約伯記 14
Chinese Contemporary Bible (Traditional)
14 「人為婦人所生,
一生短暫,充滿患難。
2 他如花盛開,轉眼凋謝;
如影消逝,無法久留。
3 你還察看這樣的世人嗎?
還要把我召來受審嗎?
4 誰能使污穢產生潔淨呢?
沒有人能。
5 人的年日已被限定,
你掌管他的歲月,
設定他無法逾越的界限。
6 求你轉身,別去管他,
好讓他如雇工度完他的日子。
7 樹木若被砍下,還有希望,
它仍可重新萌芽,
嫩枝生長不息。
8 雖然樹根在土裡衰老,
樹幹在地裡死去,
9 但一有水氣,
它就會像新栽的樹一樣發芽長枝。
10 但人一死,就失去力量;
人一嚥氣,就不知去向。
11 湖水會枯竭,
江河會乾涸,
12 人躺下便不再起來,
到諸天不復存在,
他仍不會醒來,
不會從長眠中被喚醒。
13 但願你把我藏在陰間,
把我藏起來直到你息怒,
定下眷顧我的日期。
14 人若死了,還能復生嗎?
我要在勞苦的歲月中等待,
直到我得釋放的日子來臨。
15 那時你呼喚,我便回應,
你必惦念你親手所造之物。
16 那時你必鑒察我的腳步,
但不會追究我的罪惡。
17 我的過犯會被封在袋中,
你會遮蓋我的罪愆。
18 「高山崩塌,
磐石挪移;
19 流水磨損石頭,
急流沖走泥土;
你也這樣粉碎人的希望。
20 你永遠擊敗他,使他消逝;
你改變他的容顏,讓他離世。
21 他的後人得尊榮,他無從知曉;
他們遭貶抑,他也無法察覺。
22 他只能感受自身的痛苦,
為自己哀哭。」
Yobu 14
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
14 “Munthu wobadwa mwa amayi
amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
2 Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota;
amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
3 Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa?
Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
4 Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa?
Palibe ndi mmodzi yemwe!
5 Masiku a munthu ndi odziwikiratu;
munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake
ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
6 Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule
kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
7 “Mtengo uli nacho chiyembekezo:
ngati wadulidwa, udzaphukiranso
ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
8 Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka
ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
9 koma pamene chinyontho chafika udzaphukira
ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
10 Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda,
amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
11 Monga madzi amaphwera mʼnyanja
kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
12 momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso;
mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka
kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
13 “Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda
ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita!
Achikhala munandiyikira nthawi,
kuti pambuyo pake mundikumbukirenso.
14 Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo?
Masiku anga onse a moyo wovutikawu
ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
15 Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani;
inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
16 Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga
koma simudzalondola tchimo langa.
17 Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba;
inu mudzaphimba tchimo langa.
18 “Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka
ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
19 monganso madzi oyenda amaperesera miyala
ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka,
momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
20 Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu;
Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
21 Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo;
akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
22 Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake
ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.