Add parallel Print Page Options

91 Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba
    adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.
Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa,
    Mulungu wanga amene ndimadalira.”

Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje
    ndi ku mliri woopsa;
Adzakuphimba ndi nthenga zake,
    ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo;
    kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.
Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku,
    kapena muvi wowuluka masana,
kapena mliri umene umayenda mu mdima,
    kapena zowononga za pa nthawi ya masana.
Anthu 1,000 atha kufa pambali pako,
    anthu 10,000 kudzanja lako lamanja,
    koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.
Udzapenya ndi maso ako
    ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.

Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo;
    wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.
10 Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera,
    zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.
11 Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe,
    kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;
12 ndipo adzakunyamula ndi manja awo,
    kuti phazi lako lisagunde pa mwala.
13 Udzapondaponda mkango ndi njoka,
    udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.

14 “Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa;
    ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.
15 Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha;
    ndidzakhala naye pa mavuto,
    ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.
16 Ndidzamupatsa moyo wautali
    ndi kumupulumutsa.”

Safety of Abiding in the Presence of God

91 He (A)who dwells in the secret place of the Most High
Shall abide (B)under the shadow of the Almighty.
(C)I will say of the Lord, “He is my refuge and my fortress;
My God, in Him I will trust.”

Surely (D)He shall deliver you from the snare of the [a]fowler
And from the perilous pestilence.
(E)He shall cover you with His feathers,
And under His wings you shall take refuge;
His truth shall be your shield and [b]buckler.
(F)You shall not be afraid of the terror by night,
Nor of the arrow that flies by day,
Nor of the pestilence that walks in darkness,
Nor of the destruction that lays waste at noonday.

A thousand may fall at your side,
And ten thousand at your right hand;
But it shall not come near you.
Only (G)with your eyes shall you look,
And see the reward of the wicked.

Because you have made the Lord, who is (H)my refuge,
Even the Most High, (I)your dwelling place,
10 (J)No evil shall befall you,
Nor shall any plague come near your dwelling;
11 (K)For He shall give His angels charge over you,
To keep you in all your ways.
12 In their hands they shall [c]bear you up,
(L)Lest you [d]dash your foot against a stone.
13 You shall tread upon the lion and the cobra,
The young lion and the serpent you shall trample underfoot.

14 “Because he has set his love upon Me, therefore I will deliver him;
I will [e]set him on high, because he has (M)known My name.
15 He shall (N)call upon Me, and I will answer him;
I will be (O)with him in trouble;
I will deliver him and honor him.
16 With [f]long life I will satisfy him,
And show him My salvation.”

Footnotes

  1. Psalm 91:3 One who catches birds in a trap or snare
  2. Psalm 91:4 A small shield
  3. Psalm 91:12 lift
  4. Psalm 91:12 strike
  5. Psalm 91:14 exalt him
  6. Psalm 91:16 Lit. length of days