makumi atatu ndipo ndiye amatsogolera anthu makumi atatu aja. Mwana wake Amizabadi ndiye amatsogolera gulu lake.

Wachinayi pa mwezi wachinayi anali Asaheli mʼbale wake wa Yowabu; ndipo mwana wake Zebadiya ndiye analowa mʼmalo mwake. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Wachisanu pa mwezi wachisanu anali Samihuti, mdzukulu wa Izira. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Wa 6 pa mwezi wa 6 anali Ira mwana wa Ikesi wa ku Tekowa. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

10 Wa 7 pa mwezi wa 7 anali Helezi Mpeloni wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

11 Wa 8 pa mwezi wa 8 anali Sibekai Mhusati, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000

12 Wa 9 pa mwezi wa 9 anali Abiezeri wa banja la Anatoti, wa fuko la Benjamini. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

13 Wa khumi pa mwezi wa khumi anali Mahazayi wa ku Netofa, wa mbumba ya Zera. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

14 Mtsogoleri wa 11, pa mwezi wa 11 anali Benaya wa ku Piratoni, wa fuko la Efereimu. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

15 Mtsogoleri wa 12, pa mwezi wa 12 anali Helidai Mnetofa, wa banja la Otanieli. Pa gulu lake panali asilikali 24,000.

Akuluakulu a Mafuko a Israeli

16 Akuluakulu amene amatsogolera mafuko a Israeli ndi awa:

Mtsogoleri wa fuko la Rubeni: Eliezara mwana wa Zikiri;

mtsogoleri wa fuko la Simeoni: Sefatiya mwana wa Maaka;

17 mtsogoleri wa fuko la Levi: Hasabiya mwana wa Kemueli,

mtsogoleri wa banja la Aaroni: Zadoki;

18 mtsogoleri wa fuko la Yuda: Elihu, mʼbale wake wa Davide;

mtsogoleri wa fuko la Isakara: Omuri mwana wa Mikayeli;

19 mtsogoleri wa fuko la Zebuloni: Isimaiya mwana wa Obadiya;

mtsogoleri wa fuko la Nafutali: Yerimoti mwana wa Azirieli;

20 mtsogoleri wa fuko la Efereimu: Hoseya mwana wa Azaziya;

mtsogoleri wa fuko la theka la Manase: Yoweli mwana wa Pedaya;

21 mtsogoleri wa fuko la theka la Manase limene linali ku Giliyadi: Ido mwana wa Zekariya;

mtsogoleri wa fuko la Benjamini: Yaasieli mwana wa Abineri;

22 mtsogoleri wa fuko la Dani: Azareli mwana wa Yerohamu.

Awa anali akuluakulu a mafuko a Israeli.

23 Davide sanawerenge amuna amene anali ndi zaka makumi awiri kapena kucheperapo, chifukwa Yehova analonjeza kuti adzachulukitsa Aisraeli ngati nyenyezi zamumlengalenga. 24 Yowabu mwana wa Zeruya anayamba kuwerenga amuna koma sanamalize. Mkwiyo unagwera Aisraeli chifukwa cha zimenezi ndipo chiwerengerochi sanachilowetse mʼbuku la mbiri ya mfumu Davide.

Anthu Oyangʼanira Chuma cha Mfumu

25 Azimaveti mwana wa Adieli ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa mfumu.

Yonatani mwana wa Uziya ankayangʼanira nyumba zosungiramo katundu wa maboma ozungulira, mizinda, midzi ndi malo olondera.

26 Eziri mwana wa Kelubi ankayangʼanira anthu ogwira ntchito yolima ku munda.

27 Simei wa ku Rama ankayangʼanira minda ya mpesa.

Zabidi wa ku Sifamu ankayangʼanira mphesa ndi mosungiramo mwake.

28 Baala-Hanani wa ku Gederi ankayangʼanira mitengo ya olivi ndi ya mikuyu ya ku Sefela.

Yowasi ankayangʼanira mafuta a Olivi.

29 Sitirayi wa ku Saroni ankayangʼanira ziweto zimene amaweta ku Saroni.

Safati mwana wa Adilayi ankayangʼanira ngʼombe zakuzigwa.

30 Obili Mwismaeli ankayangʼanira ngamira.

Yehideya Mmerenoti ankayangʼanira abulu.

31 Yazizi Mhagiri akayangʼanira nkhosa ndi mbuzi.

Onsewa anali akuluakulu oyangʼanira chuma cha mfumu Davide.

32 Yonatani, malume wake wa Davide, anali phungu wake ndipo anali munthu wanzeru komanso analinso mlembi. Yehieli mwana wa Hakimoni ankasamalira ana a mfumu.

