Mateyu 11
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Otumidwa ndi Yohane Mʼbatizi
11 Ndipo Yesu atamaliza kulangiza ophunzira ake khumi ndi awiri aja, anachoka kumeneko kupita kukaphunzitsa ndi kukalalikira ku mizinda ya ku Galileya.
2 Yohane ali mʼndende anamva zimene Khristu ankachita, ndipo anatumiza ophunzira ake kukamufunsa Iye. 3 Anamufunsa kuti, “Kodi Inu ndinu uja ankanena kuti mudzabwerayu kapena tidikire wina?”
4 Yesu anayankha kuti, “Bwererani ndi kukamuwuza Yohane zimene mwamva ndi kuona. 5 Osaona akuona, olumala akuyenda, akhate akuchiritsidwa, osamva akumva, akufa akuukitsidwa ndipo Uthenga Wabwino ukulalikidwa kwa osauka. 6 Odala ndi munthu amene sakhumudwa chifukwa cha Ine.”
7 Pamene ophunzira a Yohane ankachoka, Yesu anayamba kuyankhula kwa gulu la anthu za Yohane kuti, “Kodi munkapita ku chipululu kuti mukaone chiyani? Kodi bango logwedezeka ndi mphepo? 8 Nanga munkapita kukaona chiyani, munthu wovala zokongola? Ayi, wovala zokongola amakhala mʼnyumba za mafumu. 9 Nanga munkapita kukaona chiyani? Mneneri kodi? Inde ndikuwuzani kuti munkakaona woposa mneneri. 10 Uyu ndi amene malemba akunena za iye kuti,
“Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu
amene adzakonza njira yanu.
11 Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti pakati pa obadwa ndi mkazi sipanaoneke wina aliyense wamkulu woposa Yohane Mʼbatizi; komatu amene ndi wamngʼono kwambiri mu ufumu wakumwamba ndi wamkulu koposa iye. 12 Kuyambira masiku a Yohane Mʼbatizi mpaka tsopano, ufumu wakumwamba ndi wolimbirana ndipo anthu amphamvu okha ndi amene akuwulanda. 13 Pakuti aneneri onse ndi malamulo ananenera kufikira nthawi ya Yohane. 14 Ndipo ngati inu mufuna kulandira izi, iyeyu ndi Eliya amene ankanena kuti adzabwera uja. 15 Iye amene ali ndi makutu amve.
16 “Kodi mʼbado uwu ndingawufanizire ndi chiyani? Uli ngati ana opezeka mʼmisika amene akuyitana anzawo nʼkumati:
17 “ ‘Tinakuyimbirani zitoliro,
koma inu simunavine;
ife tinayimba nyimbo zamaliro,
koma inu simunalire.’
18 Pakuti Yohane sanabwerere kudya kapena kumwa koma iwo ankanena kuti, ‘Iye anali ndi chiwanda.’ 19 Mwana wa Munthu anabwera ndi kumadya ndi kumwa koma iwo akuti, ‘Munthu wadyera, woledzera, bwenzi la amisonkho ndi bwenzi la ochimwa.’ Koma nzeru imatsimikizika kuti ndi yolondola mwa ntchito zake.”
Tsoka la Mizinda Itatu Yosatembenuka mtima
20 Pamenepo Yesu anayamba kudzudzula mizinda imene zodabwitsa zake zambiri zinachitikamo, chifukwa chakuti sinatembenuke mtima. 21 “Tsoka kwa iwe Korazini! Tsoka kwa iwe Betisaida! Ngati zodabwitsa zimene zinachitika mwa iwe zikanachitidwa mu Turo ndi Sidoni, iwo akanalapa kale atavala ziguduli ndi kudzola phulusa. 22 Koma ndikuwuzani inu kuti pa tsiku lachiweruzo mlandu wa Turo ndi Sidoni udzachepako kusiyana ndi wanu. 23 Ndipo iwe Kaperenawo, kodi udzakwezedwa kufika kumwamba? Ayi, udzatsitsidwa mpaka pansi kufika ku Hade. Ngati zodabwitsa zimene zinachitika mwa iwe, zikanachitika mu Sodomu, bwenzi iye alipo kufikira lero. 24 Koma Ine ndikuwuzani kuti pa tsiku la chiweruziro mlandu wa Sodomu udzachepako kusiyana ndi wanu.”
Goli la Khristu
25 Pa nthawi imeneyo Yesu anati, “Ine ndikukuyamikani Inu Atate Ambuye akumwamba ndi dziko lapansi, chifukwa Inu mwawabisira zinthu izi anzeru ndi ophunzira ndi kuziwulula kwa ana angʼonoangʼono. 26 Inde, Atate, ichi chinali chokukomerani Inu.
