Masalimo 37:5-9
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
5 Pereka njira yako kwa Yehova;
dalira Iye ndipo Iyeyo adzachita izi:
6 Iye adzachititsa chilungamo chako kuwala ngati mʼbandakucha,
chiweruzo chako ngati dzuwa la masana.
7 Khala chete pamaso pa Yehova ndipo umudikire mofatsa;
usavutike pamene anthu apambana mʼnjira zawo,
pamene iwo achita zinthu zawo zoyipa.
8 Pewa kupsa mtima ndipo tembenuka kuchoka ku ukali,
usavutike chifukwa zimenezi zimatsogolera ku zoyipa.
9 Pakuti anthu oyipa adzachotsedwa,
koma iwo amene amayembekeza mwa Yehova adzalandira dziko.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.