Add parallel Print Page Options

捐钱给圣徒的事

16 关于捐献给圣徒的事,从前我怎样吩咐加拉太的众教会,你们也要照着去行。 每逢七日的第一日,你们各人要按着自己的收入抽一些出来留着,免得我来的时候才现凑。 我来到之后,你们选中了甚么人,我就派他们带着书信,把你们的捐款送到耶路撒冷去。 如果我也应该去,他们就可以和我一同去。

保罗的行程

我现在正要路过马其顿。过了马其顿,我就会到你们那里去。 我也许会和你们同住一些时候,甚至和你们一同过冬;这样,我无论要到哪里去,你们都可以给我送行。 我不愿意只是顺路见见你们,主若许可,我盼望和你们同住一个时期。 不过我要在以弗所住到五旬节, 因为这里有又宽大又有果效的门为我开了,同时反对的人也很多。

10 如果提摩太来了,你们务要使他在你们那里不会惧怕,因为他像我一样是作主的工作的。 11 所以,谁也不要小看他。你们要送他平平安安地前行,使他到我这里来,因为我正在等着他和弟兄们一同来。 12 至于亚波罗弟兄,我曾再三劝他要和弟兄们一同到你们那里去;但他不愿意现在就去,机会到了,他是会去的。

劝勉和问安

13 你们要警醒,要在信仰上站立得稳,要作大丈夫,要刚强。 14 你们所作的一切,都要凭爱心去作。

15 弟兄们,你们知道司提反一家人是亚该亚初结的果子,他们专心地服事圣徒。 16 我劝你们要顺服这样的人,和所有与他们一同工作一同劳苦的人。 17 司提反、福徒拿都和亚该古都来了,所以我很快乐,因为他们补上了你们的不足, 18 使我和你们的心都得着畅快。这样的人你们要敬重他们。

19 亚西亚的众教会都问候你们。亚居拉和百基拉,以及他们家里的教会在主里再三问候你们。 20 所有的弟兄都问候你们。你们要用圣洁的亲吻彼此问安。

21 我保罗亲笔问候你们。 22 如果有人不爱主,他就该受咒诅。主啊,愿你来! 23 愿主耶稣基督的恩惠与你们同在。 24 我的爱在基督耶稣里也与你们同在。(有古卷加“阿们”。)

Ndalama Zothandizira Akhristu a ku Yerusalemu

16 Tsopano za zopereka zothandiza anthu a Ambuye a ku Yerusalemu. Muchite zomwe ndinawuza mipingo ya ku Galatiya kuti ichite. Pa tsiku loyamba la sabata lililonse, aliyense wa inu azipatula ndalama molingana ndi zomwe wapezera. Asunge, kuti ndikabwera pasadzakhalenso msonkhamsonkha. Pamenepo, ndikadzafika, ndidzawapatsa makalata a umboni anthu amene mudzawasankhe ndi kuwatuma kuti akapereka mphatso zanu ku Yerusalemu. Ngati kutaoneka kuti nʼkoyenera kuti ndipite nawo, adzapita nane limodzi.

Paulo Afotokoza za Maulendo ake ndi Zina

Ndidzafika kwanuko nditadutsa ku Makedoniya pakuti ndikuyembekezera kudzera ku Makedoniyako. Mwina ndidzakhala nanu kanthawi kochepa kapenanso nyengo yonse yozizira, kuti mudzandithandize kupitiriza ulendo wanga kulikonse kumene ndingapite. Sindikufuna kuti ndikuoneni tsopano mongodutsa chabe, koma ndikuyembekezera kudzakhala nanu kwa kanthawi, ngati Ambuye alola. Koma ndikhala ndili ku Efeso mpaka nthawi ya Pentekosite, pakuti mwayi waukulu wapezeka woti nʼkugwira ntchito yaphindu, koma pali ambiri amene akutsutsana nane.

10 Ngati Timoteyo afike kwanuko, onetsetsani kuti pasakhale zina zomuchititsa mantha pamene ali pakati panu, pakuti iye akugwira ntchito ya Ambuye monga ine. 11 Wina aliyense asamunyoze. Muthandizeni kupitiriza ulendo wake mwamtendere kubwereranso kuli ine. Ndikumuyembekeza pamodzi ndi abale ena.

12 Tsono kunena za mʼbale wathu, Apolo, ndinamuwumiriza kwambiri kuti abwere kwa inu abale, ndipo iye sanafune kupita tsopano. Koma akadzapeza mpata wabwino adzabwera.

13 Khalani tcheru; khazikikani mʼchikhulupiriro chanu; limbani mtima; khalani amphamvu. 14 Chitani zonse mwachikondi.

15 Mukudziwa kuti a mʼbanja la Stefano ndiye anali oyamba kutembenuka mtima ku Akaya, ndipo akhala akudzipereka kutumikira oyera mtima. Choncho ndikukudandaulirani, inu abale, 16 kuti muziwamvera anthu oterewa, ndiponso aliyense wogwira nawo ntchitoyi modzipereka. 17 Ndikondwera kuti Stefano, Fortunato ndi Akayiko afika, chifukwa akhala akundithandiza pakuti inu simuli nane. 18 Pakuti anatsitsimutsa mzimu wanga ndi wanu womwe. Anthu a mtundu oterewa ngofunika kuwalemekeza.

Mawu Otsiriza

19 Mpingo wa mʼchigawo cha ku Asiya ukupereka moni. Akula ndi Prisila akuperekanso moni wachisangalalo, mwa Ambuye, ndiponso mpingo umene umakumana mʼnyumba mwawo ukupereka moni. 20 Abale onse kuno akupereka moni wawo. Patsanani moni wachikondi chenicheni.

21 Ineyo Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa mawu awa akuti moni.

22 Ngati wina sakonda Ambuye akhale wotembereredwa. Maranatha! (Ambuye athu bwerani)!

23 Chisomo cha Ambuye Yesu chikhale ndi inu.

24 Chikondi changa chikhale ndi nonsenu mwa Khristu Yesu.