Add parallel Print Page Options

耶和華之受膏者為王

外邦為什麼爭鬧,萬民為什麼謀算虛妄的事?
世上的君王一齊起來,臣宰一同商議,要抵擋耶和華並他的受膏者,
說:「我們要掙開他們的捆綁,脫去他們的繩索!」
那坐在天上的必發笑,主必嗤笑他們。
那時,他要在怒中責備他們,在烈怒中驚嚇他們,
說:「我已經立我的君在錫安我的聖山上了。」
受膏者說:「我要傳聖旨。耶和華曾對我說:『你是我的兒子,我今日生你。
你求我,我就將列國賜你為基業,將地極賜你為田產。
你必用鐵杖打破他們,你必將他們如同窯匠的瓦器摔碎。』」
10 現在你們君王應當醒悟,你們世上的審判官該受管教!
11 當存畏懼侍奉耶和華,又當存戰兢而快樂。
12 當以嘴親子,恐怕他發怒,你們便在道中滅亡,因為他的怒氣快要發作。凡投靠他的,都是有福的!

Nʼchifukwa chiyani anthu a mitundu ina akufuna kuchita chiwembu?
    Akonzekeranji zopanda pake anthu?
Mafumu a dziko lapansi akugwirizana nazo;
    ndipo olamulira asonkhana pamodzi
kulimbana ndi Ambuye
    ndi wodzozedwa wakeyo.
Iwo akunena kuti, “Tiyeni timasule magoli awo
    ndipo titaye zingwe zawo.”

Wokhala mmwamba akuseka;
    Ambuye akuwanyoza iwowo.
Ndipo iye awadzudzula mu mkwiyo wake
    ndi kuwaopseza mu ukali wake, kunena kuti,
“Ine ndakhazikitsa mfumu yanga
    pa Ziyoni, phiri langa loyera.”

Ine ndidzalengeza zimene Yehova walamula:

Iye anati kwa Ine, “Iwe ndiwe mwana wanga;
    lero Ine ndakhala Atate ako.
Tandipempha,
    ndipo ndidzachititsa kuti mitundu ya anthu ikhale cholowa chako;
    malekezero a dziko lapansi kuti akhale chuma chako.
Iweyo udzawalamulira ndi ndodo yaufumu yachitsulo;
    udzawaphwanya zidutswazidutswa ngati zowumba zadothi.”

10 Kotero, inu mafumu, chenjerani;
    chenjezedwani, inu olamulira a dziko lapansi.
11 Tumikirani Yehova mwa mantha
    ndi kukondwerera ulamuliro wake monjenjemera.
12 Mpsopsoneni mwanayo kuti angakwiye;
    kuti mungawonongedwe mʼnjira zanu,
pakuti ukali wake utha kuuka mʼkanthawi kochepa.
    Odala ndi onse amene amathawira kwa Iye.