Add parallel Print Page Options

预言圣殿被毁(A)

13 耶稣从圣殿里出来的时候,有一个门徒对他说:“老师,请看,这是多么了不起的石头!多么了不起的建筑!” 耶稣对他说:“你看见这些宏伟的建筑吗?这里将没有一块石头会留在另一块石头上而不被拆毁的。”

终局的预兆(B)

耶稣在橄榄山上,面向圣殿坐着;彼得雅各约翰安得烈私下问他说: “请告诉我们,什么时候有这些事呢?这一切事将成的时候有什么预兆呢?” 耶稣说:“你们要谨慎,免得有人迷惑你们。 将有好些人冒我的名来,说‘我是基督’,并且要迷惑许多人。 当你们听见打仗和打仗的风声,不要惊慌;这些事必须发生,但这还不是终结。 民要攻打民,国要攻打国,多处必有地震、饥荒。这都是灾难[a]的起头。 但你们自己要谨慎;因为有人要把你们交给议会,并且你们在会堂里要受鞭打,又为我的缘故站在统治者和君王面前,对他们作见证。 10 然而,福音必须先传给万民。 11 有人把你们解送去受审的时候,不要事先担心说什么;到那时候,赐给你们什么话,你们就说什么;因为说话的不是你们,而是圣灵。 12 兄弟要把兄弟、父亲要把儿女置于死地;儿女要起来与父母为敌,害死他们; 13 而且你们要为我的名被众人憎恨。但坚忍到底的终必得救。”

大灾难(C)

14 “当你们看见那‘施行毁灭的亵渎者’站在不当站的地方(读这经的人要会意),那时,在犹太的,应当逃到山上; 15 在屋顶上的,不要下来,也不要进家里去拿东西; 16 在田里的,不要回去取衣裳。 17 在那些日子,怀孕的和奶孩子的就苦了。 18 你们要祈求,叫这事不在冬天发生。 19 因为,在那些日子必有灾难,自从 神创造万物直到如今,从没有这样的灾难,将来也不会有。 20 若不是主减少那些日子,凡血肉之躯的,就没有一个能得救;但是为了他所拣选的选民,他将那些日子减少了。 21 那时,若有人对你们说:‘看哪,基督在这里!看哪,在那里!’你们不要信。 22 因为假基督和假先知将要起来,显神迹奇事,如果可能,连选民也迷惑了。 23 你们要谨慎!凡事我都预先告诉你们了。”

人子的来临(D)

24 “在那些日子、那灾难以后,
太阳要变黑,月亮也不放光,
25 众星要从天上坠落,
天上的万象都要震动。

26 那时,他们要看见人子带着大能力和荣耀驾云来临。 27 他要差遣天使,从四方,从地极直到天边,召集他的选民。”

从无花果树学功课(E)

28 “你们要从无花果树学习功课:当树枝发芽长叶的时候,你们就知道夏天近了。 29 同样,当你们看见这些事发生,就知道那时候近了,就在门口了。 30 我实在告诉你们,这世代还没有过去,这一切都要发生。 31 天地要废去,我的话却绝不废去。”

那日那时没有人知道(F)

32 “但那日子,那时辰,没有人知道,连天上的天使也不知道,子也不知道,惟有父知道。 33 你们要谨慎,要警醒[b],因为你们不知道那时刻几时来到。 34 这事正如一个人离家远行,授权给仆人们,分派各人的工作,又吩咐看门的警醒。 35 所以,你们要警醒,因为你们不知道这家的主人什么时候来,是晚上,或半夜,或鸡叫时,或早晨, 36 免得他忽然来到,看见你们睡着了。 37 我对你们所说的话,也是对众人说的:要警醒!”

Footnotes

  1. 13.8 “灾难”:原文直译“生产的阵痛”。
  2. 13.33 有古卷加“祈祷”。

Zizindikiro za Kutha kwa Masiku Yomaliza

13 Iye atachoka mʼNyumba ya Mulungu, mmodzi wa ophunzira ake anati kwa Iye, “Aphunzitsi taonani! Miyala ikuluikulu! Nyumba zikongolerenji!”

Yesu anayankha kuti, “Kodi mukuziona nyumba zikuluzikuluzi? Palibe mwala ndi umodzi pano umene udzakhala pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”

Yesu atakhala pansi pa phiri la Olivi moyangʼanana ndi Nyumba ya Mulungu, Petro, Yakobo, Yohane ndi Andreya anamufunsa Iye pambali kuti, “Tatiwuzani, izi zidzachitika liti? Nanga chizindikiro chakuti zatsala pangʼono kukwaniritsidwa chidzakhala chiyani?”

