Yeremiya 30
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kubwezeretsedwa kwa Israeli
30 Yehova anawuza Yeremiya kuti, 2 “Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Lemba mʼbuku mawu onse amene ndakuwuza. 3 Nthawi ikubwera pamene ndidzachotse anthu anga, Israeli ndi Yuda kuchokera ku ukapolo ndi kuwabwezera dziko limene ndinapatsa makolo awo,’ akutero Yehova.”
4 Nawa mawu amene Yehova anayankhula ndi anthu a ku Israeli ndi Yuda: 5 “Yehova akuti:
“Ndamva kulira chifukwa cha nkhawa,
ndamva kulira kwa mantha popeza palibe mtendere.
6 Tsono khalani pansi ndi kudzifunsa kuti:
Kodi munthu wamwamuna angathe kubereka mwana?
Nanga nʼchifukwa chiyani ndikuona munthu aliyense wamwamuna
atagwira manja ake pa mimba pake ngati mayi pa nthawi yake yochira?
Chifukwa chiyani nkhope iliyonse ili yakugwa?
7 Mayo ine! Tsiku limeneli ndi lalikulu kwambiri!
Sipadzakhala lina lofanana nalo.
Idzakhala nthawi ya masautso kwa Yakobo,
koma adzapulumuka ku masautsowo.”
8 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pa tsiku limenelo,
ndidzathyola goli la ukapolo mʼkhosi mwawo
ndipo ndidzadula zingwe zowamanga;
Aisraeli sadzakhalanso akapolo a alendo.
9 Mʼmalo mwake, adzatumikira Yehova Mulungu wawo
ndiponso Davide mfumu yawo,
amene ndidzawasankhira.
10 “ ‘Tsono usachite mantha, iwe mtumiki wanga Yakobo;
usade nkhawa, iwe Israeli,’
akutero Yehova.
‘Ndithu ndidzakupulumutsa kuchokera ku dziko lakutali,
zidzukulu zako kuchokera ku dziko la ukapolo wawo.
Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala modekha pa mtendere,
ndipo palibe amene adzamuchititsa mantha.
11 Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani,’
akutero Yehova.
‘Ngakhale ndidzawononga kotheratu mitundu yonse ya anthu
kumene ndinakubalalitsirani,
koma inu sindidzakuwonongani kotheratu.
Sindidzakulekani kuti mukhale osalangidwa.
Koma ndidzakulangani mwachilungamo.’ ”
12 Yehova akuti,
“Chilonda chanu nʼchosachizika,
bala lanu ndi lonyeka.
13 Palibe amene angathe kukutetezani pa mlandu wanu,
palibe chiyembekezo choti inu nʼkuchira,
palibe mankhwala ochiritsa inu.
14 Abwenzi anu onse akuyiwalani;
sasamalanso za inu.
Ndakukanthani ngati mmene mdani akanachitira.
Ndipo ndakulangani mwa nkhanza,
chifukwa machimo anu ndi ambiri,
ndipo kulakwa kwanu ndi kwakukulu.
15 Chifukwa chiyani mukulira nacho chilonda chanu?
Bala lanu silingapole ayi.
Ine ndakuchitani zimenezi chifukwa machimo anu ndi ambiri
ndipo kulakwa kwanu nʼkwakukulu.
16 “Tsono onse amene anakuwonongani, nawonso adzawonongedwa;
adani anu onse adzapita ku ukapolo.
Iwo amene anafunkha zinthu zanu, zinthu zawo zidzafunkhidwanso;
onse amene anakusakazani nawonso adzasakazidwa.
17 Ndidzachiza matenda anu
ndi kupoletsa zilonda zanu,
akutero Yehova,
‘chifukwa mukutchedwa anthu otayika.
Amati, ndi anthu a ku Ziyoni awa amene alibe wowasamala.’ ”
18 Yehova akuti,
“Ndidzabwera nalo banja la Yakobo ku dziko lawo
ndipo ndidzachitira chifundo malo ake okhalamo;
mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso pa bwinja pake,
nyumba yaufumu idzamangidwanso pa malo pake penipeni.
19 Anthuwo adzayimba nyimbo zoyamika Yehova
ndipo kudzamveka phokoso lachisangalalo.
Ndidzawachulukitsa,
ndipo chiwerengero chawo sichidzatsika;
ndidzawapatsa ulemerero,
ndipo sadzanyozedwanso.
20 Ana awo adzakhalanso monga mmene analili kale,
ndipo gulu lawo ndidzalikhazikitsa pamaso panga;
ndidzalanga onse owazunza.
21 Mtsogoleri wawo adzakhala mmodzi mwa iwo.
Wodzawalamulira adzachokera pakati pawo.
Choncho ndidzawakokera kufupi ndi Ine ndipo iye adzandiyandikira.
Ndani angalimbe mtima payekha kuyandikana nane
popanda kuyitanidwa?”
akutero Yehova.
22 “Choncho inu mudzakhala anthu anga,
ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.”
