Add parallel Print Page Options

Naomi ndi Rute

Mu nthawi imene oweruza ankalamulira Israeli, munali njala mʼdziko, ndipo munthu wina wa ku Betelehemu mʼdziko la Yuda anapita pamodzi ndi mkazi wake ndi ana ake aamuna awiri, kukakhala ku Mowabu kwa nthawi yochepa. Dzina la munthuyo linali Elimeleki, dzina la mkazi wake linali Naomi, ndipo mayina a ana awo aamuna anali Maaloni ndi Kiliyoni. Iwo anali Aefurati ochokera ku Betelehemu ku Yuda. Ndipo anapita kukakhala ku Mowabu.

Kenaka Elimeleki, mwamuna wake wa Naomi anamwalira ndipo Naomiyo anatsala ndi ana ake aamuna awiri aja.

Iwo anakwatira akazi a Chimowabu; wina dzina lake Oripa ndi wina Rute. Atakhala kumeneko pafupifupi zaka khumi, Maloni ndi Kiliyoni anamwaliranso kotero kuti Naomi anatsala yekha wopanda ana ake awiri aja ndi mwamuna wake.

Naomi ndi apongozi ake awiri aja ananyamuka kubwerera kwawo kuchokera ku Mowabu popeza anali atamva ali ku Mowabuko kuti Yehova anakomera mtima anthu ake ndi kuwapatsa chakudya.

Naomi pamodzi ndi apongozi ake awiri aja anachoka kumene ankakhala ndi kuyamba ulendo obwerera kwawo ku Yuda.

Kenaka Naomi anati kwa apongozi ake awiri aja, “Bwererani, aliyense kwa amayi ake. Yehova akukomereni mtima, monga munachita ndi malemu aja ndi ine ndemwe.

“Yehova akuthandizeni kuti aliyense wa inu apeze pokhala pabwino komanso mwamuna.” Kenaka anawapsompsona koma awiriwo analira mokweza.

10 Ndipo anati kwa Naomi, “Ife tipita nawo kwa anthu akwanu.”

11 Koma Naomi anati, “Bwererani kwanu ana anga. Chifukwa chiyani mukufuna kupita ndi ine? Kodi ine ndingaberekenso ana ena kuti akhale amuna anu? 12 Bwererani kwanu ana anga muzipita kwanu. Ine ndakalamba kwambiri kotero kuti sindingakwatiwenso. Ngakhale ndikananena kuti ndili nacho chikhulupiriro, ngakhale ndikanakhala ndi mwamuna usiku uno, ndipo nʼkubala ana aamuna, 13 kodi inu mukanadikira kuti akule? Kodi mukanakhalabe osakwatiwa kudikira iwowo? Ayi ana anga. Zimenezi zikundiwawa kwambiri kuposa inu, chifukwa ndi ineyo amene Yehova wafuna kuti ndizunzike.”

14 Atamva zimenezi analiranso kwambiri, ndipo Oripa anapsompsona apongozi ake nawatsanzika, koma Rute anakakamirabe.

15 Naomi anati “Taona, mʼbale wako wabwerera kwawo kwa anthu ake ndi kwa milungu yake. Bwerera nawenso umulondole mʼbale wako.”

16 Koma Rute anayankha kuti, “Musandikakamize kuti ndikusiyeni kapena kuti ndibwerere osakutsatani. Kumene inu mupite ine ndipita komweko, ndipo kumene mukakhale inenso ndikakhala komweko. Abale anu adzakhala abale anga ndipo Mulungu wanu adzakhala Mulungu wanga. 17 Kumene mukafere inenso ndidzafera komweko ndipo komweko ndikayikidwa mʼmanda. Yehova andichite choyipa chingakule motani, ngati china chingatirekanitse ife kupatula imfa.”

18 Naomi atazindikira kuti Rute watsimikiza kupita naye, analeka kumukakamiza.

19 Choncho amayi awiriwo anapitiriza ulendo wawo mpaka anakafika ku Betelehemu. Pamene ankafika mu Betelehemu, anthu onse a mʼmudzimo anatekeseka chifukwa cha iwowo ndipo amayi ambiri ankanena kuti, “Kodi uyu nʼkukhala Naomi?”

