Masalimo 10:1-11
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
10 Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali?
Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?
2 Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka,
amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.
3 Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake;
amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.
4 Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu;
mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.
5 Zinthu zake zimamuyendera bwino;
iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali;
amanyogodola adani ake onse.
6 Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze.
Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”
7 Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza;
zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.
8 Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi,
kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa,
amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.
9 Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba.
Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu;
amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.
10 Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka;
amakhala pansi pa mphamvu zake.
11 Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala,
wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.