Add parallel Print Page Options

所以,亲爱的,我们有了这些应许,就应该洁净自己,除去身体和心灵上的一切污秽,存着敬畏 神的心,达到成圣的地步。

哥林多人悔改,保罗得喜乐

你们的心要容得下我们。我们没有亏负过谁,没有损害过谁,也没有占过谁的便宜。 我这样说,不是要定你们的罪,因为我从前说过,你们常在我们心里,甚至可以同生共死。 我对你们大有信心,因你们而感到十分光荣;我心里满有安慰,在我们的一切患难中,格外充满喜乐。

我们从前到了马其顿的时候,身体一点安宁也没有,反而处处遭受患难,外面有争战,里面有恐惧。 但那安慰灰心的人的 神,借着提多来到,安慰了我们; 不但借着他来,也借着他从你们所得的安慰,安慰了我们。他把你们的渴望、你们的哀恸和你们对我的热诚,都告诉了我们,因此我就更加欢喜了。 虽然我在那封信上使你们忧伤,但我现在并不后悔;其实我曾经有点后悔,因为知道那封信使你们忧伤,虽然只是暂时的。 现在我快乐,不是因为你们忧伤,而是因为你们的忧伤带来了悔改。你们依照 神的意思忧伤,凡事就不会因我们受到亏损。 10 因为依照 神的意思而有的忧伤,可以生出没有懊悔的悔改,以致得救;世俗的忧伤却会招致死亡。 11 看哪,你们依照 神的意思忧伤,在你们中间就产生了怎样的热情、申诉、愤慨、战兢、渴望、热诚、正义;你们在各方面都表明了自己在那事上是清白的。 12 因此,从前我虽然写过信给你们,却不是为了那亏负人的,也不是为了那受害的,而是在 神面前把你们对我们的热情,向你们显现出来。 13 因此,我们得了安慰。

在这安慰之外,我们因提多的喜乐就更加欢喜,因为他的心从你们众人那里得到畅快。 14 我若对他夸奖过你们甚么,也不觉得惭愧。我们对你们所说的是真话,照样,我们在提多面前夸奖你们的也是真的。 15 并且他想起你们众人的服从,怎样恐惧战兢地接待他,他怀念你们的心就更加热切了。 16 现在我很欢喜,因为在一切事上我对你们都有信心。

Abwenzi okondedwa, popeza tili ndi malonjezo amenewa, tiyeni tidziyeretse, kusiyana nazo zilizonse zimene zikhoza kudetsa thupi ndi mzimu, ndipo tiyesetse kukhala oyera mtima poopa Mulungu.

Chimwemwe cha Paulo

Mutipatse malo mʼmitima mwanu. Ife sitinalakwire munthu aliyense, kapena kuyipitsa munthu aliyense, kapena kumuchenjerera munthu aliyense. Sindikunena izi kuti mupezeke olakwa. Ndinanena kale kuti ife timakuganizirani kwambiri kotero kuti tili pamodzi, ngakhale tikhale moyo kapena timwalire. Ndimakukhulupirirani kwambiri ndipo ndimakunyadirani kwambiri. Ndikulimbikitsidwa kwambiri; mʼmasautso athu onse, chimwemwe changa chilibe malire.

Pakuti titafika ku Makedoniya, sitinapume nʼkomwe, koma tinavutitsidwa mbali zonse. Kunja kunali mikangano, ndipo mʼmitima mwathu munali mantha. Koma Mulungu, amene amatonthoza mtima wopsinjika, anatitonthoza mtima ndi kufika kwa Tito, sikubwera kwake kokhako, komanso mawu achilimbikitso amene analandira kuchokera kwa inu. Iye anatiwuza kuti mukufuna kundiona, zachisoni chanu chachikulu, ndi kudzipereka kwanu kwa ine, motero chimwemwe changa chinachuluka kuposa kale.

Ngakhale kalata yanga ija inakupwetekani mtima, sindikudandaula kuti ndinalemberanji. Ngakhale zinandikhudza, ndikudziwa kuti kalata yanga inakupwetekani, koma kwa kanthawi kochepa. Koma tsopano ndine wokondwa, osati chifukwa chakuti kalatayo inakupwetekani, koma chifukwa chakuti chisoni chanu chinakuthandizani kutembenuka mtima. Pakuti munamva chisoni monga mmene Mulungu amafunira, choncho simunapwetekedwe mwanjira iliyonse. 10 Chisoni chimene Mulungu amafuna chimabweretsa kutembenuka mtima komwe kumabweretsa chipulumutso, ndipo sichikhumudwitsa. Koma chisoni cha dziko lapansi chimabweretsa imfa. 11 Taonani zimene chisoni chimene Mulungu amafuna chatulutsa mwa inu. Chatulutsa khama lalikulu, chakuthandizani kuti mudzikonze nokha, chakukwiyitsani kwambiri, komanso chakupatsani mantha aakulu. Chakuchititsani kuti mufune kundiona ine, mwakhudzidwa kwambiri ndipo mukufuna kuonetsetsa kuti chilungamo chachitikadi. Pa nkhani yonseyi, mwaonetsadi kuti ndinu osalakwa. 12 Choncho ngakhale ndinakulemberani kalata ija, sindinayilembe ndi chifukwa cha amene analakwayo kapena wolakwiridwa, koma ndinayilemba kuti inuyo muone kudzipereka kwanu kwa ife pamaso a Mulungu. 13 Zimenezi zatilimbikitsa kwambiri.

Kuwonjezera pa zotilimbikitsazo, tinakondwa kwambiri poona chisangalalo cha Tito, chifukwa nonsenu munamuthandiza kukhazikitsa mtima wake pansi. 14 Ndinamuwuza kuti ndimakunyadirani, ndipo simunandichititse manyazi. Koma monga zonse zimene tinakuwuzani zinali zoona, tsono zomwe ndinawuza Tito zokunyadirani zinali zoona. 15 Ndipo chikondi chake pa inu nʼchachikulu kwambiri akakumbukira kuti nonse munali omvera, munamulandira ndi mantha ndi kunjenjemera. 16 Ndine wokondwa kuti ndingathe kukukhulupirirani pa zonse.