Yesu anawawuza kuti, “Chenjerani kuti wina asakunyengeni. Anthu ambiri adzabwera mʼdzina langa, nadzati, ‘Ine ndi Iyeyo,’ ndipo adzanamiza anthu ambiri. Pamene mudzamva zankhondo ndi mbiri zankhondo, musadzadzidzimuke. Zinthu zotere ziyenera kuchitika, koma sikuti chimaliziro chafika kale ayi. Mtundu udzawukira mtundu unzake, ndi ufumu kuwukira ufumu unzake. Kudzakhala zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana, ndi njala. Izi ndi chiyambi chabe cha zowawa monga mayi pobereka.

“Muyenera kukhala tcheru. Mudzaperekedwa ku mabwalo oweruza ndi kukwapulidwa mwankhanza mʼmasunagoge. Mudzayima pamaso pa abwanamkubwa ndi mafumu monga mboni kwa iwo chifukwa cha Ine. 10 Ndipo Uthenga Wabwino uyenera kuyamba walalikidwa kwa anthu a mitundu yonse. 11 Nthawi iliyonse pamene mwamangidwa ndi kuyimbidwa mlandu, musadandaule za zimene mudzanena. Zimene mudzapatsidwe pa nthawiyo yankhulani; pakuti sindinu amene mudzayankhula, koma Mzimu Woyera.

12 “Mʼbale adzapereka mʼbale kuti aphedwe, ndipo abambo adzapereka mwana wawo. Ana adzawukira makolo awo ndi kuwapereka kuti aphedwe. 13 Anthu onse adzakudani chifukwa cha Ine, koma amene adzalimbika mpaka potsiriza, ameneyo ndiye adzapulumuke.

14 “Mukadzaona ‘chinthu chonyansa chosakaza’ chitayima pa malo amene si ake, owerenga azindikire. Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire kumapiri. 15 Aliyense amene ali pa denga la nyumba yake asatsike kapena kulowa mʼnyumba kukatenga kanthu kalikonse. 16 Aliyense amene ali ku munda asabwerere kukatenga mkanjo wake. 17 Kudzakhala koopsa mʼmasiku amenewo kwa amayi oyembekezera ndi amayi oyamwitsa! 18 Pempherani kuti zimenezi zisadzachitike nthawi yozizira, 19 chifukwa masiku amenewo adzakhala owawitsa osafanana ndi ena kuyambira pachiyambi, pamene Mulungu analenga dziko, kufikira lero ndipo sadzafanananso ndi ena. 20 Ambuye akanapanda kufupikitsa masikuwo, palibe amene akanapulumuka. Koma chifukwa cha osankhidwiratu, amene anawasankha, Iye anawafupikitsa. 21 Pa nthawi imeneyo, ngati wina adzati kwa inu, ‘Taonani, Khristu ali kuno, kapena, Taonani, uyo ali apoyo!’ musakhulupirire. 22 Pakuti akhristu onama ndi aneneri onama adzaonekera ndipo adzachita zizindikiro ndi zodabwitsa kuti anyenge osankhidwiratu ngati kutakhala kotheka kutero. 23 Choncho khalani tcheru; ndakuwuzani zonse nthawi isanafike.

24 “Koma masiku amenewo, masautsowo atatha,

“ ‘dzuwa lidzada,
    ndipo mwezi sudzawala;
25 nyenyezi zidzagwa kuchokera ku thambo,
    ndipo mayiko mumlengalenga adzagwedezeka!’

26 “Nthawi imeneyo anthu adzaona Mwana wa Munthu akubwera mʼmitambo ndi mphamvu yayikulu ndi ulemerero. 27 Ndipo adzatuma angelo ake kukasonkhanitsa osankhidwiratu ake ku mphepo zinayi, kuyambira kumalekezero a dziko lapansi mpaka ku malekezero ake enanso.

28 “Tsopano phunzirani phunziro ili kuchokera ku mtengo wamkuyu. Pamene msonga za nthambi zake zikhala za nthete ndipo masamba ake ayamba kuphukira, mumadziwa kuti dzinja layandikira. 29 Momwenso pamene muona zinthu izi zikuchitika, dziwani kuti wayandikira, ali pa khomo. 30 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti mʼbado uno sudzatha mpaka zinthu zonsezi zitachitika. 31 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”

Tsiku ndi Ora Sizikudziwika

32 “Palibe amene akudziwa za tsikulo kapena nthawi, ngakhale angelo akumwamba, kapena Mwana, koma Atate wokha. 33 Khalani maso! Khalani tcheru! Simudziwa pamene nthawi imeneyo idzafike. 34 Zili ngati munthu amene akuchokapo. Amasiyira nyumba yake antchito ake, aliyense ndi ntchito yake; ndi kumuwuza wa pa khomo kuti azikhala maso.

35 “Inunso muyenera kukhala maso chifukwa simukudziwa nthawi imene mwini nyumba adzabwere, kaya madzulo, kapena pakati pa usiku, kapena tambala akulira, kapena mʼbandakucha. 36 Ngati atabwera mwadzidzidzi, asadzakupezeni inu muli mtulo. 37 Zimene ndikunena kwa inu, ndikunena kwa aliyense: ‘Khalani tcheru!’ ”