Masalimo 43
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
43 Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu;
ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza;
mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga.
Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine?
Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira,
woponderezedwa ndi mdani?
3 Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu
kuti zinditsogolere;
mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera,
kumalo kumene inu mumakhala.
4 Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu,
kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa.
Ndidzakutamandani ndi zeze,
Inu Mulungu wanga.
5 Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga?
Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga?
Khulupirira Mulungu,
pakuti ndidzamutamandabe Iye,
Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.
Chinese Contemporary Bible Copyright © 1979, 2005, 2007, 2011 by Biblica® Used by permission. All rights reserved worldwide.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.