Add parallel Print Page Options

所以,我們應當離開基督道理的基礎,竭力進到成熟的地步;不必再立根基,就如懊悔致死的行為、信靠 神、 各樣洗禮、按手禮、死人復活,以及永遠的審判等的教導。  神若准許,我們就這樣做。 4-6 論到那些已經蒙了光照、嘗過天恩的滋味、又於聖靈有份、並嘗過 神的話的美味,和來世權能的人,若再離棄真道,就不可能使他們重新懊悔了;因為他們親自把 神的兒子重釘十字架,公然羞辱他。 就如一塊田地吸收過屢次下的雨水,生長蔬菜,合乎耕種的人用,就從 神得福。 這塊田地若長荊棘和蒺藜,必被廢棄,近於詛咒,結局就是焚燒。

親愛的,雖然這樣說,我們仍深信你們有更好的情況,更接近救恩。 10 因為 神並非不公義,竟忘記你們的工作和你們為他的名所顯的愛心,就是你們過去和現在伺候聖徒的愛心。 11 我們盼望你們各人都顯出同樣的熱忱,一直到底,好達成所確信的指望。 12 這樣你們才不會懶惰,卻成為效法那些藉着信和忍耐承受應許的人。

 神確切的應許

13 當初 神應許亞伯拉罕的時候,因為沒有比自己更大的可以指着起誓,就指着自己起誓, 14 說:「我必多多賜福給你;我必使你大大增多。」 15 這樣,亞伯拉罕因恆心等待而得了所應許的。 16 人都是指着比自己大的起誓,並且以起誓作保證,了結各樣的爭論。 17 照樣, 神願意為那承受應許的人更有力地顯明他的旨意不可更改,他以起誓作保證。 18 藉這兩件不可更改的事—在這些事上, 神絕不會說謊—我們這些逃往避難所的人能得到強有力的鼓勵,去抓住那擺在我們前頭的指望。 19 我們有這指望,如同靈魂的錨,又堅固又牢靠,進入幔子後面的至聖所。 20 為我們作先鋒的耶穌,既照着麥基洗德的體系成了永遠的大祭司,已經進入了。

Tsono tiyeni tisangoyima pa maphunziro oyambirira enieni a Khristu koma tipitirire kuti mukule msinkhu. Tisaphunzitsenso zinthu zomwe zili ngati maziko, monga za kutembenuka mtima kusiya ntchito zosapindulitsa pa moyo wosatha, za kukhulupirira Mulungu, za maubatizo, za kusanjika manja, za kuuka kwa akufa ndi za chiweruzo chotsiriza. Ndipo Mulungu akalola, tidzaterodi.

Nʼkosatheka kuwabwezanso anthu amene nthawi ina anawunikiridwa. Iwowa analawapo mphatso yochokera kumwamba, nʼkulandira nawo Mzimu Woyera. Analawa kukoma kwa mawu a Mulungu ndi mphamvu za nthawi ikubwera. Popeza anabwerera mʼmbuyo, nʼkosatheka kuti atembenukenso mtima chifukwa akupachikanso Mwana wa Mulungu ndi kumunyozetsa poyera.

Nthaka yolandira mvula kawirikawiri nʼkubala mbewu zopindulitsa oyilima, Mulungu amayidalitsa. Koma nthaka yobereka minga ndi nthula ndi yopanda phindu ndipo ili pafupi kutembereredwa. Matsiriziro ake idzatenthedwa mʼmoto.

Okondedwa anga, ngakhale tikuyankhula zimenezi, ife tikudziwa kuti muli nazo zinthu zabwino zomwe zimabwera pamodzi ndi chipulumutso. 10 Mulungu ndi wolungama, sangayiwale ntchito zanu ndi chikondi chanu chimene munamuonetsa pothandiza anthu ake monga mmene mukuchitirabe tsopano. 11 Ife tikufuna kuti aliyense wa inu aonetse changu chomwechi mpaka kumapeto, kuti zichitikedi zomwe mukuyembekezera. 12 Ife sitikufuna kuti inu mukhale aulesi, koma mutsatire anthu amene, pokhulupirira ndi kupirira, akulandira zimene zinalonjezedwa.

Kukhazikika kwa Malonjezo a Mulungu

13 Pamene Mulungu ankamulonjeza Abrahamu, popeza panalibe wamkulu womuposa, amene akanamutchula ndikulumbira mwa Iye, analumbira mwa Iye yekha kuti, 14 “Ine ndidzakudalitsa ndithu, ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zambiri.” 15 Ndipo Abrahamu atayembekezera mofatsa, analandira zimene anamulonjezazo.

16 Anthu amalumbira mʼdzina la wina amene akuwaposa, ndipo lumbiro lotere limatsimikizira zomwe zayankhulidwa ndi kuthetsa mikangano yonse. 17 Momwemonso Mulungu pofuna kutsimikizira anthu amene adzalandire lonjezo, kuti Iye sangasinthe maganizo, anatsimikiza lonjezo lakelo ndi lumbiro. 18 Mulungu anachita zinthu ziwiri, lonjezo ndi lumbiro, zimene sizingathe kusintha ndipo Mulungu sangathe kunama. Choncho Mulungu akutilimbikitsa mtima ife amene tinathawira kwa Iye kuti tichigwiritsitse chiyembekezo chimene tinalandira. 19 Chiyembekezo chimenechi tili nacho ngati nangula wa moyo wathu. Nʼchokhazikika ndi chosagwedezeka ndipo chimalowa mʼkatikati mwa malo opatulika, kuseri kwa chinsalu chotchinga. 20 Yesu anatitsogolera kupita kumeneko, nalowako mʼmalo mwathu. Iye anasanduka Mkulu wa ansembe onse wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.