33 Ahitofele anali phungu wa mfumu.

Husai Mwariki anali bwenzi la mfumu. 34 Ahitofele atamwalira mʼmalo mwake munalowa Yehoyada mwana wa Benaya ndi Abiatara.

Yowabu anali mtsogoleri wa gulu lankhondo la mfumu.

Army Divisions

27 This is the list of the Israelites—heads of families, commanders of thousands and commanders of hundreds, and their officers, who served the king in all that concerned the army divisions that were on duty month by month throughout the year. Each division consisted of 24,000 men.

In charge of the first division, for the first month, was Jashobeam(A) son of Zabdiel. There were 24,000 men in his division. He was a descendant of Perez and chief of all the army officers for the first month.

In charge of the division for the second month was Dodai(B) the Ahohite; Mikloth was the leader of his division. There were 24,000 men in his division.

The third army commander, for the third month, was Benaiah(C) son of Jehoiada the priest. He was chief and there were 24,000 men in his division. This was the Benaiah who was a mighty warrior among the Thirty and was over the Thirty. His son Ammizabad was in charge of his division.

The fourth, for the fourth month, was Asahel(D) the brother of Joab; his son Zebadiah was his successor. There were 24,000 men in his division.

The fifth, for the fifth month, was the commander Shamhuth(E) the Izrahite. There were 24,000 men in his division.

The sixth, for the sixth month, was Ira(F) the son of Ikkesh the Tekoite. There were 24,000 men in his division.

10 The seventh, for the seventh month, was Helez(G) the Pelonite, an Ephraimite. There were 24,000 men in his division.

11 The eighth, for the eighth month, was Sibbekai(H) the Hushathite, a Zerahite. There were 24,000 men in his division.

12 The ninth, for the ninth month, was Abiezer(I) the Anathothite, a Benjamite. There were 24,000 men in his division.

13 The tenth, for the tenth month, was Maharai(J) the Netophathite, a Zerahite. There were 24,000 men in his division.

14 The eleventh, for the eleventh month, was Benaiah(K) the Pirathonite, an Ephraimite. There were 24,000 men in his division.

15 The twelfth, for the twelfth month, was Heldai(L) the Netophathite, from the family of Othniel.(M) There were 24,000 men in his division.

Leaders of the Tribes

16 The leaders of the tribes of Israel:

over the Reubenites: Eliezer son of Zikri;

over the Simeonites: Shephatiah son of Maakah;

17 over Levi: Hashabiah(N) son of Kemuel;

over Aaron: Zadok;(O)

18 over Judah: Elihu, a brother of David;

over Issachar: Omri son of Michael;

19 over Zebulun: Ishmaiah son of Obadiah;

over Naphtali: Jerimoth son of Azriel;

20 over the Ephraimites: Hoshea son of Azaziah;

over half the tribe of Manasseh: Joel son of Pedaiah;

21 over the half-tribe of Manasseh in Gilead: Iddo son of Zechariah;

over Benjamin: Jaasiel son of Abner;

22 over Dan: Azarel son of Jeroham.

These were the leaders of the tribes of Israel.

23 David did not take the number of the men twenty years old or less,(P) because the Lord had promised to make Israel as numerous as the stars(Q) in the sky. 24 Joab son of Zeruiah began to count the men but did not finish. God’s wrath came on Israel on account of this numbering,(R) and the number was not entered in the book[a] of the annals of King David.

The King’s Overseers

25 Azmaveth son of Adiel was in charge of the royal storehouses.

Jonathan son of Uzziah was in charge of the storehouses in the outlying districts, in the towns, the villages and the watchtowers.

26 Ezri son of Kelub was in charge of the workers who farmed the land.

27 Shimei the Ramathite was in charge of the vineyards.

Zabdi the Shiphmite was in charge of the produce of the vineyards for the wine vats.

28 Baal-Hanan the Gederite was in charge of the olive and sycamore-fig(S) trees in the western foothills.

Joash was in charge of the supplies of olive oil.

29 Shitrai the Sharonite was in charge of the herds grazing in Sharon.(T)

Shaphat son of Adlai was in charge of the herds in the valleys.

30 Obil the Ishmaelite was in charge of the camels.

Jehdeiah the Meronothite was in charge of the donkeys.

31 Jaziz the Hagrite(U) was in charge of the flocks.

All these were the officials in charge of King David’s property.

32 Jonathan, David’s uncle, was a counselor, a man of insight and a scribe. Jehiel son of Hakmoni took care of the king’s sons.

33 Ahithophel(V) was the king’s counselor.

Hushai(W) the Arkite was the king’s confidant. 34 Ahithophel was succeeded by Jehoiada son of Benaiah and by Abiathar.(X)

Joab(Y) was the commander of the royal army.

Footnotes

  1. 1 Chronicles 27:24 Septuagint; Hebrew number