23 Taonani ukali wa Yehova wowomba
ngati mphepo ya mkuntho.
Mphepo ya namondwe
ikuwomba pa mitu ya anthu oyipa.
24 Mkwiyo woopsa wa Yehova sudzachoka
mpaka atakwaniritsa zolinga
za mu mtima mwake.
Mudzamvetsa zimenezi
masiku akubwerawo.
Jeremiah 30
International Standard Version
A Message of Consolation
30 This message came from the Lord to Jeremiah: 2 “This is what the Lord God of Israel says: ‘Write all the words that I’ve spoken to you in a book. 3 Indeed, the time[a] will come,’ declares the Lord, ‘when I’ll restore the security of my people Israel and Judah,’ says the Lord. ‘I’ll bring them back to the land that I gave to their ancestors, and they’ll possess it.’”
4 These are the words that the Lord spoke about Israel and Judah:
5 “Indeed, this is what the Lord says:
‘We have heard a sound of terror
and of fear, and there is no peace.
6 Ask about this and think about it—
Can a man give birth to a child?
Why then do I see every strong man
with his hands on his thighs
like a woman giving birth,
and all their faces have turned pale?
7 Oh how terrible! That time[b] will be worse
than any like it.
It will be a time of trouble for Jacob,
but he will be rescued from it.
8 On that day,’ declares the Lord
of the Heavenly Armies,
‘I’ll break the yoke[c] from your neck
and will tear off your restraints.[d]
Foreigners will no longer make you[e] serve them.[f]
9 Rather, they will serve the Lord their God
and David their king,
whom I will raise up for them.
10 ‘My servant Jacob, don’t be afraid,’ declares the Lord,
‘and Israel, don’t be dismayed.
For I’ll deliver you from a distant place
and your descendants from the land of their captivity.
Jacob will return. He will be undisturbed and secure,
and no one will cause him to fear.
11 For I’ll be with you to save you,’
declares the Lord.
‘For I’ll put an end to all the nations
where I scattered you;
but I won’t make an end of you.
I’ll discipline you justly,
but I certainly won’t leave you unpunished.’
The Healing of Zion’s Wounds
12 “For this is what the Lord says:
‘Your injury won’t heal;
your wound is severe.
13 There is no one to plead your cause.
There is no medicine for your sore;[g]
no healing for you.
14 All your lovers have forgotten you;
they don’t seek you.
Indeed, I’ve struck you down
with the blow of an enemy,
with the punishment of a cruel foe[h]
because your wickedness is great,
and your sins are numerous.
15 Why do you cry out because of your injury?
Your wound won’t heal.
Because your wickedness is severe,
and your sins are numerous,
I’ve done all these things to you.
16 In addition, all who devour you will be devoured,
and all your oppressors—all of them—
will go into captivity.
Those who plunder you will become plunder,
and all who spoil you will become spoil.
17 Indeed, I’ll bring you healing,
and I’ll heal you of your wounds,’
declares the Lord,
‘because they have called you an outcast
and have said,[i] “It is Zion, no one cares for her!”’”[j]
Jacob’s Restoration
18 “This is what the Lord says:
‘I’m going to restore the fortunes of the tents of Jacob
and have compassion on his dwellings.
A city will be rebuilt on its ruins
and a palace[k] will sit on its rightful place.
19 Thanksgiving and the sounds of laughter
will come out of them.
I’ll cause them to increase in numbers and not decrease.
I’ll honor them and not make them insignificant.
20 Their[l] children will be as they were before,
and their congregation will be established before me.
I’ll punish all who oppress them.
21 Their leader will be one of their own,[m]
and their ruler will come from among them.
I’ll bring him near, and he will approach me,
for who would otherwise dare to approach me?’
declares the Lord.
22 ‘You will be my people,
and I’ll be your God.’”
The Coming Judgment
23 Look, the storm of the Lord!
His[n] wrath has gone forth, a twisting storm.
It will swirl around the head of the wicked.
24 The fierce anger of the Lord won’t turn back
until he has accomplished and established the plan of his heart.
In the days to come, you will understand this.
Footnotes
- Jeremiah 30:3 Lit. days
- Jeremiah 30:7 Lit. day
- Jeremiah 30:8 Lit. his yoke
- Jeremiah 30:8 Or cords
- Jeremiah 30:8 Lit. him (i.e. Jacob)
- Jeremiah 30:8 I.e. enslave you
- Jeremiah 30:13 Lit. for a sore
- Jeremiah 30:14 Lit. cruel one
- Jeremiah 30:17 The Heb. lacks and have said
- Jeremiah 30:17 Or seeks her
- Jeremiah 30:18 Or fortress
- Jeremiah 30:20 Lit. his children and so through v. 21
- Jeremiah 30:21 Lit. of them
- Jeremiah 30:23 The Heb. lacks His
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Copyright © 1995-2014 by ISV Foundation. ALL RIGHTS RESERVED INTERNATIONALLY. Used by permission of Davidson Press, LLC.
