帖撒罗尼迦前书 1
Revised Chinese Union Version (Simplified Script) Shen Edition
问候
1 保罗、西拉、提摩太写信给帖撒罗尼迦在父 神和主耶稣基督里的教会。愿恩惠、平安[a]归给你们!
帖撒罗尼迦信徒的信心和榜样
2 我们为你们众人常常感谢 神,祷告的时候提到你们, 3 在我们的父 神面前,不住地记念你们因信心所做的工作,因爱心所受的劳苦,因盼望我们主耶稣基督所存的坚忍。 4 神所爱的弟兄啊,我知道你们是蒙拣选的; 5 因为我们的福音传到你们那里,不仅在言语,也在能力,也在圣灵和充足的确信。你们知道,我们在你们那里,为你们的缘故是怎样为人。 6 你们成为效法我们,更效法主的人,因圣灵所激发的喜乐,在大患难中领受了真道, 7 从此你们作了马其顿和亚该亚所有信主的人的榜样。 8 因为主的道已经从你们那里传播出去,你们向 神的信心不只在马其顿和亚该亚,就是在各处也都传开了,所以不用我们说什么话。 9 因为他们自己已经传讲我们是怎样进到你们那里,你们是怎样离弃偶像,归向 神来服侍那又真又活的 神, 10 等候他儿子从天降临,就是 神使他从死人中复活的那位救我们脱离将来愤怒的耶稣。
Footnotes
- 1.1 “平安”或译“和平”。
1 Atesalonika 1
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
1 Paulo, Silivano ndi Timoteyo.
Tikulembera mpingo wa ku Tesalonika, umene uli mwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu.
Chisomo ndi mtendere kwa inu.
Kuyamikira Chikhulupiriro cha Atesalonika
2 Ife timayamika Mulungu nthawi zonse chifukwa cha inu. Timakutchulani mʼmapemphero athu. 3 Nthawi zonse timakumbukira ntchito yanu yachikhulupiriro, yachikondi ndi kupirira kwanu kwa chiyembekezo mwa Ambuye athu Yesu Khristu, pamaso pa Mulungu wathu ndi Atate.
4 Abale okondedwa ndi Mulungu, tikudziwa kuti Mulungu anakusankhani, 5 chifukwa uthenga wathu wabwino sunafike kwa inu ndi mawu okha, koma ndi mphamvu za Mzimu Woyera ndi chitsimikizo chachikulu. Mukudziwa mmene tinkakhalira pakati panu kuti tikuthandizeni. 6 Inu mwakhala otitsatira athu ndi a Ambuye; ngakhale kuti panali masautso akulu, munalandira uthenga mwachimwemwe chochokera kwa Mzimu Woyera. 7 Ndipo potero munakhala chitsanzo kwa abale onse a ku Makedoniya ndi Akaya. 8 Kuchokera kwa inu, uthenga wa Ambuye unamveka ku Makedoniya ndi ku Akaya ndipo mbiri ya chikhulupiriro chanu mwa Mulungu yamveka ponseponse. Choncho sikofunikanso kuti tinene kanthu, 9 pakuti iwo amafotokoza za momwe munatilandirira. Iwo amatiwuza za momwe munatembenukira kwa Mulungu kusiya mafano ndi kutumikira Mulungu wamoyo ndi woona. 10 Ndipo mukudikira Mwana wake kuchokera kumwamba, Yesu, amene Mulungu anamuukitsa kwa akufa. Iyeyo amatipulumutsa ku mkwiyo umene ukubwera.
和合本修訂版經文 © 2006, 2010, 2017 香港聖經公會。蒙允許使用。 Scripture Text of Revised Chinese Union Version © 2006, 2010, 2017 Hong Kong Bible Society. www.hkbs.org.hk/en/ Used by permission.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.