Add parallel Print Page Options

Yehova Agonjetsa Anthu a Mitundu Ina

63 Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu,
    atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira?
Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola,
    akuyenda mwa mphamvu zake?

“Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo
    ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”

Nanga bwanji zovala zanu zili psuu,
    ngati za munthu wofinya mphesa?

“Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa,
    palibe ndi mmodzi yemwe anali nane.
Ndinawapondereza ndili wokwiya
    ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali;
magazi awo anadothera pa zovala zanga,
    ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.
Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga;
    ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.
Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza.
    Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza;
choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga,
    ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.
Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya;
    ndipo ndinawasakaza
    ndipo ndinathira magazi awo pansi.”

Matamando ndi Pemphero

Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova,
    ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa.
    Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira.
Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake
    Yehova wachitira nyumba ya Israeli
    zinthu zabwino zambiri.
Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga,
    ana anga amene sadzandinyenga Ine.”
    Choncho anawapulumutsa.
Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse,
    ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa.
Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa,
    anawanyamula ndikuwatenga
    kuyambira kale lomwe.
10 Komabe iwo anawukira
    ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera.
Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo
    ndipo Iye mwini anamenyana nawo.

11 Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana,
    masiku a Mose mtumiki wake;
ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja,
    pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo?
Ali kuti Iye amene anayika
    Mzimu Woyera pakati pawo?
12 Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa
    ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose?
Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona,
    kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,
13 amene anawayendetsa pa nyanja yozama?
Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu,
    iwo sanapunthwe;
14 Mzimu Woyera unawapumulitsa
    ngati mmene ngʼombe zimapumulira.
Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu
    kuti dzina lanu lilemekezeke.”

15 Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka,
    wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife.
Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti?
    Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.
16 Koma Inu ndinu Atate athu,
    ngakhale Abrahamu satidziwa
    kapena Israeli kutivomereza ife;
Inu Yehova, ndinu Atate athu,
    kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.
17 Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu?
    Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso?
Bwererani chifukwa cha atumiki anu;
    mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.
18 Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa,
    adani athu anasakaza malo anu opatulika.
19 Ife tili ngati anthu amene
    simunawalamulirepo
    ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.

God’s Day of Vengeance and Redemption

63 Who is this coming from Edom,(A)
    from Bozrah,(B) with his garments stained crimson?(C)
Who is this, robed in splendor,
    striding forward in the greatness of his strength?(D)

“It is I, proclaiming victory,
    mighty to save.”(E)

Why are your garments red,
    like those of one treading the winepress?(F)

“I have trodden the winepress(G) alone;
    from the nations no one was with me.
I trampled(H) them in my anger
    and trod them down in my wrath;(I)
their blood spattered my garments,(J)
    and I stained all my clothing.
It was for me the day of vengeance;(K)
    the year for me to redeem had come.
I looked, but there was no one(L) to help,
    I was appalled that no one gave support;
so my own arm(M) achieved salvation for me,
    and my own wrath sustained me.(N)
I trampled(O) the nations in my anger;
    in my wrath I made them drunk(P)
    and poured their blood(Q) on the ground.”

Praise and Prayer

I will tell of the kindnesses(R) of the Lord,
    the deeds for which he is to be praised,
    according to all the Lord has done for us—
yes, the many good things(S)
    he has done for Israel,
    according to his compassion(T) and many kindnesses.
He said, “Surely they are my people,(U)
    children who will be true to me”;
    and so he became their Savior.(V)
In all their distress he too was distressed,
    and the angel(W) of his presence(X) saved them.[a]
In his love and mercy he redeemed(Y) them;
    he lifted them up and carried(Z) them
    all the days of old.(AA)
10 Yet they rebelled(AB)
    and grieved his Holy Spirit.(AC)
So he turned and became their enemy(AD)
    and he himself fought(AE) against them.

11 Then his people recalled[b] the days of old,
    the days of Moses and his people—
where is he who brought them through the sea,(AF)
    with the shepherd of his flock?(AG)
Where is he who set
    his Holy Spirit(AH) among them,
12 who sent his glorious arm(AI) of power
    to be at Moses’ right hand,
who divided the waters(AJ) before them,
    to gain for himself everlasting renown,(AK)
13 who led(AL) them through the depths?(AM)
Like a horse in open country,
    they did not stumble;(AN)
14 like cattle that go down to the plain,
    they were given rest(AO) by the Spirit of the Lord.
This is how you guided your people
    to make for yourself a glorious name.

15 Look down from heaven(AP) and see,
    from your lofty throne,(AQ) holy and glorious.
Where are your zeal(AR) and your might?
    Your tenderness and compassion(AS) are withheld(AT) from us.
16 But you are our Father,(AU)
    though Abraham does not know us
    or Israel acknowledge(AV) us;
you, Lord, are our Father,
    our Redeemer(AW) from of old is your name.
17 Why, Lord, do you make us wander(AX) from your ways
    and harden our hearts(AY) so we do not revere(AZ) you?
Return(BA) for the sake of your servants,
    the tribes that are your inheritance.(BB)
18 For a little while(BC) your people possessed your holy place,
    but now our enemies have trampled(BD) down your sanctuary.(BE)
19 We are yours from of old;
    but you have not ruled over them,
    they have not been called[c] by your name.(BF)

Footnotes

  1. Isaiah 63:9 Or Savior in their distress. / It was no envoy or angel / but his own presence that saved them
  2. Isaiah 63:11 Or But may he recall
  3. Isaiah 63:19 Or We are like those you have never ruled, / like those never called