Add parallel Print Page Options

Kukonzekera Kumanga Nyumba ya Mulungu

Hiramu mfumu ya ku Turo atamva kuti Solomoni wadzozedwa kukhala mfumu mʼmalo mwa abambo ake Davide, anatumiza akazembe ake kwa Solomoni, chifukwa mfumu Hiramu inali pa ubale wabwino ndi Davide nthawi zonse. Solomoni anabweza mawu awa kwa Hiramu:

“Inu mukudziwa kuti chifukwa cha nkhondo zimene zinkachokera ku mbali zonse kulimbana ndi abambo anga, iwo sanathe kumangira Nyumba Yehova Mulungu wawo, mpaka Yehova atawayika adani awo pansi pa ulamuliro wawo. Koma tsopano Yehova Mulungu wanga wandipatsa mtendere mbali zonse za dziko ndipo ndilibe mdani kapena chovuta chilichonse. Choncho ine ndikufuna kumangira nyumba Yehova Mulungu wanga, monga momwe Iye anawuzira abambo anga Davide kuti, ‘Mwana wako amene ndidzamukhazike pa mpando waufumu mʼmalo mwako ndiye adzandimangire Nyumba.’

“Choncho lamulani kuti andidulire mikungudza ya ku Lebanoni. Anthu anga adzagwira ntchito imeneyo pamodzi ndi anthu anuwo, ndipo ine ndidzalipira anthu anuwo malipiro amene inu mungakhazikitse. Inu mukudziwa kuti ife tilibe anthu aluso locheka matabwa monga Asidoni.”

Hiramu anakondwa kwambiri atamva uthenga wa Solomoni ndipo anati, “Lero Yehova atamandike chifukwa wapatsa Davide mwana wanzeru kuti alamulire mtundu waukuluwu.”

Tsono Hiramu anabweza mawu awa kwa Solomoni:

“Ndalandira uthenga umene mwanditumizira ndipo ine ndidzachita zonse zimene mukufuna pokupatsani mitengo ya mkungudza ndi payini. Anthu anga adzatsika nayo kuchokera ku Lebanoni mpaka ku nyanja, ndipo adzayiyandamitsa pa nyanja mpaka ku malo amene munene. Kumeneko ndidzayimasula ndipo mudzayitenga. Ndipo inu mudzakwaniritsa chokhumba changa pondipatsa chakudya cha banja langa laufumu.”

10 Motero Hiramu anapereka kwa Solomoni mitengo yonse ya mkungudza ndi payini imene ankayifuna, 11 ndipo Solomoni anamupatsa Hiramu mitanga ya tirigu 20,000 ngati chakudya cha pa nyumba yake, kuwonjezera pa migolo ya mafuta a olivi yokwana 20,000. Solomoni anapitiriza kupereka zimenezi chaka ndi chaka. 12 Yehova anamupatsa Solomoni nzeru monga momwe analonjezera. Panali ubale wa mtendere pakati pa Solomoni ndi Hiramu, ndipo awiriwa anachita pangano.

13 Mfumu Solomoni inasonkhanitsa anthu ogwira ntchito ya thangata mʼdziko lonse la Israeli ndipo anthu athangatawo analipo 30,000. 14 Iye ankatumiza anthu 10,000 ku Lebanoni pa mwezi mosinthanasinthana, kotero kuti ankakhala ku Lebanoniko mwezi umodzi ndipo kwawo ankakhalako miyezi iwiri. Adoniramu ndiye ankayangʼanira ogwira ntchito yathangatayo. 15 Solomoni anali ndi anthu amtengatenga 70,000, anthu 80,000 osema miyala ku mapiri, 16 ndi akapitawo 33,000 amene ankayangʼanira ntchitoyi ndiponso anthu ogwira ntchito zina. 17 Molamulidwa ndi mfumu, anakumba ndi kusema miyala ikuluikulu kwambiri yoti akamangire maziko a Nyumba ya Mulungu. 18 Amisiri a Solomoni ndi a Hiramu ndiponso anthu a ku Gebala anasema miyala ndi kukonza matabwa ndi miyala yomangira Nyumba ya Mulungu.

Preparations for Building the Temple(A)

[a]When Hiram(B) king of Tyre heard that Solomon had been anointed king to succeed his father David, he sent his envoys to Solomon, because he had always been on friendly terms with David. Solomon sent back this message to Hiram:

“You know that because of the wars(C) waged against my father David from all sides, he could not build(D) a temple for the Name of the Lord his God until the Lord put his enemies under his feet.(E) But now the Lord my God has given me rest(F) on every side, and there is no adversary(G) or disaster. I intend, therefore, to build a temple(H) for the Name of the Lord my God, as the Lord told my father David, when he said, ‘Your son whom I will put on the throne in your place will build the temple for my Name.’(I)

“So give orders that cedars(J) of Lebanon be cut for me. My men will work with yours, and I will pay you for your men whatever wages you set. You know that we have no one so skilled in felling timber as the Sidonians.”

When Hiram heard Solomon’s message, he was greatly pleased and said, “Praise be to the Lord(K) today, for he has given David a wise son to rule over this great nation.”

So Hiram sent word to Solomon:

“I have received the message you sent me and will do all you want in providing the cedar and juniper logs. My men will haul them down from Lebanon to the Mediterranean Sea(L), and I will float them as rafts by sea to the place you specify. There I will separate them and you can take them away. And you are to grant my wish by providing food(M) for my royal household.”

10 In this way Hiram kept Solomon supplied with all the cedar and juniper logs he wanted, 11 and Solomon gave Hiram twenty thousand cors[b] of wheat as food(N) for his household, in addition to twenty thousand baths[c][d] of pressed olive oil. Solomon continued to do this for Hiram year after year. 12 The Lord gave Solomon wisdom,(O) just as he had promised him. There were peaceful relations between Hiram and Solomon, and the two of them made a treaty.(P)

13 King Solomon conscripted laborers(Q) from all Israel—thirty thousand men. 14 He sent them off to Lebanon in shifts of ten thousand a month, so that they spent one month in Lebanon and two months at home. Adoniram(R) was in charge of the forced labor. 15 Solomon had seventy thousand carriers and eighty thousand stonecutters in the hills, 16 as well as thirty-three hundred[e] foremen(S) who supervised the project and directed the workers. 17 At the king’s command they removed from the quarry(T) large blocks of high-grade stone(U) to provide a foundation of dressed stone for the temple. 18 The craftsmen of Solomon and Hiram(V) and workers from Byblos(W) cut and prepared the timber and stone for the building of the temple.

Footnotes

  1. 1 Kings 5:1 In Hebrew texts 5:1-18 is numbered 5:15-32.
  2. 1 Kings 5:11 That is, probably about 3,600 tons or about 3,250 metric tons
  3. 1 Kings 5:11 Septuagint (see also 2 Chron. 2:10); Hebrew twenty cors
  4. 1 Kings 5:11 That is, about 120,000 gallons or about 440,000 liters
  5. 1 Kings 5:16 Hebrew; some Septuagint manuscripts (see also 2 Chron. 2:2,18) thirty-six hundred