Aroma 5
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Mtendere ndi Chimwemwe
5 Tsopano popeza tayesedwa olungama mwa chikhulupiriro, tili ndi mtendere ndi Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. 2 Iyeyo ndiye amene anatsekulira njira mwachikhulupiriro yolowera mʼchisomo mʼmene takhazikikamo. Ndipo tikukondwerera chiyembekezo cha ulemerero wa Mulungu. 3 Koma si pokhapo ayi, koma ife tikukondweranso mʼmasautso athu chifukwa tikudziwa kuti masautso amatiphunzitsa kupirira. 4 Ndipo kupirira kumabweretsa makhalidwe, makhalidwe amabweretsa chiyembekezo. 5 Ndipo chiyembekezo chimenechi sichitikhumudwitsa chifukwa Mulungu mwa Mzimu Woyera, amene Iye anatipatsa, wadzaza mʼmitima mwathu ndi chikondi chake.
6 Pakuti pa nthawi yake, tikanali ochimwa, Khristu anatifera anthu osapembedzafe. 7 Sizichitika kawirikawiri kuti munthu wina afere munthu wolungama, ngakhale kuti chifukwa cha munthu wabwino wina atha kulimba mtima kumufera. 8 Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.
9 Popeza chifukwa cha magazi ake ife tapezeka olungama pamaso pa Mulungu, Iyeyo adzatipulumutsa koposa kotani ku mkwiyo wa Mulungu. 10 Pakuti pamene tinali adani a Mulungu, tinayanjanitsidwa ndi Iye kudzera mu imfa ya Mwana wake. Nanga tidzapulumutsidwa bwanji kudzera mʼmoyo wake, titayanjanitsidwa naye? 11 Sikuti izi zili chomwechi chabe, koma timakondweranso mwa Mulungu kudzera mwa Ambuye athu Yesu Khristu. Kudzera mwa Iye, ife tsopano tayanjanitsidwa ndi Mulungu.
Imfa Kudzera mwa Adamu, Moyo Kudzera mwa Yesu
12 Choncho monga momwe tchimo linalowa mʼdziko lapansi kudzera mwa munthu mmodzi, ndi imfa kudzera mu tchimo, mʼnjirayi imfa inafika kwa anthu onse pakuti onse anachimwa. 13 Pakuti Malamulo asanaperekedwe, tchimo linali mʼdziko lapansi. Koma pamene palibe Malamulo, tchimo silitengedwa kukhala tchimo. 14 Komabe, imfa inalamulira kuyambira nthawi ya Adamu mpaka nthawi ya Mose. Inalamulira ngakhalenso pa iwo amene sanachimwe posamvera Malamulo monga anachitira Adamu. Adamuyo amene anali chifaniziro cha wina amene ankabwera.
15 Koma sitingafananitse mphatso yaulereyo ndi kuchimwa kwa anthu. Pakuti ngati anthu ambiri anafa chifukwa cha kuchimwa kwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga chisomo cha Mulungu ndi mphatso zomwe zinabwera ndi chisomo cha munthu mmodzi, Yesu Khristu, ndi kusefukira kwa ambiri! 16 Ndiponso, mphatso ya Mulungu sifanana ndi zotsatira za kuchimwa kwa munthu mmodzi. Chiweruzo chinatsatira tchimo la munthu mmodzi ndi kubweretsa kutsutsidwa koma mphatso inatsatira zolakwa zambiri ndi kubweretsa kulungamitsidwa. 17 Pakuti ngati, chifukwa cha kulakwa kwa munthu mmodziyo, imfa inalamulira kudzera mwa munthu mmodziyo, kuli koposa bwanji nanga kwa iwo amene adzalandira chisomo chochuluka ndi mphatso yachilungamo, adzalamulira mʼmoyo kudzera mwa munthu mmodzi, Yesu Khristu.
18 Choncho monga tchimo limodzi linabweretsa kutsutsika pa anthu onse, chimodzimodzinso ntchito imodzi yolungama inabweretsa chilungamo kwa anthu onse ndi kuwapatsa moyo. 19 Pakuti kusamvera kwa munthu mmodzi kunasandutsa anthu ambiri kukhala ochimwa, chimodzimodzinso anthu ambiri adzasanduka olungama kudzera mwa munthu mmodzinso.
20 Malamulo a Mulungu anaperekedwa ndi cholinga chakuti anthu onse azindikire kuchuluka kwa machimo awo. Koma pamene machimo anachuluka, chisomo chinachuluka koposa. 21 Choncho monga momwe tchimo linkalamulira anthu ndi kubweretsa imfa pa iwo, chomwecho kunali koyenera kuti chisomo chilamulire pobweretsa chilungamo kwa anthu, ndi kuwafikitsa ku moyo wosatha mwa Yesu Khristu Ambuye athu.
Romans 5
GOD’S WORD Translation
We Are at Peace with God because of Jesus
5 Now that we have God’s approval by faith, we have peace with God because of what our Lord Jesus Christ has done. 2 Through Christ we can approach God [a] and stand in his favor.[b] So we brag because of our confidence that we will receive glory from God. 3 But that’s not all. We also brag when we are suffering. We know that suffering creates endurance, 4 endurance creates character, and character creates confidence. 5 We’re not ashamed to have this confidence, because God’s love has been poured into our hearts by the Holy Spirit, who has been given to us.
6 Look at it this way: At the right time, while we were still helpless, Christ died for ungodly people. 7 Finding someone who would die for a godly person is rare. Maybe someone would have the courage to die for a good person. 8 Christ died for us while we were still sinners. This demonstrates God’s love for us.
9 Since Christ’s blood has now given us God’s approval, we are even more certain that Christ will save us from God’s anger. 10 If the death of his Son restored our relationship with God while we were still his enemies, we are even more certain that, because of this restored relationship, the life of his Son will save us. 11 In addition, our Lord Jesus Christ lets us continue to brag about God. After all, it is through Christ that we now have this restored relationship with God.
A Comparison between Adam and Christ
12 Sin came into the world through one person, and death came through sin. So death spread to everyone, because everyone sinned. 13 Sin was in the world before there were any laws. But no record of sin can be kept when there are no laws. 14 Yet, death ruled from the time of Adam to the time of Moses, even over those who did not sin in the same way Adam did when he disobeyed. Adam is an image of the one who would come.
15 There is no comparison between ⌞God’s⌟ gift and ⌞Adam’s⌟ failure. If humanity died as the result of one person’s failure, it is certainly true that God’s kindness [c] and the gift given through the kindness of one person, Jesus Christ, have been showered on humanity.
16 There is also no comparison between ⌞God’s⌟ gift and the one who sinned. The verdict which followed one person’s failure condemned everyone. But, even after many failures, the gift brought God’s approval. 17 It is certain that death ruled because of one person’s failure. It’s even more certain that those who receive God’s overflowing kindness and the gift of his approval will rule in life because of one person, Jesus Christ.
18 Therefore, everyone was condemned through one failure, and everyone received God’s life-giving approval through one verdict. 19 Clearly, through one person’s disobedience humanity became sinful, and through one person’s obedience humanity will receive God’s approval. 20 The laws in Moses’ Teachings were added to increase the failure. But where sin increased, God’s kindness increased even more. 21 As sin ruled by bringing death, God’s kindness would rule by bringing us his approval. This results in our living forever because of Jesus Christ our Lord.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Copyright © 1995, 2003, 2013, 2014, 2019, 2020 by God’s Word to the Nations Mission Society. All rights reserved.