约翰一书 4
Chinese Contemporary Bible (Simplified)
灵的分辨
4 亲爱的弟兄姊妹,不要什么灵都信,总要试验那些灵是否出于上帝,因为世上已经出现了许多假先知! 2 任何灵若承认耶稣基督曾降世为人,就是从上帝来的,你们可以凭这一点认出上帝的灵。 3 任何灵若不承认耶稣,就不是从上帝来的,而是敌基督者的灵。以前你们听说敌基督者要来,现在他已经在世上了。
4 孩子们,你们属于上帝,你们已经胜过了那些假先知,因为在你们里面的圣灵比在世上运行的邪灵更有能力。 5 他们属于世界,所以他们谈论的都是世俗的事,世人也听从他们。 6 我们属于上帝,认识上帝的人听从我们,不属于上帝的人不听从我们。这样,我们就可以分辨真理的灵和错谬的灵。
上帝是爱
7 亲爱的弟兄姊妹,我们应当彼此相爱,因为爱是从上帝来的。凡有爱心的人都是从上帝生的,并且认识上帝。 8 没有爱心的人不认识上帝,因为上帝就是爱。 9 上帝差遣祂独一的儿子到世上来,是为了叫我们靠着祂得到生命。这就显明了上帝对我们的爱。 10 不是我们爱上帝,而是上帝爱我们,并且差遣祂儿子为我们的罪作了赎罪祭,这就是爱。
11 亲爱的弟兄姊妹,上帝既然这样爱我们,我们也应该彼此相爱。 12 从来没有人见过上帝,如果我们彼此相爱,上帝就住在我们里面,祂的爱就在我们里面得到成全。
13 上帝将祂的灵赐给了我们,所以我们知道自己住在祂里面,祂也住在我们里面。 14 我们看见过,现在做见证:父差遣了祂的儿子成为世人的救主。 15 无论是谁,他若承认耶稣是上帝的儿子,上帝必住在他里面,他也住在上帝里面。 16 我们已经认识并且相信了上帝对我们的爱。
上帝就是爱,住在爱中的,就是住在上帝里面,上帝也住在他里面。 17 这样,爱在我们里面得到成全,使我们在审判的日子可以坦然无惧,因为我们在这世上以基督为榜样。 18 爱里没有恐惧,纯全的爱能驱除恐惧,因为恐惧意味着怕受惩罚。人若心里恐惧,就表示他尚未明白那纯全的爱。
19 我们爱,因为上帝先爱了我们。 20 若有人说“我爱上帝”,却恨自己的弟兄姊妹,这人就是说谎话,因为人若不爱看得见的弟兄姊妹,又怎能爱看不见的上帝呢? 21 爱上帝的人也应该爱弟兄姊妹,这是上帝给我们的命令。
1 Yohane 4
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kuyesa Mizimu
4 Anzanga okondedwa, musakhulupirire mzimu uliwonse, koma yesani mizimu ngati ikuchokera kwa Mulungu, chifukwa aneneri onama ambiri afalikira mʼdziko lapansi. 2 Mungathe kuzindikira Mzimu wa Mulungu motere: Mzimu uliwonse umene umavomereza kuti Yesu Khristu anabwera mʼthupi, ndi wochokera kwa Mulungu, 3 koma mzimu uliwonse umene suvomereza Yesu, siwochokera kwa Mulungu. Uwu ndi mzimu wa wokana Khristu umene munawumva kuti ukubwera ndipo ngakhale tsopano wabwera kale mʼdziko lapansi.
4 Inu ana okondedwa, ndinu ochokera kwa Mulungu ndipo mwawagonjetsa aneneri onyengawa, chifukwa Iye amene ali mwa inu ndi wamkulu kuposa amene ali mʼdziko lapansi. 5 Aneneri onyengawa ndi ochokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake amayankhula za dziko lapansi, ndipo dziko lapansi limawamvera. 6 Ife ndi ochokera kwa Mulungu, ndipo aliyense amene amadziwa Mulungu amamvera zimene timayankhula. Koma aliyense amene sachokera kwa Mulungu samvera zimene timayankhula. Mmenemu ndiye mmene timasiyanitsira pakati pa mzimu wachoonadi ndi Mzimu wachinyengo.
Mulungu ndiye Chikondi
7 Anzanga okondedwa, tiyeni tikondane wina ndi mnzake, pakuti chikondi chimachokera kwa Mulungu. Aliyense amene ali ndi chikondi ndi mwana wa Mulungu ndipo amadziwa Mulungu. 8 Aliyense amene alibe chikondi sadziwa Mulungu, chifukwa Mulungu ndiye chikondi. 9 Mmene Mulungu anaonetsera chikondi chake pakati pathu ndi umu: Iye anatumiza Mwana wake mmodzi yekha ku dziko lapansi kuti mwa Iyeyo tikhale ndi moyo. 10 Chikondi ndi ichi: osati kuti ife ndife amene tinamukonda Mulungu, koma kuti Iyeyo ndiye amene anatikonda ndipo anatumiza Mwana wake kuti akhale nsembe yopepesera machimo athu. 11 Anzanga okondedwa, popeza Mulungu anatikonda chotere, ifenso tiyenera kukondana wina ndi mnzake. 12 Palibe amene anaonapo Mulungu, koma tikakondana wina ndi mnzake, ndiye kuti Mulungu amakhala mwa ife ndipo chikondi chake chafika pachimake penipeni mwa ife.
13 Ife tikudziwa kuti timakhala mwa Iye ndipo Iyeyo amakhala mwa ife chifukwa anatipatsa Mzimu wake. 14 Ndipo taona ndipo tikuchitira umboni, kuti Atate anatuma Mwana wake kuti akhale Mpulumutsi wa dziko lapansi. 15 Ngati aliyense avomereza kuti Yesu ndi Mwana wa Mulungu, Mulungu amakhala mwa iye ndipo iyeyo amakhala mwa Mulungu. 16 Tikudziwa ndipo timadalira chikondi chimene Mulungu ali nacho pa ife.
Mulungu ndiye chikondi. Aliyense amene amakhala moyo wachikondi, ali mwa Mulungu ndipo Mulungu amakhala mwa iye. 17 Chikondi chafika pachimake penipeni pakati pathu, kotero kuti pa tsiku lachiweruzo tidzakhala olimba mtima chifukwa mʼdziko lapansi moyo wathu uli ngati wa Khristu. 18 Mulibe mantha mʼchikondi. Koma chikondi ndi changwiro chimachotsa mantha, chifukwa mantha amabwera chifukwa choopa chilango. Munthu amene ali ndi mantha, chikondi chake sichangwiro.
19 Ife timakonda Mulungu chifukwa ndiye anayamba kutikonda. 20 Ngati wina anena kuti, “Ine ndimakonda Mulungu,” koma namadana ndi mʼbale wake ndi wabodza ameneyo. Pakuti aliyense amene sakonda mʼbale wake, amene akumuona, sangathenso kukonda Mulungu amene sanamuone. 21 Ndipo Iye anatipatsa lamulo lakuti: Aliyense amene amakonda Mulungu ayenera kukondanso mʼbale wake.
Chinese Contemporary Bible Copyright © 1979, 2005, 2007, 2011 by Biblica® Used by permission. All rights reserved worldwide.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.