Add parallel Print Page Options

36 Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:

“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani
    kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali;
    ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
Ndithudi mawu anga si abodza;
    wanzeru zangwiro ali ndi inu.

“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu;
    Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo
    koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama;
    amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu
    ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo,
    ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
Iye amawafotokozera zomwe anachita,
    kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake
    ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira,
    adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere,
    adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 Koma ngati samvera,
    adzaphedwa ndi lupanga
    ndipo adzafa osadziwa kanthu.

13 “Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo;
    akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Amafa akanali achinyamata,
    pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo;
    Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.

16 “Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso,
    kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani,
    kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu;
    chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma;
    musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Kodi chuma chanu
    kapena mphamvu zanu zonse
    zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Musalakalake kuti usiku ubwere,
    pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo,
    chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.

22 “Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu.
    Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite,
    kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Kumbukirani kutamanda ntchito zake
    zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 Anthu onse amaziona ntchitozo;
    anthuwo amaziona ali kutali.
26 Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe!
    Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.

27 “Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo,
    timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 mitambo imagwetsa mvulayo
    ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera,
    momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse,
    zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu
    ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani,
    ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho;
    ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.

36 Elihu continued:

“Bear with me a little longer and I will show you
    that there is more to be said in God’s behalf.
I get my knowledge from afar;(A)
    I will ascribe justice to my Maker.(B)
Be assured that my words are not false;(C)
    one who has perfect knowledge(D) is with you.(E)

“God is mighty,(F) but despises no one;(G)
    he is mighty, and firm in his purpose.(H)
He does not keep the wicked alive(I)
    but gives the afflicted their rights.(J)
He does not take his eyes off the righteous;(K)
    he enthrones them with kings(L)
    and exalts them forever.(M)
But if people are bound in chains,(N)
    held fast by cords of affliction,(O)
he tells them what they have done—
    that they have sinned arrogantly.(P)
10 He makes them listen(Q) to correction(R)
    and commands them to repent of their evil.(S)
11 If they obey and serve him,(T)
    they will spend the rest of their days in prosperity(U)
    and their years in contentment.(V)
12 But if they do not listen,
    they will perish by the sword[a](W)
    and die without knowledge.(X)

13 “The godless in heart(Y) harbor resentment;(Z)
    even when he fetters them, they do not cry for help.(AA)
14 They die in their youth,(AB)
    among male prostitutes of the shrines.(AC)
15 But those who suffer(AD) he delivers in their suffering;(AE)
    he speaks(AF) to them in their affliction.(AG)

16 “He is wooing(AH) you from the jaws of distress
    to a spacious place(AI) free from restriction,(AJ)
    to the comfort of your table(AK) laden with choice food.(AL)
17 But now you are laden with the judgment due the wicked;(AM)
    judgment and justice have taken hold of you.(AN)
18 Be careful that no one entices you by riches;
    do not let a large bribe(AO) turn you aside.(AP)
19 Would your wealth(AQ) or even all your mighty efforts
    sustain you so you would not be in distress?
20 Do not long for the night,(AR)
    to drag people away from their homes.[b]
21 Beware of turning to evil,(AS)
    which you seem to prefer to affliction.(AT)

22 “God is exalted in his power.(AU)
    Who is a teacher like him?(AV)
23 Who has prescribed his ways(AW) for him,(AX)
    or said to him, ‘You have done wrong’?(AY)
24 Remember to extol his work,(AZ)
    which people have praised in song.(BA)
25 All humanity has seen it;(BB)
    mortals gaze on it from afar.
26 How great is God—beyond our understanding!(BC)
    The number of his years is past finding out.(BD)

27 “He draws up the drops of water,(BE)
    which distill as rain to the streams[c];(BF)
28 the clouds pour down their moisture
    and abundant showers(BG) fall on mankind.(BH)
29 Who can understand how he spreads out the clouds,
    how he thunders(BI) from his pavilion?(BJ)
30 See how he scatters his lightning(BK) about him,
    bathing the depths of the sea.(BL)
31 This is the way he governs[d] the nations(BM)
    and provides food(BN) in abundance.(BO)
32 He fills his hands with lightning
    and commands it to strike its mark.(BP)
33 His thunder announces the coming storm;(BQ)
    even the cattle make known its approach.[e](BR)

Footnotes

  1. Job 36:12 Or will cross the river
  2. Job 36:20 The meaning of the Hebrew for verses 18-20 is uncertain.
  3. Job 36:27 Or distill from the mist as rain
  4. Job 36:31 Or nourishes
  5. Job 36:33 Or announces his coming— / the One zealous against evil