诗篇 47
Chinese Contemporary Bible (Simplified)
至高的主宰
可拉后裔的诗,交给乐长。
47 万民啊,你们要鼓掌,
向上帝高声欢呼!
2 因为至高者耶和华当受敬畏,
祂是普天下的大君王。
3 祂使列国降服于我们,
让列邦伏在我们脚下。
4 祂为我们选定产业,
就是祂所爱的雅各引以为荣的产业。(细拉)
5 在欢呼声中,上帝登上宝座;
在号角声中,耶和华登上宝座。
6 要颂赞,颂赞上帝!
要颂赞,颂赞我们的君王!
7 因为上帝是普天下的君王,
要向祂唱赞美的乐章。
8 祂坐在圣洁的宝座上治理列国。
9 列邦的首领聚集在一起,
要做亚伯拉罕之上帝的子民,
因为上帝是主宰天下的君王,
祂至高无上。
Masalimo 47
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.
47 Ombani mʼmanja, inu anthu onse;
fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
2 Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba;
Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
3 Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu;
anayika anthu pansi pa mapazi athu.
4 Iye anatisankhira cholowa chathu,
chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda.
Sela
5 Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe,
Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
6 Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando;
imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
7 Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi;
imbirani Iye salimo la matamando.
8 Mulungu akulamulira mitundu ya anthu;
Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
9 Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana
monga anthu a Mulungu wa Abrahamu,
pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu;
Iye wakwezedwa kwakukulu.
Chinese Contemporary Bible Copyright © 1979, 2005, 2007, 2011 by Biblica® Used by permission. All rights reserved worldwide.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.