20 Iye anawawuza kuti, “Musanditchenso Naomi. Muzinditchula ine kuti Mara, chifukwa Wamphamvuzonse wandizunza kwambiri. 21 Ine ndinapita wolemera, koma Yehova wabwera nane wopanda kanthu. Nanga munditchulirenji Naomi pamene Yehova wandisautsa. Wamphamvuzonse uja wandigwetsera mavuto owawa.”

22 Naomi anabwerera kuchoka ku dziko la Mowabu pamodzi ndi Rute mpongozi wake. Ndipo anafika ku Betelehemu nthawi yoyamba kukolola barele.

Ruth and Naomi Come to Bethlehem

During the days of the judges,[a] a famine occurred in the land. So a man left Bethlehem in Judah to stay awhile[b] in the territory[c] of Moab—he, his wife, and his two sons. The man’s name was Elimelek, his wife’s name was Naomi, and the names of his two sons were Mahlon and Kilion. They were from the clan of Ephrath from Bethlehem in Judah. They entered the territory of Moab and remained there.

But Elimelek, Naomi’s husband, died, so she was left with her two sons. They then married Moabite wives. The name of the first was Orpah, and the name of the second was Ruth. They lived there for about ten years. But Naomi’s sons, Mahlon and Kilion, also died. So the woman was left without her two children and without her husband.

Then Naomi set out with her daughters-in-law to return from the territory of Moab, because while she was in the territory of Moab, she had heard that the Lord had graciously visited[d] his people by providing them with food. So she left the place where she had been, and her two daughters-in-law left with her. They set out on the road to return to the land of Judah.

But Naomi said to her two daughters-in-law, “Go back. Both of you return to your mother’s house. May the Lord show you kindness[e] as you have shown kindness to the dead and to me. May the Lord grant that each of you finds security[f] in the house of a husband.” Then she kissed them, and they wept loudly.

10 But they said to her, “No, we will return with you to your people.”

11 Then Naomi said, “Turn back, my daughters. Why should you go with me? Am I going to give birth to any more sons[g] who could become your husbands? 12 Turn back, my daughters. Go! For I am too old to be married to another husband. Suppose I say, ‘I have hope, and I will be married to another husband tonight, and I will even give birth to sons.’ 13 Would you wait for them until they grow up? On the basis of that hope would you give up the chance to marry another husband? No, my daughters. It is much more bitter for me than for you, because the hand of the Lord has reached out against me.”

14 They once again wept loudly. Then Orpah kissed her mother-in-law, but Ruth would not let her go.

15 Naomi said, “Look, your sister-in-law has returned to her people and to her gods. Go back! Follow your sister-in-law.”

16 But Ruth said, “Do not urge me to abandon you or to turn back from following you. Because wherever you go, I will go, and wherever you make your home, I will make my home. Your people will be my people, and your God will be my God. 17 Wherever you die, I will die, and there I will be buried. May the Lord punish me severely and double it[h] if anything but death[i] separates me from you.”

18 When Naomi saw that Ruth was determined to go with her, she stopped urging her.

19 Then the two of them traveled until they arrived at Bethlehem. When they entered Bethlehem, the whole town became excited over them. The women said, “Is this Naomi?”

20 But she said to them, “Do not call me Naomi. Call me Mara,[j] because the Almighty has made me very bitter. 21 I went away full, but the Lord brought me back empty. Why should you call me Naomi? For the Lord has testified against me,[k] and the Almighty has treated me badly.”

22 So Naomi returned with Ruth the Moabite, her daughter-in-law, who came back with her from the territory of Moab. When they entered Bethlehem, it was the beginning of the barley harvest.[l]

Footnotes

  1. Ruth 1:1 The judges served not only as judicial officials but also as military deliverers.
  2. Ruth 1:1 Or live as an alien
  3. Ruth 1:1 Literally the field. In Ruth the word field is a key term, which is used in various senses throughout the book.
  4. Ruth 1:6 When God visits people, he comes to bring blessing or correction. Here, obviously, it is blessing.
  5. Ruth 1:8 Or faithfulness
  6. Ruth 1:9 Or rest
  7. Ruth 1:11 Literally do I still have sons in my womb
  8. Ruth 1:17 Literally may the Lord do all this to me and even more. This is an oath with the specific curse left unstated.
  9. Ruth 1:17 Or even death
  10. Ruth 1:20 Naomi means pleasant; Mara means bitter.
  11. Ruth 1:21 Or has afflicted me
  12. Ruth 1:22 March or April