Add parallel Print Page Options

11 Kodi tsopano dzenje la mikango lili kuti,
    malo amene mikango inkadyetserako ana ake,
kumene mkango waumuna ndi waukazi unkapitako,
    ndipo ana a mkango sankaopa kanthu kalikonse?
12 Mkango waumuna unkapha nyama yokwanira ana ake
    ndiponso kuphera nyama mkango waukazi,
kudzaza phanga lake ndi zimene wapha
    ndiponso dzenje lake ndi nyama imene waphayo.

13 Yehova Wamphamvuzonse akuti,
    “Ine ndikutsutsana nawe.
Ndidzatentha magaleta ako mpaka utsi tolotolo,
    ndipo lupanga lidzapha mikango yako yayingʼono;
sindidzakusiyira chilichonse choti udye pa dziko lapansi.
Mawu a amithenga anu sadzamvekanso.”

Read full chapter