Add parallel Print Page Options

Abweretsanso Bokosi la Chipangano

13 Davide anakambirana ndi akuluakulu ake, atsogoleri a anthu 1,000 ndi atsogoleri a anthu 100. Ndipo anati kwa gulu lonse la Israeli, “Ngati kukukomerani komanso ngati chili chifuniro cha Yehova Mulungu wathu, tiyeni titumize uthenga kulikonse kumene kuli abale athu ena onse ku dziko lonse la Israeli ndiponso kwa ansembe ndi Alevi amene ali nawo mʼmidzi yawo ndi madera odyetsera ziweto, kuti abwere adzakhale nafe. Tiyeni tibweretsenso Bokosi la Mulungu wathu kuno kwathu, pakuti nthawi ya Sauli sitinafunse za bokosili.” Gulu lonse linavomereza izi, pakuti anthu onse anaona kuti kunali kofunika kutero.

Kotero Davide anasonkhanitsa Aisraeli onse, kuchokera ku mtsinje wa Sihori ku Igupto mpaka ku Lebo Hamati, kuti abweretse Bokosi la Mulungu kuchokera ku Kiriati-Yearimu. Davide pamodzi ndi Aisraeli onse anapita ku Baalahi (Kiriati-Yearimu) ku Yuda kukatenga Bokosi la Yehova Mulungu, amene amakhala pakati pa akerubi. Limeneli ndiye Bokosi la Chipangano lomwe limadziwika ndi Dzina lake.

Iwo anachotsa Bokosi la Mulungu ku nyumba ya Abinadabu pa ngolo yatsopano. Uza ndi Ahiyo ndiwo ankayendetsa ngoloyo. Davide pamodzi ndi Aisraeli onse ankakondwerera ndi mphamvu zawo zonse pamaso pa Mulungu, poyimba nyimbo pogwiritsa ntchito azeze, apangwe, matambolini, maseche ndi malipenga.

Atafika pa malo opunthira tirigu ku Kidoni, Uza anatambalitsa dzanja lake kuti agwire bokosilo, chifukwa ngʼombe zinkafuna kugwa. 10 Yehova anapsera mtima Uza ndipo anamukantha chifukwa chogwira bokosilo. Choncho iyeyo anafera pomwepo pamaso pa Mulungu.

11 Ndipo Davide anakhumudwa chifukwa Yehova anakantha Uza ndipo mpaka lero malowo amatchedwa Perezi Uza.

12 Tsiku limenelo Davide anachita mantha ndi Mulungu ndipo anafunsa kuti, “Kodi Bokosi la Mulungu lingafike bwanji kwathu?” 13 Iye sanapitenso nalo Bokosi la Mulungu ku Mzinda wa Davide. Mʼmalo mwake anapita nalo ku nyumba ya Obedi-Edomu Mgiti. 14 Ndipo Bokosi la Mulungu linakhala mʼbanja la Obedi-Edomu mʼnyumba mwake kwa miyezi itatu ndipo Yehova anadalitsa nyumba yake ndi chilichonse chimene anali nacho.

Bringing Back the Ark(A)

13 David conferred with each of his officers, the commanders of thousands and commanders of hundreds. He then said to the whole assembly of Israel, “If it seems good to you and if it is the will of the Lord our God, let us send word far and wide to the rest of our people throughout the territories of Israel, and also to the priests and Levites who are with them in their towns and pasturelands, to come and join us. Let us bring the ark of our God back to us,(B) for we did not inquire(C) of[a] it[b] during the reign of Saul.” The whole assembly agreed to do this, because it seemed right to all the people.

So David assembled all Israel,(D) from the Shihor River(E) in Egypt to Lebo Hamath,(F) to bring the ark of God from Kiriath Jearim.(G) David and all Israel went to Baalah(H) of Judah (Kiriath Jearim) to bring up from there the ark of God the Lord, who is enthroned between the cherubim(I)—the ark that is called by the Name.

They moved the ark of God from Abinadab’s(J) house on a new cart, with Uzzah and Ahio guiding it. David and all the Israelites were celebrating with all their might before God, with songs and with harps, lyres, timbrels, cymbals and trumpets.(K)

When they came to the threshing floor of Kidon, Uzzah reached out his hand to steady the ark, because the oxen stumbled. 10 The Lord’s anger(L) burned against Uzzah, and he struck him down(M) because he had put his hand on the ark. So he died there before God.

11 Then David was angry because the Lord’s wrath had broken out against Uzzah, and to this day that place is called Perez Uzzah.[c](N)

12 David was afraid of God that day and asked, “How can I ever bring the ark of God to me?” 13 He did not take the ark to be with him in the City of David. Instead, he took it to the house of Obed-Edom(O) the Gittite. 14 The ark of God remained with the family of Obed-Edom in his house for three months, and the Lord blessed his household(P) and everything he had.

Footnotes

  1. 1 Chronicles 13:3 Or we neglected
  2. 1 Chronicles 13:3 Or him
  3. 1 Chronicles 13:11 Perez Uzzah means outbreak against Uzzah.