27 “Zinthu zonse zapatsidwa kwa Ine ndi Atate anga. Palibe mmodzi amene adziwa Mwana kupatula Atate ndipo palibe mmodzi amene adziwa Atate kupatula Mwana ndi kwa iwo amene Mwana awasankha kuwawululira.
28 “Idzani kwa Ine, inu nonse otopa ndi olemedwa ndipo Ine ndidzakupatsani mpumulo. 29 Senzani goli langa ndipo phunzirani kwa Ine, pakuti ndine wofatsa ndi wodzichepetsa. Ndipo inu mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu. 30 Pakuti goli langa ndi losavuta ndipo katundu wanga ndi wopepuka.”
Matthew 11
English Standard Version
Messengers from John the Baptist
11 When Jesus had finished instructing his twelve disciples, he went on from there to teach and preach in their cities.
2 (A)Now when John heard (B)in prison about the deeds of (C)the Christ, he sent word by (D)his disciples 3 and said to him, “Are you (E)the one who is to come, or shall we (F)look for another?” 4 And Jesus answered them, “Go and tell John what you hear and see: 5 (G)the blind receive their sight and the lame walk, lepers[a] are cleansed and the deaf hear, and the dead are raised up, and (H)the poor have good news preached to them. 6 And blessed is the one who (I)is not offended by me.”
7 As they went away, Jesus began to speak to the crowds concerning John: “What did you go out (J)into the wilderness to see? (K)A reed shaken by the wind? 8 What then did you go out to see? A man[b] dressed in soft clothing? Behold, those who wear soft clothing are in kings' houses. 9 What then did you go out to see? (L)A prophet?[c] Yes, I tell you, and more than a prophet. 10 This is he of whom it is written,
(M)“‘Behold, I send my messenger before your face,
who will prepare your way before you.’
11 Truly, I say to you, among those born of women there has arisen no one greater than John the Baptist. Yet the one who is least in the kingdom of heaven is greater than he. 12 (N)From the days of John the Baptist until now the kingdom of heaven has suffered violence,[d] and the violent take it by force. 13 (O)For all the Prophets and the Law prophesied until John, 14 and if you are willing to accept it, he is (P)Elijah who is to come. 15 (Q)He who has ears to hear,[e] let him hear.
16 “But to what shall I compare this generation? It is like children sitting in the marketplaces and calling to their playmates,
17 “‘We played the flute for you, and you did not dance;
we sang a dirge, and you did not mourn.’
18 For John came (R)neither eating (S)nor drinking, and they say, ‘He has a demon.’ 19 The Son of Man came (T)eating and drinking, and they say, ‘Look at him! A glutton and a drunkard, (U)a friend of (V)tax collectors and sinners!’ Yet wisdom is justified by her deeds.”[f]
Woe to Unrepentant Cities
20 (W)Then he began to denounce the cities where most of his mighty works had been done, because they did not repent. 21 (X)“Woe to you, Chorazin! Woe to you, Bethsaida! For if the mighty works done in you had been done in (Y)Tyre and Sidon, they would have repented long ago in sackcloth and ashes. 22 (Z)But I tell you, it will be more bearable on (AA)the day of judgment for (AB)Tyre and Sidon than for you. 23 And you, (AC)Capernaum, will you be exalted to heaven? You will be brought down to (AD)Hades. For if the mighty works done in you had been done in Sodom, it would have remained until this day. 24 (AE)But I tell you that (AF)it will be more tolerable on (AG)the day of judgment for the land of Sodom than for you.”
Come to Me, and I Will Give You Rest
25 (AH)At that time Jesus declared, “I thank you, Father, (AI)Lord of heaven and earth, that (AJ)you have hidden these things from the wise and understanding and (AK)revealed them to little children; 26 yes, Father, for such was your (AL)gracious will.[g] 27 (AM)All things have been handed over to me by my Father, and no one knows the Son (AN)except the Father, and no one knows the Father except the Son and anyone (AO)to whom the Son chooses to reveal him. 28 (AP)Come to (AQ)me, all who labor and are (AR)heavy laden, and I will give you rest. 29 Take my yoke upon you, and (AS)learn from me, for I am (AT)gentle and lowly in heart, and (AU)you will find rest for your souls. 30 For (AV)my yoke is easy, and my burden is light.”
Footnotes
- Matthew 11:5 Leprosy was a term for several skin diseases; see Leviticus 13
- Matthew 11:8 Or Why then did you go out? To see a man
- Matthew 11:9 Some manuscripts Why then did you go out? To see a prophet?
- Matthew 11:12 Or has been coming violently
- Matthew 11:15 Some manuscripts omit to hear
- Matthew 11:19 Some manuscripts children (compare Luke 7:35)
- Matthew 11:26 Or for so it pleased you well
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
The ESV® Bible (The Holy Bible, English Standard Version®), © 2001 by Crossway, a publishing ministry of Good News Publishers. ESV Text Edition: 2025.
