Nahumu 2:11-13
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti,
malo amene mikango inkadyetserako ana ake,
kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako,
ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake
ndiponso kuphera nyama mkango waukazi,
kudzaza phanga lake ndi zimene wapha
ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.
13 Yehova Wamphamvuzonse akuti,
“Ine ndikutsutsana nawe.
Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo,
ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono;
sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi.
Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.